< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
Le jour où Moïse acheva de dresser la Demeure, de l’oindre et de la sanctifier avec tous ses ustensiles, ainsi que l’autel avec tous ses ustensiles; lorsqu’il les eut oints et sanctifiés,
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
les princes d’Israël, chefs de leurs maisons patriarcales, présentèrent leurs offrandes: c’étaient les princes des tribus, ceux qui avaient présidé au dénombrement.
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
Ils amenèrent leur offrande devant Yahweh: six chars couverts et douze bœufs, soit un char pour deux princes et un bœuf pour chaque prince, et ils les présentèrent devant la Demeure.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh parla à Moïse, en disant:
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
« Reçois d’eux ces choses, et qu’elles soient employées pour le service de la tente de réunion; tu les donneras aux Lévites, à chacun selon les besoins de son service. »
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
Moïse, ayant pris les chars et les bœufs, les remit aux Lévites.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Il donna deux chars et quatre bœufs aux fils de Gerson, selon les besoins de leur service;
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
il donna quatre chars et huit bœufs aux fils de Mérari, selon les besoins de leur service, sous la surveillance d’Ithamar, fils d’Aaron, le prêtre.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
Mais il n’en donna pas aux fils de Caath, parce que, ayant le service des objets sacrés, ils devaient les porter sur leurs épaules.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
Les princes présentèrent leur offrande pour la dédicace de l’autel, le jour où on l’oignit; les princes présentèrent leur offrande devant l’autel.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
Et Yahweh dit à Moïse: « Que chaque jour un prince vienne présenter son offrande pour la dédicace de l’autel. »
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
Celui qui présenta son offrande le premier jour fut Nahasson, fils d’Aminadab, de la tribu de Juda.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
Il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande de Nahasson, fils d’Aminadab.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
Le second jour, Nathanaël, fils de Suar, prince de la tribu d’Issachar, présenta son offrande.
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
Il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande de Nathanaël, fils de Suar.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
Le troisième jour vint le prince des fils de Zabulon, Eliab, fils de Hélon;
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Eliab, fils de Hélon.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
Le quatrième jour vint le prince des fils de Ruben, Elisur, fils de Sédéur;
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Elisur, fils de Sédéur.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
Le cinquième jour vint le prince des fils de Siméon, Salamiel, fils de Surisaddaï;
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande de Salamiel, fils de Surisaddaï.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
Le sixième jour vint le prince des fils de Gad, Eliasaph, fils de Duel;
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Eliasaph, fils de Duel.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
Le septième jour vint le prince des fils d’Ephraïm, Elisama, fils d’Ammiud;
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Elisama, fils d’Ammiud.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
Le huitième jour vint le prince des fils de Manassé, Gamaliel, fils de Phadassur;
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande de Gamaliel, fils de Phadassur.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
Le neuvième jour vint le prince des fils de Benjamin, Abidan, fils de Gédéon;
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Abidan, fils de Gédéon.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
Le dixième jour vint le prince des fils de Dan, Ahiéser, fils d’Ammisaddaï;
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Ahiéser, fils d’Ammisaddaï.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
Le onzième jour vint le prince des fils d’Aser, Phégiel, fils d’Ochran;
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande de Phégiel, fils d’Ochran.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
Le douzième jour vint le prince des fils de Nephtali, Ahira, fils d’Enan;
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
il offrit: un plat d’argent du poids de cent trente sicles, et une coupe d’argent de soixante-dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, l’un et l’autre pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour l’oblation;
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
un godet d’or de dix sicles, plein de parfum;
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
un jeune taureau, un bélier et un agneau d’un an pour l’holocauste;
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
un bouc pour le sacrifice pour le péché,
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
et, pour le sacrifice pacifique, deux bœufs, cinq béliers, cinq boucs et cinq agneaux d’un an. Telle fut l’offrande d’Ahira, fils d’Enan.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
Tels furent les dons des princes d’Israël pour la dédicace de l’autel, le jour où on l’oignit: douze plats d’argent, douze coupes d’argents et douze godets d’or;
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
chaque plat d’argent pesait cent trente sicles, et chaque coupe soixante-dix; total de l’argent de ces ustensiles: deux mille quatre cent sicles, selon le sicle du sanctuaire; —
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
les douze godets d’or pleins de parfum, chacun de dix sicles, selon le sicle du sanctuaire; total de l’or des godets: cent vingt sicles. —
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Total des animaux pour l’holocauste: douze jeunes taureaux, douze béliers et douze agneaux d’un an, avec leurs oblations. Douze boucs pour le sacrifice pour le péché. —
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
Total des animaux pour le sacrifice pacifique: vingt-quatre bœufs, soixante béliers, soixante boucs et soixante agneaux d’un an. Tels furent les dons offerts pour la dédicace de l’autel, après qu’on l’eut oint.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
Lorsque Moïse entrait dans la tente de réunion pour parler avec Yahweh, il entendait la voix qui lui parlait de dessus le propitiatoire placé sur l’arche du témoignage, entre les deux chérubins. Et il lui parlait.

< Numeri 7 >