< Miyambo 19 >

1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Better is the poor who walks in his integrity than he who is perverse in his lips and is a fool.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
It isn't good to have zeal without knowledge; nor being hasty with one's feet and missing the way.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
The foolishness of man subverts his way; his heart rages against the LORD.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Wealth adds many friends, but the poor is separated from his friend.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
A false witness shall not be unpunished. He who pours out lies shall not go free.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Many will seek the favor of a ruler, and everyone is a friend to a man who gives gifts.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
All the relatives of the poor shun him: how much more do his friends avoid him. He pursues them with pleas, but they are gone.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
He who gets wisdom loves his own soul. He who keeps understanding shall find good.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
A false witness shall not be unpunished. He who utters lies shall perish.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Delicate living is not appropriate for a fool, much less for a servant to have rule over princes.
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
The discretion of a man makes him slow to anger. It is his glory to overlook an offense.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
The king's wrath is like the roaring of a lion, but his favor is like dew on the grass.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
A foolish son is the calamity of his father. A wife's quarrels are a continual dripping.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
House and riches are an inheritance from fathers, but a prudent wife is from the LORD.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Slothfulness casts into a deep sleep. The idle soul shall suffer hunger.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
He who keeps the commandment keeps his soul, but he who is contemptuous in his ways shall die.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
He who has pity on the poor lends to the LORD; he will reward him.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Discipline your son, for there is hope; do not be a willing party to his death.
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
A hot-tempered man must pay the penalty, for if you rescue him, you must do it again.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Listen to counsel and receive instruction, that you may be wise in your latter end.
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
There are many plans in a man's heart, but the LORD's counsel will prevail.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
That which makes a man to be desired is his kindness. A poor man is better than a liar.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
The fear of the LORD leads to life, then contentment; he rests and will not be touched by trouble.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
The sluggard buries his hand in the dish; he will not so much as bring it to his mouth again.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Flog a scoffer, and the simple will learn prudence; rebuke one who has understanding, and he will gain knowledge.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
He who robs his father and drives away his mother, is a son who causes shame and brings reproach.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
If you stop listening to instruction, my son, you will stray from the words of knowledge.
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
A corrupt witness mocks justice, and the mouth of the wicked gulps down iniquity.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Penalties are prepared for scoffers, and beatings for the backs of fools.

< Miyambo 19 >