< Numeri 35 >

1 Ku zigwa za Mowabu pafupi ndi Yorodani ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede fremdeles til Moses på Moabs Sletter ved Jordan over for Jeriko og sagde:
2 “Lamula Aisraeli kuti apereke kwa Alevi midzi yoti azikhalamo kuchokera pa cholowa chomwe adzalandira. Muwapatsenso malo oweteramo ziweto kuzungulira midziyo.
byd Israelitterne, at de af de Besiddelser, de får i Arv, skal give Leviterne nogle Byer at bo i; I skal også give Leviterne Græsmarker rundt om disse Byer,
3 Midziyo idzakhala yawo ndipo azidzakhala mʼmenemo. Malo a msipu adzakhala a ngʼombe, nkhosa ndi zoweta zawo zina zonse.
Disse Byer skal de have at bo i, og deres Græsmarker skal de have til deres Kvæg, deres Hjorde og andre Dyr.
4 “Malo a msipu a mudziwo amene mudzawapatse Aleviwo, adzayambire ku khoma la mudzi ndipo adzatuluke kunja mamita 450, kuzungulira mudziwo.
Græsmarkerne om Byerne, som I skal give Leviterne, skal strække sig 1000 Alen fra Bymuren ud til alle Sider;
5 Kunja kwa mudzi yezani mamita 900 kummawa, mamita 900 kumpoto ndipo mudziwo ukhale pakati. Adzakhala ndi dera limeneli ngati malo a midziyo, owetera ziweto zawo.
og uden for Byen skal I til Østside opmåle 2000 Alen, til Sydside 2000, til Vestside 2000 og til Nordside 2000, med Byen i Midten. Det skal tilfalde dem som Græsgange til Byerne.
6 “Isanu ndi umodzi mwa midzi imene mudzapereke kwa Alevi idzakhala mizinda yopulumukirako, kumene munthu wopha mnzake adzathawireko. Ndipo mudzawapatsenso midzi ina 42.
Hvad de Byer angår, som I skal give Leviterne, så skal I give dem de seks Tilflugtsbyer, som Manddrabere kan ty ind i, og desuden to og fyrretyve Byer.
7 Midzi yonse imene mudzapereke kwa Alevi idzakhale 48, pamodzi ndi malo oweterako ziweto.
De Byer, I skal give Leviterne, bliver således i alt otte og fyrretyve Byer med tilhørende Græsmarker.
8 Pamene mukupatula midzi imeneyi pa cholowa cha Aisraeli, muchotsepo midzi yambiri pa mafuko aakulu, ndipo midzi pangʼono pa mafuko aangʼono. Fuko lililonse lidzapereka kwa Alevi molingana ndi kukula kwa cholowa chimene lalandira.”
Og af de Byer, I skal give dem af Israelitternes Besiddelser, skal I lade de større Stammer give flere, de mindre færre; hver Stamme skal give Leviterne så mange af sine Byer, som svarer til den Arvelod, der tildeles den.
9 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
10 “Yankhula ndi Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mu Kanaani,
Tal til Israelitterne og sig til dem: Når I kommer over Jordan til Kana'ans Land,
11 sankhani midzi ina kuti ikhale mizinda yanu yopulumukirako, kumene munthu wopha munthu wina mwangozi angathawireko.
skal I udse eder nogle Byer, I kan have som Tilflugtsbyer, så at en Manddraber, der begår et Drab af Vanvare, kan ty derhen.
12 Adzakhala malo obisalako pothawa munthu wofuna kulipsira, kuti munthu wopha mnzake mwangozi asaphedwe mpaka akayime pamaso pa gulu la anthu kuti akaweruzidwe.
I disse Byer skal I have Ret til at søge Tilflugt for Blodhævneren, for at ikke Manddraberen skal dø, før han er blevet stillet for Menighedens Domstol.
13 Midzi isanu ndi umodzi imene muyiperekeyi idzakhala mizinda yopulumukirako.
Det skal være seks Byer, I skal afstå til Tilflugtsbyer;
14 Mupereke itatu mbali ino ya Yorodani ndi itatu ina mu Kanaani kuti ikhale mizinda yopulumukirako.
de tre skal I afstå hinsides Jordan og de tre andre i Kana'ans Land; de skal være Tilflugtsbyer.
15 Midzi isanu ndi umodzi idzakhala malo opulumukirako Aisraeli, alendo ndi anthu ena onse okhala pakati pawo kuti wina aliyense wopha mnzake mwangozi adzathawireko.
Israelitterne, de fremmede og de indvandrede iblandt dem skal have Ret til at søge Tilflugt i de seks Byer, så at enhver, der begår et Drab af Vanvare, kan ty derhen.
16 “‘Ngati munthu amenya mnzake ndi chitsulo, munthuyo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha ndipo wakuphayo aphedwe.
Men slår han ham ihjel med et Jernredskab, så er han en Manddraber, og Manddraberen skal lide Døden;
17 Kapenanso ngati wina wake ali ndi mwala mʼdzanja mwake womwe ungaphe munthu, ndipo agenda nawo wina, munthu winayo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha ndipo wakuphayo adzayenera kuphedwa.
og slår han ham ihjel med en Sten, som han har i Hånden, og som kan slå en Mand ihjel, så er han en Manddraber, og Manddraberen skal lide Døden;
18 Kapenanso ngati wina ali ndi chibonga mʼdzanja mwake choti nʼkupha nacho munthu, namenya nacho munthu, munthuyo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha, wakuphayo ayenera kuphedwa.
og slår han ham ihjel med et Træredskab, som han har i Hånden, og som kan slå en Mand ihjel, så er han en Manddraber, og Måddraberen skal lide Døden.
