< Numeri 27 >

1 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
Then drew near the daughters of Zelophehad, the son of Hepher, the son of Gilead, the son of Makir, the son of Manasseh, of the families of Manasseh the son of Joseph; and these are the names of his daughters: Mahlah, Noah, and Hoglah, and Milcah, and Tirzah.
2 pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
They stood before Moses, and before Eleazar the priest, and before the princes and all the congregation, at the door of the Tent of Meeting, saying,
3 “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
"Our father died in the wilderness, and he was not among the company of those who gathered themselves together against Jehovah in the company of Korah: but he died in his own sin; and he had no sons.
4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
Why should the name of our father be taken away from among his family, because he had no son? Give to us a possession among the brothers of our father."
5 Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
Moses brought their cause before Jehovah.
6 ndipo Yehova anati kwa iye,
Jehovah spoke to Moses, saying,
7 “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
"The daughters of Zelophehad speak right: you shall surely give them a possession of an inheritance among their father's brothers; and you shall cause the inheritance of their father to pass to them.
8 “Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
You shall speak to the children of Israel, saying, 'If a man dies, and has no son, then you shall cause his inheritance to pass to his daughter.
9 Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
If he has no daughter, then you shall give his inheritance to his brothers.
10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
If he has no brothers, then you shall give his inheritance to his father's brothers.
11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
If his father has no brothers, then you shall give his inheritance to his kinsman who is next to him of his family, and he shall possess it: and it shall be to the children of Israel a statute and ordinance, as Jehovah commanded Moses.'"
12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
Jehovah said to Moses, "Go up into this mountain of Abarim, and see the land which I have given to the children of Israel.
13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
When you have seen it, you also shall be gathered to your people, as Aaron your brother was gathered;
14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
because you rebelled against my word in the wilderness of Zin, in the strife of the congregation, to sanctify me at the waters before their eyes." (These are the waters of Meribah of Kadesh in the wilderness of Zin.)
15 Mose anati kwa Yehova,
Moses spoke to Jehovah, saying,
16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
"Let Jehovah, the God of the spirits of all flesh, appoint a man over the congregation,
17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
who may go out before them, and who may come in before them, and who may lead them out, and who may bring them in; that the congregation of Jehovah not be as sheep which have no shepherd."
18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
Jehovah said to Moses, "Take Joshua the son of Nun, a man in whom is the Spirit, and lay your hand on him;
19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
and set him before Eleazar the priest, and before all the congregation; and commission him in their sight.
20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
You shall put of your honor on him, that all the congregation of the children of Israel may obey.
21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
He shall stand before Eleazar the priest, who shall inquire for him by the judgment of the Urim before Jehovah: at his word shall they go out, and at his word they shall come in, both he, and all the children of Israel with him, even all the congregation."
22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
Moses did as Jehovah commanded him; and he took Joshua, and set him before Eleazar the priest, and before all the congregation:
23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.
and he laid his hands on him, and commissioned him, as Jehovah spoke by Moses.

< Numeri 27 >