< Numeri 36 >

1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
And the heads of the fathers of the family of the sons of Gilead, the son of Machir, the son of Manasseh, of the families of the sons of Joseph, came near, and spoke before Moses, and before the rulers, the heads of the fathers of the sons of Israel.
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
And they said, Jehovah commanded my lord to give the land for inheritance by lot to the sons of Israel. And my lord was commanded by Jehovah to give the inheritance of Zelophehad our brother to his daughters.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
And if they be married to any of the sons of the other tribes of the sons of Israel, then their inheritance will be taken away from the inheritance of our fathers, and will be added to the inheritance of the tribe to which they shall belong. So it will be taken away from the lot of our inheritance.
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
And when the jubilee of the sons of Israel shall be, then their inheritance will be added to the inheritance of the tribe to which they shall belong. So their inheritance will be taken away from the inheritance of the tribe of our fathers.
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
And Moses commanded the sons of Israel according to the word of Jehovah, saying, The tribe of the sons of Joseph speak right.
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
This is the thing which Jehovah commands concerning the daughters of Zelophehad, saying, Let them be married to whom they think best, only into the family of the tribe of their father shall they be married.
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
So no inheritance of the sons of Israel shall remove from tribe to tribe, for the sons of Israel shall cling each one to the inheritance of the tribe of his fathers.
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
And every daughter, who possesses an inheritance in any tribe of the sons of Israel, shall be wife to one of the family of the tribe of her father, that the sons of Israel may possess every man the inheritance of his fathers.
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
So no inheritance shall move from one tribe to another tribe, for the tribes of the sons of Israel shall cling each one to his own inheritance.
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
Even as Jehovah commanded Moses, so did the daughters of Zelophehad,
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
for Mahlah, Tirzah, and Hoglah, and Milcah, and Noah, the daughters of Zelophedad, were married to their father's brothers' sons.
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
They were married into the families of the sons of Manasseh the son of Joseph, and their inheritance remained in the tribe of the family of their father.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
These are the commandments and the ordinances which Jehovah commanded by Moses to the sons of Israel in the plains of Moab by the Jordan at Jericho.

< Numeri 36 >