< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
智慧妇人建立家室; 愚妄妇人亲手拆毁。
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
行动正直的,敬畏耶和华; 行事乖僻的,却藐视他。
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
愚妄人口中骄傲,如杖责打己身; 智慧人的嘴必保守自己。
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
家里无牛,槽头干净; 土产加多乃凭牛力。
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
诚实见证人不说谎话; 假见证人吐出谎言。
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
亵慢人寻智慧,却寻不着; 聪明人易得知识。
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
到愚昧人面前, 不见他嘴中有知识。
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
通达人的智慧在乎明白己道; 愚昧人的愚妄乃是诡诈。
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
愚妄人犯罪,以为戏耍; 正直人互相喜悦。
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
心中的苦楚,自己知道; 心里的喜乐,外人无干。
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
奸恶人的房屋必倾倒; 正直人的帐棚必兴盛。
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
有一条路,人以为正, 至终成为死亡之路。
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
人在喜笑中,心也忧愁; 快乐至极就生愁苦。
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
心中背道的,必满得自己的结果; 善人必从自己的行为得以知足。
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
愚蒙人是话都信; 通达人步步谨慎。
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
智慧人惧怕,就远离恶事; 愚妄人却狂傲自恃。
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
轻易发怒的,行事愚妄; 设立诡计的,被人恨恶。
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
愚蒙人得愚昧为产业; 通达人得知识为冠冕。
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
坏人俯伏在善人面前; 恶人俯伏在义人门口。
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
贫穷人连邻舍也恨他; 富足人朋友最多。
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
藐视邻舍的,这人有罪; 怜悯贫穷的,这人有福。
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
谋恶的,岂非走入迷途吗? 谋善的,必得慈爱和诚实。
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
诸般勤劳都有益处; 嘴上多言乃致穷乏。
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
智慧人的财为自己的冠冕; 愚妄人的愚昧终是愚昧。
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
作真见证的,救人性命; 吐出谎言的,施行诡诈。
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
敬畏耶和华的,大有倚靠; 他的儿女也有避难所。
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
敬畏耶和华就是生命的泉源, 可以使人离开死亡的网罗。
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
帝王荣耀在乎民多; 君王衰败在乎民少。
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
不轻易发怒的,大有聪明; 性情暴躁的,大显愚妄。
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
心中安静是肉体的生命; 嫉妒是骨中的朽烂。
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
欺压贫寒的,是辱没造他的主; 怜悯穷乏的,乃是尊敬主。
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
恶人在所行的恶上必被推倒; 义人临死,有所投靠。
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
智慧存在聪明人心中; 愚昧人心里所存的,显而易见。
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
公义使邦国高举; 罪恶是人民的羞辱。
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
智慧的臣子蒙王恩惠; 贻羞的仆人遭其震怒。

< Miyambo 14 >