< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Quando sederis ut comedas cum principe, diligenter attende quæ apposita sunt ante faciem tuam:
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
et statue cultrum in gutture tuo, si tamen habes in potestate animam tuam,
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
ne desideres de cibis eius, in quo est panis mendacii.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Noli laborare ut diteris: sed prudentiæ tuæ ponde modum.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Ne erigas oculos tuos ad opes, quas non potes habere: quia facient sibi pennas quasi aquilæ, et volabunt in cælum.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Ne comedas cum homine invido, et ne desideres cibos eius:
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
quoniam in similitudinem arioli, et coniectoris, æstimat quod ignorat. Comede et bibe, dicet tibi: et mens eius non est tecum.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Cibos, quos comederas, evomes: et perdes pulchros sermones tuos.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
In auribus insipientium ne loquaris: qui despicient doctrinam eloquii tui.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Ne attingas parvulorum terminos: et agrum pupillorum ne introeas:
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
Propinquus enim illorum fortis est: et ipse iudicabit contra te causam illorum.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Ingrediatur ad doctrinam cor tuum: et aures tuæ ad verba scientiæ.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Noli subtrahere a puero disciplinam: si enim percusseris eum virga, non morietur.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Tu virga percuties eum: et animam eius de inferno liberabis. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Fili mi, si sapiens fuerit animus tuus, gaudebit tecum cor meum:
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
et exultabunt renes mei, cum locuta fuerint rectum labia tua.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Non æmuletur cor tuum peccatores: sed in timore Domini esto tota die:
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
quia habebis spem in novissimo, et præstolatio tua non auferetur.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Audi fili mi, et esto sapiens: et dirige in via animum tuum.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Noli esse in conviviis potatorum, nec in comessationibus eorum, qui carnes ad vescendum conferunt:
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
quia vacantes potibus, et dantes symbola consumentur, et vestietur pannis dormitatio.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Audi patrem tuum, qui genuit te: et ne contemnas cum senuerit mater tua.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Veritatem eme, et noli vendere sapientiam, et doctrinam, et intelligentiam.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Exultat gaudio pater iusti: qui sapientem genuit, lætabitur in eo.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Gaudeat pater tuus, et mater tua, et exultet quæ genuit te.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Præbe fili mi cor tuum mihi: et oculi tui vias meas custodiant.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
Fovea enim profunda est meretrix: et puteus angustus, aliena.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Insidiatur in via quasi latro, et quos incautos viderit, interficiet.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Cui væ? cuius patri væ? cui rixæ? cui foveæ? cui sine causa vulnera? cui suffusio oculorum?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Nonne his, qui commorantur in vino, et student calicibus epotandis?
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Ne intuearis vinum quando flavescit, cum splenduerit in vitro color eius: ingreditur blande,
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
sed in novissimo mordebit ut coluber, et sicut regulus venena diffundet.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Oculi tui videbunt extraneas, et cor tuum loquetur perversa.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
Et eris sicut dormiens in medio mari, et quasi sopitus gubernator, amisso clavo:
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
et dices: Verberaverunt me, sed non dolui: traxerunt me, et ego non sensi: quando evigilabo, et rursus vina reperiam?

< Miyambo 23 >