< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
И рече Господь к Моисею и Аарону, глаголя:
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
возми сочисление сынов Каафовых от среды сынов Левииных, по сонмом их, по домом отечеств их,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, всяк входяй служити, творити вся дела в скинии свидения.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
И сия дела сынов Каафовых от среды сынов Левииных, по сонмом их, по домом отечеств их, в скинии свидения Святое Святых.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
И да внидут Аарон и сынове его, егда воздвигнется полк, и да снимут завесу осеняющую, и да обвиют в ню кивот свидения,
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
и да покрыют его покровом кожаным синим, и да возложат нань одежду всю синетную сверху, и да вложат носила:
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
и на трапезе предложения да положат на ней одежду всю багряную и блюда, и кадилницы и чашы, и возливалницы, имиже возливают, и хлебы на ней всегда да будут:
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
и да возложат на ню одежду червлену, и да покрыют ю покровом кожаным синим, и да вложат носила ея:
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
и да возмут одежду синю, и покрыют светилник светящий и свещы его, и щипцы его и очищала его, и вся сосуды елеа его, имиже служат в них:
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
и да вложат его и вся сосуды его в покров кожан синий, и да возложат его на носила:
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
и на олтарь златый да положат одежду синю, и да покрыют его покровом кожаным синим, и да вложат носила его:
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
и да возмут вся сосуды служебныя, еликими служат в них во святых, и вложат во одежду синю, и да покрыют их покровом кожаным синим, и да возложат на носила:
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
и покров да возложат на олтарь, и покрыют его одеждою всею багряною:
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
и да возложат на него вся сосуды его, еликими служат на нем в них, и кадилники, и вилицы и чашы, и покров и вся сосуды олтаря, и да возложат на него покров кожан синь и да вложат носила его: и да возмут одежду багряну, и да покрыют умывалницу и стояла ея: и да вложат ю в покров кожаный синий, и да возложат на носила.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
И совершат Аарон и сынове его, покрывающе святая и вся сосуды святыя, внегда воздвизатися полку: и по сих да внидут сынове Каафовы воздвизати, и да не прикоснутся святых, да не умрут. Сия да воздвизают сынове Каафовы в скинии свидения.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
Надсмотритель Елеазар, сын Аарона жерца, елей светилный, и фимиам сложения, и жертва яже по вся дни, и елей помазания, надсмотрение всея скинии и елика суть в ней во святем, во всех делех.
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
И рече Господь к Моисею и Аарону, глаголя:
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
не потребите сонм племене Каафова от среды левитов:
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
сие сотворите им, и живи будут и не умрут: приходящым им ко Святым Святых, Аарон и сынове его да внидут и да устроят их коегождо по ношению его,
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
и да не внидут внезапу видети святая, и умрут.
21 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господь к Моисею, глаголя:
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
возми сочисление сынов Гирсоних, и иже по домом отечеств их, по сонмом их и по племенем их,
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, соглядайте я, всяк входяй служити и творити дела в скинии свидения.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
Сия служба сонма Гирсонова, служити и воздвизати.
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
И да воздвигнет опоны скинии и скинию свидения, и покров ея и покров синий сущий сверх ея, и опону дверий скинии свидения,
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
и опоны двора, и завесу дверий двора, елика над скиниею свидения, и яже окрест олтаря, и прочая их, и вся сосуды служебныя, еликими служат в них, да сотворят.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
По слову Аарона и сынов его да будет вся служба сынов Гирсоновых по всем службам их и по всем делам их: и да соглядаеши их по именам, вся носимая ими.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
Сия служба сонма сынов Гирсоновых в скинии свидения, и стражба их рукою Ифамара, сына Аароня жерца.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Сынове Мерарины по сонмом их, по домом отечеств их, соглядайте их,
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, соглядайте их, всяк входяй служити дела скинии свидения.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
И сия хранения воздвизаемых ими, по всем делом их в скинии свидения: главицы скинии и вереи ея, и столпы ея и стояла ея, и покров и стояла их, и столпы их, и покров дверий скинии,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
и столпы двора окрест и стояла их, и столпы завесы дверий двора и стояла их, и колки их и верви их, и вся сосуды их и вся служения их: по именам соглядайте их и вся сосуды стражбы воздвизаемых ими.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
Сия служба сонма сынов Мерариных во всех делех их, в скинии свидения рукою Ифамара, сына Аароня жерца.
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
И согляда Моисей и Аарон и князи Израилевы сыны Каафовы по сонмом их, по домом отечеств их,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, всяк входяй служити и творити дела в скинии свидения.
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
И бысть соглядание их по сонмом их, две тысящы седмь сот пятьдесят.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Сие сочтение сонма Каафова, всех служащих в скинии свидения, якоже согляда Моисей и Аарон повелением Господним, рукою Моисеовою.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
И соглядани быша сынове Гирсони по сонмом своим, по домом отечеств своих,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, всяк входяй служити и творити дела в скинии свидения.
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
И бысть соглядание их по сонмом их, по домом отечеств их, две тысящы шесть сот тридесять.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Сие соглядание сонма сынов Гирсоновых, всех служащих в скинии свидения, ихже соглядаша Моисей и Аарон по глаголу Господню, рукою Моисеовою.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Соглядани же быша сынове Мерарины по сонмом своим, по домом отечеств своих,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, всяк входяй служити на дела скинии свидения.
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
И бысть сочтение их по племеном их, по сонмом их, по домом отечеств их, три тысящы и двести.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
Сие сочисление сонма сынов Мерариных, ихже согляда Моисей и Аарон по глаголу Господню, рукою Моисеовою.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Вси согляданнии левиты, ихже согляда Моисей и Аарон и князи сынов Израилевых, по сонмом их и по домом отечеств их,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
от двадесяти и пяти лет и вышше, даже до пятидесяти лет, всяк входяй на дело дел, и к делам воздвизаемым в скинии свидения.
48 analipo 8,580.
И быша согляданнии осмь тысящ пять сот осмьдесят.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
Повелением Господним соглядаше их Моисей, мужа по мужу над делы их, и яже воздвизаху сии, и соглядани суть, якоже повеле Господь Моисею.

< Numeri 4 >