< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
And it came to pass in the day in which Moses finished the setting-up of the tabernacle, that he anointed it, and consecrated it, and all its furniture, and the altar and all its furniture, he even anointed them, and consecrated them.
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
And the princes of Israel brought [gifts], twelve princes of their fathers' houses: these were the heads of tribes, these are they that presided over the numbering.
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
And they brought their gift before the Lord, six covered waggons, and twelve oxen; a waggon from two princes, and a calf from each: and they brought them before the tabernacle.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying,
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
Take of them, and they shall be for the works of the services of the tabernacle of witness: and you shall give them to the Levites, to each one according to his ministration.
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
And Moses took the waggons and the oxen, and gave them to the Levites.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
And he gave two waggons and four oxen to the sons of Gedson, according to their ministrations.
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
And four waggons and eight oxen he gave to the sons of Merari according to their ministrations, by Ithamar the son of Aaron the priest.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
But to the sons of Caath he gave them not, because they have the ministrations of the sacred things: they shall bear them on their shoulders.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
And the rulers brought [gifts] for the dedication of the altar, in the day in which he anointed it, and the rulers brought their gifts before the altar.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
And the Lord said to Moses, One chief each day, they shall offer their gifts a chief each day for the dedication of the altar.
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
And he that offered his gift on the first day, was Naasson the son of Aminadab, prince of the tribe of Juda.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
And he brought his gift, one silver charger of a hundred and thirty shekels was its weight, one silver bowl, of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels full of incense.
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Naasson the son of Aminadab.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
On the second day Nathanael son of Sogar, the prince of the tribe of Issachar, brought [his offering].
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
And he brought his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
One censer of ten golden shekels, full of incense.
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
And for a sacrifice, a peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Nathanael the son of Sogar.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
On the third day the prince of the sons of Zabulon, Eliab the son of Chaelon.
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Eliab the son of Chaelon.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
On the fourth day Elisur the son of Sediur, the prince of the children of Ruben.
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels full of incense.
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Elisur the son of Sediur.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
On the fifth day the prince of the children of Symeon, Salamiel the son of Surisadai.
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight one hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Salamiel the son of Surisadai.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
On the sixth day the prince of the sons of Gad, Elisaph the son of Raguel.
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat offering.
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Elisaph the son of Raguel.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
On the seventh day the prince of the sons of Ephraim, Elisama the son of Emiud.
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight was a hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Elisama the son of Emiud.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
On the eighth day the prince of the sons of Manasse, Gamaliel the son of Phadassur.
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight one hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour mingled with oil for a meat-offering.
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
One golden censer of ten shekels, full of incense.
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
And for a sacrifice of peace-offering two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Gamaliel the son of Phadassur.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
On the ninth day the prince of the sons of Benjamin, Abidan the son of Gadeoni.
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty [shekels], one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour mingled with oil for a meat-offering.
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Abidan the son of Gadeoni.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
On the tenth day the prince of the sons of Dan, Achiezer the son of Amisadai.
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty [shekels], one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour kneaded with oil for a meat-offering.
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old. This [was] the gift of Achiezer the son of Amisadai.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
On the eleventh day the prince of the sons of Aser, Phageel the son of Echran.
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty [shekels], one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour mingled with oil for a meat-offering.
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Phageel the son of Echran.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
On the twelfth day the prince of the sons of Nephthali, Achire the son of Aenan.
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
[He brought] his gift, one silver charger, its weight a hundred and thirty shekels; one silver bowl of seventy shekels according to the holy shekel; both full of fine flour mingled with oil for a meat offering.
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One golden censer of ten shekels, full of incense.
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One calf of the herd, one ram, one he-lamb of a year old for a whole burnt offering,
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
and one kid of the goats for a sin-offering.
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
And for a sacrifice of peace-offering, two heifers, five rams, five he-goats, five ewe-lambs of a year old: this [was] the gift of Achire the son of Aenan.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
This was the dedication of the altar in the day in which [Moses] anointed it, by the princes of the sons of Israel; twelve silver chargers, twelve silver bowls, twelve golden censers:
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
each charger of a hundred and thirty shekels, and each bowl of seventy shekels: all the silver of the vessels [was] two thousand four hundred shekels, the shekels according to the holy shekel.
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
Twelve golden censers full of incense: all the gold of the shekels, a hundred and twenty shekels.
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
All the cattle for whole burnt offerings, twelve calves, twelve rams, twelve he-lambs of a year old, and their meat-offerings, and their drink-offerings: and twelve kids of the goats for sin-offering.
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
All the cattle for a sacrifice of peace-offering, twenty-four heifers, sixty rams, sixty he-goats of a year old, sixty ewe-lambs of a year old without blemish: this is the dedication of the altar, after that [Moses] consecrated [Aaron], and after he anointed him.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
When Moses went into the tabernacle of witness to speak to God, then he heard the voice of the Lord speaking to him from off the mercy-seat, which is upon the ark of the testimony, between the two cherubs; and he spoke to him.

< Numeri 7 >