< Numeri 29 >

1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
И в месяц седмый, первый (день) месяца нарочит свят да будет вам: всякаго дела служебна да не сотворите: день знамения будет вам.
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
И сотворите всесожжения в воню благовония Господу, телца от волов единаго, овна единаго, агнцев единолетных седмь непорочных:
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
жертва их мука пшенична вмешана в елеи: три десятины телцу единому и две десятины овну единому:
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
по десятине агнцу единому, седми агнцем:
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
и козла от коз единаго греха ради, во еже умолити о вас:
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
кроме всесожжений новомесячия и жертвы их, и возлияния их, и всесожжение всегдашнее: и жертвы их и возлияния их, по уставу их, в воню благовония Господу.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
И десятый день месяца сего нарочит свят да будет вам: и озлобите душы вашя, и всякаго дела служебна да не сотворите,
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
и принесете всесожжение в воню благовония Господу, приносы Господу: телца единаго от говяд, овна единаго, агнцев единолетных седмь: непорочны да будут вам:
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
жертва их мука пшенична вмешана в елеи: три десятины телцу единому и две десятины овну единому:
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
по десятине агнцу единому, на седмь агнцев:
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
и козла единаго от коз греха ради, во еже умолити о вас: кроме еже греха ради очищения, и всесожжение всегдашнее: жертва его и возлияние его, по уставу его в воню благовония принос Господу.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
И пятыйнадесять день седмаго месяца сего нарочит свят да будет вам: всякаго дела служебна да не сотворите, и празднуйте той праздник Господеви седмь дний,
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
и принесите всесожжения принос в воню благовония Господу: в первый день телцев от говяд тринадесять, овна два, агнцев единолетных четыренадесять: непорочны да будут вам:
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
жертвы их мука пшенична вмешана в елеи: три десятины телцу единому, тремнадесяти телцем, и две десятины овну единому, на два овна:
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
по десятине агнцу единому, на четыренадесять агнцев:
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла единаго от коз греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
И в день вторый телцев дванадесять, овна два, агнцев единолетных четыренадесять непорочных:
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертва их и возлияния их телцем и овном и агнцем по числу их, по уставу их:
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла единаго от коз греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
В день третий телцев единнадесять, овна два, агнцев единолетных четыренадесять непорочных:
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертва их и возлияния их телцем и овном и агнцем по числу их, по уставу их:
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла от коз единаго греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
В день четвертый телцев десять, овна два, агнцев единолетных четыренадесять непорочных:
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертвы их и возлияния их телцем и овном и агнцем по числу их, по уставу их:
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла от коз единаго греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
В день пятый телцев девять, овна два, агнцев единолетных четыренадесять непорочных:
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертвы их и возлияния их телцем и овном и агнцем но числу их, по уставу их:
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла от коз единаго греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
В день шестый телцев осмь, овна два, агнцев единолетных четыренадесять непорочных:
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертвы их и возлияния их телцем и овном и агнцем по числу их, по уставу их:
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла от коз единаго греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
В день седмый телцев седмь, овна два, агнцев единолетных четыренадесять непорочных:
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертвы их и возлияния их телцем и овном и агнцем по числу их, по уставу их:
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла от коз единаго греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
И в день осмый исход будет вам: всякаго дела служебна да не сотворите в онь,
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
и да принесете всесожжения в воню благовония Господу, телца единаго, овна единаго, агнцев единолетных седмь непорочных:
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
жертвы их и возлияния их телцу и овну и агнцем по числу их, по уставу их:
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
и козла от коз единаго греха ради: кроме всесожжения всегдашняго, жертвы их и возлияния их.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
Сия сотворите Господу в праздники вашя, кроме обетов ваших, и вольная ваша, и всесожжения ваша, и жертвы вашя, и возлияния ваша, и спасителная ваша.
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
И глагола Моисей сыном Израилевым по всем, елика заповеда Господь Моисею:

< Numeri 29 >