< Numeri 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
Speak to Aaron, and thou shalt say to him: When thou shalt place the seven lamps, let the candlestick be set up on the south side. Give orders therefore that the lamps look over against the north, towards the table of the leaves of proposition, over against that part shall they give light, towards which the candlestick looketh.
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
And Aaron did so, and he put the lamps upon the candlestick, as the Lord had commanded Moses.
4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
Now this was the work of the candlestick, it was of beaten gold, both the shaft in the middle, and all that came out of both sides of the branches: according to the pattern which the Lord had shewn to Moses, so he made the candlestick.
5 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
Take the Levites out of the midst of the children of Israel, and thou shalt purify them,
7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
According to this rite: Let them be sprinkled with the water of purification, and let them shave all the hairs of their flesh. And when they shall have washed their garments, and are cleansed,
8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
They shall take an ox of the herd, and for the offering thereof fine flour tempered with oil: and thou shalt take another ox of the herd for a sin offering:
9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
And thou shalt bring the Levites before the tabernacle of the covenant, calling together all the multitude of the children of Israel:
10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
And when the Levites are before the Lord, the children of Israel shall put their hands upon them:
11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
And Aaron shall offer the Levites, as a gift in the sight of the Lord from the children of Israel, that they may serve in his ministry.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
The Levites also shall put their hands upon the heads of the oxen, of which thou shalt sacrifice one for sin, and the other for a holocaust to the Lord, to pray for them.
13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
And thou shalt set the Levites in the sight of Aaron and of his sons, and shalt consecrate them being offered to the Lord,
14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
And shalt separate them from the midst of the children of Israel, to be mine.
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
And afterwards they shall enter into the tabernacle of the covenant, to serve me. And thus shalt thou purify and consecrate them for an oblation of the Lord: for as a gift they were given me by the children of Israel.
16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
I have taken them instead of the firstborn that open every womb in Israel,
17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
For all the firstborn of the children of Israel, both of men and of beasts, are mine. From the day that I slew every firstborn in the land of Egypt, have I sanctified them to myself:
18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
And I have taken the Levites for all the firstborn of the children of Israel:
19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
And have delivered them for a gift to Aaron and his sons out of the midst of the people, to serve me for Israel in the tabernacle of the covenant, and to pray for them, lest there should be a plague among the people, if they should presume to approach unto my sanctuary.
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
And Moses and Aaron and all the multitude of the children of Israel did with the Levites all that the Lord had commanded Moses:
21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
And they were purified, and washed their garments. And Aaron lifted them up in the sight of the Lard, and prayed for them,
22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
That being purified they might go into the tabernacle of the covenant to do their services before Aaron and his sons. As the Lord had commanded Moses touching the Levites, so was it done.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
This is the law of the Levites: From twenty-five years old and upwards, they shall go in to minister in the tabernacle of the covenant.
25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
And when they shall have accomplished the fiftieth year of their age, they shall cease to serve:
26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
And they shall be the ministers of their brethren in the tabernacle of the covenant, to keep the things that are committed to their care, but not to do the works. Thus shalt thou order the Levites touching their charge.

< Numeri 8 >