< Miyambo 16 >

1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
Hominis est animam praeparare: et Domini gubernare linguam.
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
Omnes viae hominis patent oculis eius: spirituum ponderator est Dominus.
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
Revela Domino opera tua, et dirigentur cogitationes tuae.
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
Universa propter semetipsum operatus est Dominus: impium quoque ad diem malum.
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
Abominatio Domini est omnis arrogans: etiamsi manus ad manum fuerit, non est innocens. Initium viae bonae, facere iustitiam: accepta est autem apud Deum magis, quam immolare hostias.
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
Misericordia et veritate redimitur iniquitas: et in timore Domini declinatur a malo.
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
Cum placuerint Domino viae hominis, inimicos quoque eius convertet ad pacem.
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
Melius est parum cum iustitia, quam multi fructus cum iniquitate.
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
Cor hominis disponit viam suam: sed Domini est dirigere gressus eius.
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
Divinatio in labiis regis, in iudicio non errabit os eius.
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
Pondus et statera iudicia Domini sunt: et opera eius omnes lapides sacculi.
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
Abominabiles regi qui agunt impie: quoniam iustitia firmatur solium.
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
Voluntas regum labia iusta: qui recta loquitur, diligetur:
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
Indignatio regis, nuncii mortis: et vir sapiens placabit eam.
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
In hilaritate vultus regis, vita: et clementia eius quasi imber serotinus.
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
Posside sapientiam, quia auro melior est: et acquire prudentiam, quia pretiosior est argento.
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
Semita iustorum declinat mala: custos animae suae servat viam suam.
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
Contritionem praecedit superbia: et ante ruinam exaltatur spiritus.
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
Melius est humiliari cum mitibus, quam dividere spolia cum superbis.
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
Eruditus in verbo reperiet bona: et qui sperat in Domino, beatus est.
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
Qui sapiens est corde, appellabitur prudens: et qui dulcis eloquio, maiora reperiet.
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
Fons vitae eruditio possidentis: doctrina stultorum fatuitas.
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
Cor sapientis erudiet os eius: et labiis eius addet gratiam.
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
Favus mellis, composita verba: dulcedo animae, sanitas ossium.
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
Est via quae videtur homini recta: et novissima eius ducunt ad mortem.
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
Anima laborantis laborat sibi, quia compulit eum os suum:
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
Vir impius fodit malum, et in labiis eius ignis ardescit.
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
Homo perversus suscitat lites: et verbosus separat principes.
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
Vir iniquus lactat amicum suum: et ducit eum per viam non bonam.
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
Qui attonitis oculis cogitat prava, mordens labia sua perficit malum.
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
Corona dignitatis senectus, quae in viis iustitiae reperietur.
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
Melior est patiens viro forti: et qui dominatur animo suo, expugnatore urbium.
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
Sortes mittuntur in sinum, sed a Domino temperantur.

< Miyambo 16 >