19 Wolipsira adzamuphanso wakuphayo. Pamene akumana naye adzayenera kumupha ndithu.
Blodhævneren skal dræbe Manddraberen; når han træffer ham, skal han dræbe ham.
20 Ndipo ngati wina wake, chifukwa cha udani, aganiza zokankha munthu wina kapena kumuponyera chinthu china mwadala munthuyo nʼkufa,
Og støder han til ham af Had eller kaster noget på ham i ond Hensigt, så han dør deraf,
21 kapena ngati, chifukwa cha udani, amenya mnzake ndi nkhonya, mnzakeyo ndi kufa, munthuyo ayenera kuphedwa. Iyeyo ndi wakupha. Wolipsira adzamuphe wakuphayo pamene akumana naye.
eller slår han ham med Hånden i Fjendskab, så han dør deraf, skal drabsmanden lide Døden, thi han er en Manddraber; Blodhævneren skal dræbe Manddraberen, når han træffer ham.
22 “‘Koma ngati popanda udani wina uliwonse, mwadzidzidzi akankha wina kapena kumuponyera chinthu osati mwadala,
Støder han derimod til ham af Vanvare, ikke i Fjendskab, eller kaster han et Redskab på ham, uden at det er i ond Hensigt,
23 kapena mosamuona nʼkumuponyera mwala womwe utha kumupha, munthuyo nʼkufa, tsono pakuti sanali mdani wake ndipo sanaganizire zomupweteka,
eller rammer han ham uden at se ham med en Sten, som kan slå en Mand ihjel, så han dør deraf, og han ikke er hans Uven eller har pønset på ondt imod ham,
24 gulu liweruze pakati pa iye ndi wolipsira monga mwa malamulo ake.
så skal Menigheden dømme Drabsmanden og Blodhævneren imellem på Grundlag af disse Lovbud;
25 Gulu lidzapulumutsa munthu wakuphayo mʼmanja mwa wolipsira uja ndi kumubwezera ku mzinda wopulumukirako kumene anathawira. Ayenera kukhala kumeneko kufikira imfa ya mkulu wa ansembe, amene anadzozedwa ndi mafuta oyera.
og Menigheden skal værne Manddraberen mod Blodhævneren, og Menigheden skal føre ham tilbage til hans Tilflugtsby, hvorhen han var tyet, og der skal han blive boende, indtil den med hellig Olie salvede Ypperstepræst dør.
26 “‘Koma ngati wolakwayo atuluka kunja kwa malire a mzinda wopulumukirako kumene anathawira
Men hvis Manddraberen for lader sin Tilflugtsbys Område, hvorhen han er tyet,
27 ndipo wobwezera choyipa nʼkumupeza kunja kwa mzindawo, wolipsirayo atha kumupha wolakwayo popanda kugamula mlandu wakupha.
og Blodhævneren træffer ham uden for hans Tilflugtsbys Område, så kan Blodhævneren dræbe Manddraberen uden at pådrage sig Blodskyld;
28 Wolakwayo ayenera kukhala mu mzinda wopulumukiramowo mpaka imfa ya mkulu wa ansembe ndipo pamenepo atha kubwerera kwawo. Pokhapokha atafa mkulu wa ansembe ndi pamene angathe kubwerera ku malo ake.
thi han skal blive i sin Tilflugtsby indtil Ypperstepræstens Død; først efter Ypperstepræstens Død kan Manddraberen vende tilbage til den Jord, han ejer.
29 “‘Amenewa akhale malamulo ndi malangizo kwa inu nthawi zonse ndi ku mibado ya mʼtsogolo, kulikonse kumene mudzakhalako.
Det skal være eder en retsgyldig Anordning fra Slægt til Slægt, hvor I end bor.
30 “‘Aliyense wopha munthu ayeneranso kuphedwa ngati pali umboni okwanira. Koma wina asaphedwe ngati pali mboni imodzi yokha.
Når nogen slår et Menneske ihjel, må man kun dræbe Manddraberen efter flere Vidners Udsagn. Et enkelt Vidnes Udsagn er ikke nok til en Dødsdom.
31 “‘Osalola kulandira dipo lowombolera munthu wakupha yemwe ayenera kuphedwa. Wakupha ayenera kuphedwa.
I må ikke tage mod Sonebøde for en Manddraber, når han har forbrudt sit Liv; han skal lide Døden,
32 “‘Simuyeneranso kulandira dipo kwa munthu amene wathawira ku mzinda wopulumikirako kuti wothawayo abwerere kwawo, pokhapokha ngati mkulu wa ansembe wamwalira.
Heller ikke må I tage mod Sonebøde, således at den, der er tyet til sin Tilflugtsby, før Ypperstepræstens Død kan vende tilbage og bosætte sig i Landet.
33 “‘Musayipitse dziko limene mukukhalamolo. Magazi amayipitsa dziko ndipo nʼkosatheka kulipirira dziko chifukwa cha magazi amene akhetsedwa mʼmenemo, kupatula pokhetsa magazi a munthu amene anakhetsa magaziyo.
Vanhelliger ikke det Land, I er i, thi Blodet vanhelliger Landet, og Landet får kun Soning for det Blod, der er udgydt deri, ved dens Blod, der har udgydt det.
34 Choncho musadetse dziko limene mukukhalamo, dziko limene Inenso ndimakhalamo, pakuti Ine Yehova, ndimakhala pakati pa Aisraeli.’”
Gør ikke det Land urent, I er bosat i, og i hvis Midte jeg bor; thi jeg HERREN bor midt iblandt Israels Børn.

< Numeri 35 >