< Afilipi 3 >

1 Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.
I øvrigt, mine Brødre glæder eder i Herren! At skrive det samme til eder er ikke til Besvær for mig, men er betryggende for eder.
2 Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo.
Holder Øje med Hundene, holder Øje med de slette Arbejdere, holder Øje med Sønderskærelsen!
3 Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi
Thi vi ere Omskærelsen, vi, som tjene i Guds Ånd og rose os i Kristus Jesus og ikke forlade os på Kødet",
4 ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo. Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo.
endskønt også jeg har det, jeg kunde forlade mig på også i Kødet, Dersom nogen anden synes, han kan forlade sig på Kødet, kan jeg det mere.
5 Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi.
Jeg er omskåren på den ottende Dag, af Israels Slægt, Benjamins Stamme, en Hebræer af Hebræere, over for Loven en Farisæer,
6 Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.
i Nidkærhed en Forfølger af Menigheden, i Retfærdigheden efter Loven udadlelig.
7 Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu.
Men hvad der var mig Vinding, det har jeg for Kristi Skyld agtet for Tab;
8 Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu
ja sandelig, jeg agter endog alt for at være Tab imod det langt højere, at kende Kristus Jesus, min Herre, for hvis Skyld jeg har lidt Tab på alt og agter det for Skarn, for at jeg kan vinde Kristus
9 ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro.
og findes i ham, så jeg ikke har min Retfærdighed, den af Loven, men den ved Tro på Kristus, Retfærdigheden fra Gud på Grundlag af Troen,
10 Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake
for at jeg må kende ham og hans Opstandelses Kraft og hans Lidelsers Samfund, idet jeg bliver ligedannet med hans Død,
11 kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.
om jeg dog kunde nå til Opstandelsen fra de døde.
12 Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira.
Ikke at jeg allerede har grebet det eller allerede er fuldkommen; men jeg jager derefter, om jeg dog kunde gribe det, efterdi jeg også er greben af Kristus Jesus.
13 Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga.
Brødre! jeg mener ikke om mig selv, at jeg har grebet det.
14 Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.
Men eet gør jeg: glemmende, hvad der er bagved, men rækkende efter det, som er foran, jager jeg imod Målet, til den Sejrspris, hvortil Gud fra det høje kaldte os i Kristus Jesus.
15 Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani.
Lader da os, så mange som ere fuldkomne, have dette Sindelag; og er der noget, hvori I ere anderledes sindede, da skal Gud åbenbare eder også dette.
16 Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.
Kun at vi, så vidt vi ere komne, vandre i samme Retning.
17 Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira.
Vorder mine Efterlignere, Brødre! og agter på dem, der vandre således, som I have os til Forbillede.
18 Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu.
Thi mange vandre, som jeg ofte har sagt eder, men nu også siger med Tårer, som Kristi Kors's Fjender,
19 Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi.
hvis Ende er Fortabelse, hvis Gud er Bugen, og hvis Ære er i deres Skændsel, de, som tragte efter de jordiske Ting.
20 Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu.
Thi vort Borgerskab er i Himlene, hvorfra vi også forvente som Frelser den Herre Jesus Kristus,
21 Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.
der skal forvandle vort Fornedrelses-Legeme til at blive ligedannet med hans Herligheds-Legeme, efter den Kraft, ved hvilken han også kan underlægge sig alle Ting.

< Afilipi 3 >