< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
The proverbs of Solomon the son of David, king of Israel;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
To know wisdom and instruction; to perceive the words of understanding;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
To receive the instruction of wisdom, justice, and judgment, and equity;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
To give prudence to the simple, to the young man knowledge and discretion.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
A wise man will hear, and will increase learning; and a man of understanding shall attain to wise counsels:
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
To understand a proverb, and the interpretation; the words of the wise, and their dark sayings.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
The fear of the LORD is the beginning of knowledge: but fools despise wisdom and instruction.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
My son, hear the instruction of thy father, and forsake not the law of thy mother:
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
For they shall be an ornament of grace to thy head, and chains about thy neck.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
My son, if sinners entice thee, consent thou not.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
If they say, Come with us, let us lay wait for blood, let us lurk secretly for the innocent without cause:
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Let us swallow them up alive as the grave; and whole, as those that go down into the pit: (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
We shall find all precious substance, we shall fill our houses with spoil:
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Cast in thy lot among us; let us all have one purse:
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
My son, walk not thou in the way with them; keep thy foot from their path:
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
For their feet run to evil, and make haste to shed blood.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Surely in vain the net is spread in the sight of any bird.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
And they lay wait for their own blood; they lurk secretly for their own lives.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
So are the ways of every one that is greedy of gain; who taketh away the life of its owners.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Wisdom crieth outside; she uttereth her voice in the streets:
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
She crieth in the chief place of concourse, in the openings of the gates: in the city she uttereth her words, saying,
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
How long, ye simple ones, will ye love simplicity? and the scorners delight in their scorning, and fools hate knowledge?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Turn ye at my reproof: behold, I will pour out my spirit to you, I will make known to you my words.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Because I have called, and ye refused; I have stretched out my hand, and no man regarded;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
But ye have set at nought all my counsel, and rejected my reproof:
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
I also will laugh at your calamity; I will mock when your fear cometh;
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
When your fear cometh as desolation, and your destruction cometh as a whirlwind; when distress and anguish cometh upon you.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Then shall they call upon me, but I will not answer; they shall seek me early, but they shall not find me:
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Because they hated knowledge, and did not choose the fear of the LORD:
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
They rejected my counsel: they despised all my reproof.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Therefore shall they eat of the fruit of their own way, and be filled with their own devices.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
For the turning away of the simple shall slay them, and the prosperity of fools shall destroy them.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
But whoever hearkeneth to me shall dwell in safety, and shall be quiet from fear of evil.

< Miyambo 1 >