< Numeri 3 >

1 Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
Now these are the generations of Aaron and Moses in the day that Jehovah spoke with Moses in mount Sinai:
2 Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
And these are the names of the sons of Aaron: Nadab the firstborn, and Abihu, Eleazar, and Ithamar.
3 Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
These are the names of the sons of Aaron, the priests who were anointed, whom he consecrated to minister in the priest's office.
4 Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
And Nadab and Abihu died before Jehovah when they offered strange fire before Jehovah in the wilderness of Sinai, and they had no sons. And Eleazar and Ithamar ministered in the priest's office in the presence of Aaron their father.
5 Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
6 “Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
Bring the tribe of Levi near, and set them before Aaron the priest, that they may minister to him.
7 Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
And they shall keep his charge, and the charge of the whole congregation before the tent of meeting, to do the service of the tabernacle.
8 Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
And they shall keep all the furniture of the tent of meeting, and the charge of the sons of Israel, to do the service of the tabernacle.
9 Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
And thou shall give the Levites to Aaron and to his sons. They are wholly given to him on the behalf of the sons of Israel.
10 Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
And thou shall appoint Aaron and his sons, and they shall keep their priesthood. And the stranger who comes near shall be put to death.
11 Yehova anawuzanso Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
12 “Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
And I, behold, I have taken the Levites from among the sons of Israel instead of all the firstborn who opens the womb among the sons of Israel. And the Levites shall be mine,
13 pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
for all the firstborn are mine. On the day that I smote all the firstborn in the land of Egypt I hallowed to me all the firstborn in Israel, both man and beast. They shall be mine. I am Jehovah.
14 Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
And Jehovah spoke to Moses in the wilderness of Sinai, saying,
15 “Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
Number the sons of Levi by their fathers' houses, by their families. Thou shall number them, every male from a month old and upward.
16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
And Moses numbered them according to the word of Jehovah, as he was commanded.
17 Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
And these were the sons of Levi by their names: Gershon, and Kohath, and Merari.
18 Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
And these are the names of the sons of Gershon by their families: Libni and Shimei.
19 Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
And the sons of Kohath by their families: Amram, and Izhar, Hebron, and Uzziel.
20 Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
And the sons of Merari by their families: Mahli and Mushi. These are the families of the Levites according to their fathers' houses.
21 Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
Of Gershon was the family of the Libnites, and the family of the Shimeites. These are the families of the Gershonites.
22 Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
Those who were numbered of them, according to the number of all the males, from a month old and upward, even those who were numbered of them were seven thousand and five hundred.
23 Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
The families of the Gershonites shall encamp behind the tabernacle westward.
24 Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
And the ruler of the fathers' house of the Gershonites shall be Eliasaph the son of Lael.
25 Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
And the charge of the sons of Gershon in the tent of meeting shall be the tabernacle, and the tent, the covering of it, and the screen for the door of the tent of meeting,
26 ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
and the hangings of the court, and the screen for the door of the court, which is by the tabernacle, and by the altar round about, and the cords of it for all the service thereof.
27 Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
And of Kohath was the family of the Amramites, and the family of the Izharites, and the family of the Hebronites, and the family of the Uzzielites. These are the families of the Kohathites.
28 Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
According to the number of all the males, from a month old and upward, there were eight thousand and six hundred, keeping the charge of the sanctuary.
29 Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
The families of the sons of Kohath shall encamp on the side of the tabernacle southward.
30 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
And the ruler of the fathers' house of the families of the Kohathites shall be Elizaphan the son of Uzziel.
31 Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
And their charge shall be the ark, and the table, and the lampstand, and the altars, and the vessels of the sanctuary with which they minister, and the screen, and all the service thereof.
32 Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
And Eleazar the son of Aaron the priest shall be ruler of the rulers of the Levites, with the oversight of those who keep the charge of the sanctuary.
33 Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
Of Merari was the family of the Mahlites, and the family of the Mushites. These are the families of Merari.
34 Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
And those who were numbered of them, according to the number of all the males, from a month old and upward, were six thousand and two hundred.
35 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
And the ruler of the fathers' house of the families of Merari was Zuriel the son of Abihail. They shall encamp on the side of the tabernacle northward.
36 Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
And the appointed charge of the sons of Merari shall be the boards of the tabernacle, and the bars of it, and the pillars of it, and the sockets of it, and all the instruments of it, and all the service thereof,
37 pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
and the pillars of the court round about, and their sockets, and their pegs, and their cords.
38 Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
And those who encamp before the tabernacle eastward, before the tent of meeting toward the sunrise, shall be Moses, and Aaron and his sons, keeping the charge of the sanctuary for the charge of the sons of Israel. And the stranger that comes near shall be put to death.
39 Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
All who were numbered of the Levites, whom Moses and Aaron numbered at the commandment of Jehovah, by their families, all the males from a month old and upward, were twenty-two thousand.
40 Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
And Jehovah said to Moses, Number all the firstborn males of the sons of Israel from a month old and upward, and take the number of their names.
41 Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
And thou shall take the Levites for me (I am Jehovah) instead of all the firstborn among the sons of Israel, and the cattle of the Levites instead of all the firstlings among the cattle of the sons of Israel.
42 Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
And Moses numbered, as Jehovah commanded him, all the firstborn among the sons of Israel.
43 Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
And all the firstborn males according to the number of names, from a month old and upward, of those who were numbered of them, were twenty-two thousand two hundred and seventy-three.
44 Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
45 “Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
Take the Levites instead of all the firstborn among the sons of Israel, and the cattle of the Levites instead of their cattle. And the Levites shall be mine. I am Jehovah.
46 Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
And for the redemption of the two hundred and seventy-three of the firstborn of the sons of Israel, who are over and above the number of the Levites,
47 utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
thou shall take five shekels apiece by the poll. According to the shekel of the sanctuary thou shall take them (the shekel is twenty gerahs),
48 Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
and thou shall give the money, with which the odd number of them is redeemed, to Aaron and to his sons.
49 Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
And Moses took the redemption-money from those who were over and above those who were redeemed by the Levites.
50 Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
He took the money from the firstborn of the sons of Israel, a thousand three hundred and sixty-five shekels, according to the shekel of the sanctuary.
51 Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.
And Moses gave the redemption-money to Aaron and to his sons, according to the word of Jehovah, as Jehovah commanded Moses.

< Numeri 3 >