< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Die Sprüche Salomos, des Davidssohnes und Herrschers über Israel,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
sind dazu da, daß man Charakter und Weisheit würdige und kluge Worte wohl verstehe
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
und Zucht und Anstand lerne, was recht und rechtlich, ehrlich sei,
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
daß Bildung Unerfahrene empfangen und daß die Jugend Lebenskunst erlerne.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Vernimmt ein Weiser sie, so kann er seine Rede fesselnder gestalten; ein kluger Mann kann sich die richtige Belehrung sichern.
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Er kann das Gleichnis und den Sinnspruch faßlicher gestalten, wie auch der Weisen Worte, ihre dunklen Reden. -
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Die Furcht des Herrn ist Anfang der Erkenntnis, Weisheit, Bildung. Nur Toren sind's, die sie verachten.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Der väterlichen Zucht, mein Sohn, gehorche! Der Mutter Mahnung achte nicht gering!
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Sie zieren wie ein Kranz dein Haupt und deinen Hals wie Kettenschmuck.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mein Sohn, wenn dich Verbrecher locken, folg ihnen nicht!
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Wenn sie dir sagen: "Halt's mit uns! Wir haben einen Anschlag gegen einen Menschen vor; wir wollen ungefährdet im Versteck Arglosen auflauern.
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Wir wollen selbst am Leben bleiben und sie verschlingen gleich der Unterwelt, mit Haut und Haar als solche, die zur Grube fahren. (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Und wir gewinnen alles mögliche kostbare Gut und füllen unsere Häuser mit dem Raub.
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Du darfst auch mit uns teilen; wir alle haben einen Beutel."
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Mein Sohn, geh nicht auf einem Weg mit ihnen! Halt deinen Fuß von ihren Pfaden fern!
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Denn ihre Füße laufen dem Verderben zu und eilen blutigem Tod entgegen.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Vergeblich wird man Netze spannen vor den Blicken der beschwingten Vögel;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
sie aber lauern auf ihr eigen Blut und stellen sich selbst nach dem Leben.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
So ist das Schicksal eines jeden, der auf unrechten Gewinn ausgeht. Er bringt ihn um sein Leben.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Auf Straßen ruft die Weisheit; auf Plätzen ruft sie laut.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Hoch oben auf den Mauern predigt sie, an Stadttoren; vor aller Welt nimmt sie das Wort:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
"Wie lange liebt ihr Toren noch Betörung, gefällt den Dünkelhaften Spott und hassen Toren Einsicht?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Ihr kommt auf meine Mahnrede zurück. Fürwahr, ich sag euch unumwunden, was ich auf dem Herzen habe. Ich tue meine Warnungen euch kund.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Ich rief; ihr aber wolltet nicht; ich winkte euch, und niemand gab drauf acht.
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Ihr schluget meinen Ratschlag in den Wind und mochtet meine Rüge nicht.
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
So lache ich bei eurem Unglück nur und spotte, wenn euch Angst befällt,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
wenn wie ein Ungewitter euer Schrecken kommt, einherfährt gleich dem Sturmwind euer Unglück und Not und Drangsal euch befällt.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Dann rufen sie mich an; ich gebe keine Antwort. Sie suchen, aber finden mich nicht mehr.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Erkenntnis haben sie gehaßt und nach der Furcht des Herren nicht gefragt,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
sie wollten nichts von meinem Rate wissen, und meine Rüge haben sie verschmäht.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
So mögen sie denn ihres Handels Frucht genießen, sich sättigen mit dem, was sie sich selbst bereitet!
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Ihr Fehlgehn bringt sie, diese Dummen, um; Sorglosigkeit vernichtet diese Toren.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Wer aber mir gehorcht, der kann in Ruhe wohnen und unbesorgt vor Unheilsschrecken sein."

< Miyambo 1 >