< Numeri 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Eternel parla aussi à Moïse, en disant:
2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
Parle à Aaron, et lui dis: Quand tu allumeras les lampes, les sept lampes éclaireront sur le devant du chandelier.
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
Et Aaron le fit ainsi, et il alluma les lampes [pour éclairer] sur le devant du chandelier, comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse.
4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
Or le chandelier était fait de telle manière, qu'il était d'or battu au marteau, [d'ouvrage] fait au marteau, sa tige aussi, [et] ses fleurs. On fit ainsi le chandelier selon le modèle que l'Eternel en avait fait voir à Moïse.
5 Yehova anawuza Mose kuti,
Puis l'Eternel parla à Moïse, en disant:
6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
Prends les Lévites d'entre les enfants d'Israël, et les purifie.
7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
Tu leur feras ainsi pour les purifier. Tu feras aspersion sur eux de l'eau de purification; ils feront passer le rasoir sur toute leur chair, ils laveront leurs vêtements, et ils se purifieront.
8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
Puis ils prendront un veau pris du troupeau avec son gâteau de fine farine pétrie à l'huile; et tu prendras un second veau pris du troupeau [pour l'offrande] pour le péché.
9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
Alors tu feras approcher les Lévites devant le Tabernacle d assignation, et tu convoqueras toute l'assemblée des enfants d'Israël.
10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
Tu feras, [dis-je], approcher les Lévites devant l'Eternel, et les enfants d'Israël poseront leurs mains sur les Lévites.
11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
Et Aaron présentera les Lévites en offrande devant l'Eternel de la part des enfants d'Israël, et ils seront employés au service de l'Eternel.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
Et les Lévites poseront leurs mains sur la tête des veaux; puis tu en sacrifieras l'un [en offrande] pour le péché, et l'autre en holocauste à l'Eternel, afin de faire propitiation pour les Lévites.
13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
Après tu feras tenir les Lévites devant Aaron et devant ses fils, et tu les présenteras en offrande à l'Eternel.
14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
Ainsi tu sépareras les Lévites d'entre les enfants d'Israël, et les Lévites seront à moi.
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
Après cela les Lévites viendront pour servir au Tabernacle d'assignation, quand tu les auras purifiés, et présentés en offrande.
16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
Car ils me sont entièrement donnés d'entre les enfants d'Israël; je les ai pris pour moi au lieu de tous ceux qui ouvrent la matrice, au lieu de tous les premiers-nés d'entre les enfants d'Israël.
17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
Car tout premier-né d'entre les enfants d'Israël est à moi, tant des hommes que des bêtes; je me les suis sanctifiés le jour que je frappai tout premier-né au pays d'Egypte.
18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
r j'ai pris les Lévites au lieu de tous les premiers-nés d'entre les enfants d'Israël.
19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
Et j'ai entièrement donné d'entre les enfants d'Israël les Lévites à Aaron et à ses fils, pour faire le service des enfants d'Israël dans le Tabernacle d'assignation, et pour servir de rachat pour les enfants d'Israël; afin qu'il n'y ait point de plaie sur les enfants d'Israël, [comme il y aurait] si les enfants d'Israël s'approchaient du Sanctuaire.
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
Moïse et Aaron, et toute l'assemblée des enfants d'Israël firent aux Lévites toutes les choses que l'Eternel avait commandées à Moïse touchant les Lévites; les enfants d'Israël le firent ainsi.
21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
Les Lévites donc se purifièrent, et lavèrent leurs vêtements, et Aaron les présenta en offrande devant l'Eternel, et fit propitiation pour eux afin de les purifier.
22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
Cela étant fait, les Lévites vinrent pour faire leur service au Tabernacle d'assignation devant Aaron, et devant ses fils; et on leur fit comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse touchant les Lévites.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
Puis l'Eternel parla à Moïse, en disant:
24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
C'est ici ce qui concerne les Lévites. Le Lévite depuis l'âge de vingt-cinq ans et au dessus, entrera en service pour être employé au Tabernacle d'assignation;
25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
Mais depuis l'âge de cinquante ans il sortira de service, et ne servira plus.
26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
Cependant il servira ses frères au Tabernacle d'assignation, pour garder ce qui [leur a été commis], mais il ne fera aucun service; tu feras donc ainsi aux Lévites touchant leurs charges.

< Numeri 8 >