< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Ženska mudrost sagradi kuću, a ludost je rukama razgrađuje.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Tko živi s poštenjem, boji se Jahve, a tko ide stranputicom, prezire ga.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
U luđakovim je ustima šiba za oholost njegovu, a mudre štite vlastite usne.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Gdje nema volova, prazne su jasle, a obilna je žetva od snage bikove.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Istinit svjedok ne laže, a krivi svjedok širi laž.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Podsmjevač traži mudrost i ne nalazi je, a razumni lako dolazi do znanja.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Idi od čovjeka bezumna jer nećeš upoznati usne što zbore znanje.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Mudrost je pametna čovjeka u tom što pazi na svoj put, a bezumnička ludost prijevara je.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Luđacima je grijeh šala, a milost je Božja s poštenima.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Srce poznaje svoj jad, i veselje njegovo ne može dijeliti nitko drugi.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
Dom opakih propast će, a šator će pravednika procvasti.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Neki se put učini čovjeku prav, a na koncu vodi k smrti.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
I u smijehu srce osjeća bol, a poslije veselja dolazi tuga.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Otpadnik se siti svojim prestupcima, a dobar čovjek svojim radom.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Glupan vjeruje svakoj riječi, a pametan pazi na korak svoj.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Mudar se boji i oda zla se uklanja, a bezuman se raspaljuje i bez straha je.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
Nagao čovjek čini ludosti, a razborit ih podnosi.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Glupaci baštine ludost, a mudre ovjenčava znanje.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Zli padaju ničice pred dobrima i opaki pred vratima pravednikovim.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
I svom prijatelju mrzak je siromah, a bogataš ima mnogo ljubitelja.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Griješi tko prezire bližnjega svoga, a blago onomu tko je milostiv ubogima.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Koji snuju zlo, ne hode li stranputicom, a zar nisu dobrota i vjernost s onima koji snuju dobro?
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
U svakom trudu ima probitka, a pusto brbljanje samo je na siromaštvo.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
Mudrima je vijenac bogatstvo njihovo, a bezumnima kruna - njihova ludost.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Istinit svjedok izbavlja duše, a tko laži širi, taj je varalica.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
U strahu je Gospodnjem veliko pouzdanje i njegovim je sinovima utočište.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Strah Gospodnji izvor je života: on izbavlja od zamke smrti.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
Mnoštvo je naroda ponos kralju, a bez puka knez propada.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Tko se teško srdi, velike je razboritosti, a nabusit duhom pokazuje ludost.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Mirno je srce život tijelu, a ljubomor je gnjilež u kostima.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Tko tlači siromaha huli na stvoritelja, a časti ga tko je milostiv ubogomu.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Opaki propada zbog vlastite pakosti, a pravednik i u samoj smrti nalazi utočište.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
U razumnu srcu mudrost počiva, a što je u bezumnome, to se i pokaže.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Pravednost uzvisuje narod, a grijeh je sramota pucima.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
Kralju je mio razborit sluga, a na sramotna se srdi.

< Miyambo 14 >