< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Every wise woman builds her house: but the foolish plucks it down with her hands.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
He that walks in his uprightness fears the LORD: but he that is perverse in his ways despises him.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
In the mouth of the foolish is a rod of pride: but the lips of the wise shall preserve them.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Where no oxen are, the crib is clean: but much increase is by the strength of the ox.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
A faithful witness will not lie: but a false witness will utter lies.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
A scorner seeks wisdom, and finds it not: but knowledge is easy to him that understands.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Go from the presence of a foolish man, when you perceive not in him the lips of knowledge.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
The wisdom of the prudent is to understand his way: but the folly of fools is deceit.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Fools make a mock at sin: but among the righteous there is favor.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
The heart knows his own bitterness; and a stranger does not intermeddle with his joy.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
The house of the wicked shall be overthrown: but the tabernacle of the upright shall flourish.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
There is a way which seems right to a man, but the end thereof are the ways of death.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Even in laughter the heart is sorrowful; and the end of that mirth is heaviness.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
The backslider in heart shall be filled with his own ways: and a good man shall be satisfied from himself.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
The simple believes every word: but the prudent man looks well to his going.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
A wise man fears, and departs from evil: but the fool rages, and is confident.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
He that is soon angry deals foolishly: and a man of wicked devices is hated.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
The simple inherit folly: but the prudent are crowned with knowledge.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
The evil bow before the good; and the wicked at the gates of the righteous.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
The poor is hated even of his own neighbor: but the rich has many friends.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
He that despises his neighbor sins: but he that has mercy on the poor, happy is he.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Do they not err that devise evil? but mercy and truth shall be to them that devise good.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
In all labor there is profit: but the talk of the lips tends only to penury.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
The crown of the wise is their riches: but the foolishness of fools is folly.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
A true witness delivers souls: but a deceitful witness speaks lies.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
In the fear of the LORD is strong confidence: and his children shall have a place of refuge.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
The fear of the LORD is a fountain of life, to depart from the snares of death.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
In the multitude of people is the king’s honor: but in the want of people is the destruction of the prince.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
He that is slow to wrath is of great understanding: but he that is hasty of spirit exalts folly.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
A sound heart is the life of the flesh: but envy the rottenness of the bones.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
He that oppresses the poor reproaches his Maker: but he that honors him has mercy on the poor.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
The wicked is driven away in his wickedness: but the righteous has hope in his death.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Wisdom rests in the heart of him that has understanding: but that which is in the middle of fools is made known.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Righteousness exalts a nation: but sin is a reproach to any people.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
The king’s favor is toward a wise servant: but his wrath is against him that causes shame.

< Miyambo 14 >