< Numeri 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh spoke to Moses. He said,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
“Speak to the people of Israel. Say to them, 'When a man or a woman separates himself to Yahweh with a special vow of a Nazirite,
3 sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
he must keep himself from wine and strong drink. He must not drink vinegar made from wine or from strong drink. He must not drink any grape juice or eat fresh grapes or raisins.
4 Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
In all the days that he is separate to me, he must eat nothing that is made from grapes, including everything made from the seeds to their skins.
5 “‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
During all the time of his vow of separation, no razor is to be used on his head until the days of his separation to Yahweh are fulfilled. He must be set apart to Yahweh. He must let the hair grow long on his head.
6 Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
During all the time that he separates himself to Yahweh, he must not come near a dead body.
7 Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
He must not make himself unclean even for his father, mother, brother, or sister, if they die. This is because he is separated to God, as everyone can see by his long hair.
8 Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
During all the time of his separation he is holy, reserved for Yahweh.
9 “Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
If someone very suddenly dies beside him and defiles his consecrated head, then he must shave his head on the day of his purification—on the seventh day he must shave it.
10 Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
On the eighth day he must bring two doves or two young pigeons to the priest at the entrance to the tent of meeting.
11 Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
The priest must offer one bird as a sin offering and the other as a burnt offering. These will atone for him because he sinned by being near the dead body. He must consecrate his head again on that day.
12 Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
He must set himself apart to Yahweh for the days of his consecration. He must bring a male lamb one year old as a guilt offering. The days before he defiled himself must not be counted, because his consecration was defiled.
13 “Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
This is the law about the Nazirite for when the time of his separation is complete. He must be brought to the entrance of the tent of meeting.
14 Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
He must present his offering to Yahweh. He must offer as a burnt offering a male lamb one year old and without blemish. He must bring as a sin offering a female lamb one year old and without blemish. He must bring a ram as a fellowship offering that is without blemish.
15 ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
He must also bring a basket of bread made without yeast, loaves of fine flour mixed with oil, wafers without yeast rubbed with oil, together with their grain offering and drink offerings.
16 “Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
The priest must present them before Yahweh. He must offer his sin offering and burnt offering.
17 Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
With the basket of unleavened bread, he must present the ram as a sacrifice, the fellowship offering to Yahweh. The priest must present also the grain offering and the drink offering.
18 “Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
The Nazirite must shave his head indicating his separation to God at the entrance to the tent of meeting. He must take the hair from his head and put it on the fire that is under the sacrifice of fellowship offerings.
19 “Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
The priest must take the boiled shoulder of the ram, one loaf of bread without yeast out of the basket, and one wafer without yeast. He must place them into the hands of the Nazirite after he has shaved his head indicating separation.
20 Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
The priest must wave them as an offering before Yahweh, a holy portion for the priest, together with the breast that was waved and the thigh that was presented for the priest. After that, the Nazirite may drink wine.
21 “Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
This is the law for the Nazirite who vows his offering to Yahweh for his separation. Whatever else he may give, he must keep the obligations of the vow he has taken, to keep the promise indicated by the law for the Nazirite.'”
22 Yehova anawuza Mose kuti,
Again Yahweh spoke to Moses. He said,
23 “Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
“Speak to Aaron and to his sons. Say, 'You must bless the people of Israel in this way. You must say to them,
24 “‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
“May Yahweh bless you and keep you.
25 Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
May Yahweh make his face shine on you and be gracious to you.
26 Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
May Yahweh look on you with favor and give you peace.”'
27 Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.
It is in this way that they must give my name to the people of Israel. Then I will bless them.”

< Numeri 6 >