< Numeri 24 >

1 Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu.
And when Balaam saw that it pleased Jehovah to bless Israel, he did not go, as at the other times, to meet with omens, but he set his face toward the wilderness.
2 Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye
And Balaam lifted up his eyes, and he saw Israel dwelling according to their tribes, and the Spirit of God came upon him.
3 ndipo ananena uthenga wake: “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,
And he took up his oracle, and said, Balaam the son of Beor says, and the man whose eye was closed says,
4 uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:
he says who hears the words of God, who sees the vision of the Almighty, falling down, and having his eyes open,
5 “Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo, misasa yako, iwe Israeli!
How goodly are thy tents, O Jacob, thy tabernacles, O Israel!
6 “Monga zigwa zotambalala, monga minda mʼmbali mwa mtsinje, monga aloe wodzalidwa ndi Yehova, monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.
As valleys they are spread forth, as gardens by the river-side, as aloes which Jehovah has planted, as cedar trees beside the waters.
7 Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake; mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri. “Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi; ufumu wake udzakwezedwa.
Water shall flow from his buckets, and his seed shall be in many waters, and his king shall be higher than Agag, and his kingdom shall be exalted.
8 “Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto ali ndi mphamvu ngati za njati. Amawononga mitundu yomuwukira ndi kuphwanya mafupa awo, amalasa ndi mivi yake.
God brings him forth out of Egypt. He has as it were the strength of the wild-ox. He shall eat up the nations his adversaries, and shall break their bones in pieces, and smite them through with his arrows.
9 Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi, monga mkango waukazi, adzamuputa ndani? “Amene adalitsa iwe, adalitsike ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”
He couched, he lay down as a lion, and as a lioness. Who shall rouse him up? He who blesses thee is blessed, And he who curses thee is cursed.
10 Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka.
And Balak's anger was kindled against Balaam, and he struck his hands together. And Balak said to Balaam, I called thee to curse my enemies, and, behold, thou have altogether blessed them these three times.
11 Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”
Therefore now flee thou to thy place. I thought to promote thee to great honor, but, lo, Jehovah has kept thee back from honor.
12 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine,
And Balaam said to Balak, Did I not also speak to thy messengers that thou sent to me, saying,
13 kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena?
If Balak would give me his house full of silver and gold, I cannot go beyond the word of Jehovah, to do either good or bad of my own mind. What Jehovah speaks, that I will speak?
14 Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
And now, behold, I go to my people. Come, I will advise thee what this people shall do to thy people in the latter days.
15 Ndipo iye ananena uthenga wake nati, “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.
And he took up his oracle, and said, Balaam the son of Beor says, and the man whose eye was closed says,
16 Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba, amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:
he says who hears the words of God, and knows the knowledge of the Most High, who sees the vision of the Almighty, falling down, and having his eyes open:
17 “Ndikumuona iye koma osati tsopano; ndikumupenya iye koma osati pafupi. Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo; ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli. Iye adzagonjetsa Mowabu ndi kugonjetsa ana onse a Seti.
I see him, but not now. I behold him, but not near. There shall come forth a star out of Jacob, and a scepter shall rise out of Israel, and shall smite through the corners of Moab, and break down all the sons of tumult.
18 Edomu adzagonjetsedwa; Seiri, mdani wake, adzawonongedwa koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.
And Edom shall be a possession, Seir also shall be a possession, who were his enemies, while Israel does valiantly.
19 Wolamulira adzachokera mwa Yakobo ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”
And out of Jacob shall come he who shall have dominion, and shall destroy the remnant from the city.
20 Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: “Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu koma potsiriza pake adzawonongeka.”
And he looked on Amalek, and took up his oracle, and said, Amalek was the first of the nations, but his latter end shall come to destruction.
21 Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake, “Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa, chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;
And he looked on the Kenite, and took up his oracle, and said, Strong is thy dwelling-place, and thy nest is set in the rock.
22 komabe inu Akeni mudzawonongedwa, pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”
Nevertheless Kain shall be wasted, until Asshur shall carry thee away captive.
23 Ndipo ananenanso uthenga wina kuti, “Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?
And he took up his oracle, and said, Alas, who shall live when God does this?
24 Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu; kupondereza Asuri ndi Eberi, koma iwonso adzawonongeka.”
But ships shall come from the coast of Kittim, and they shall afflict Asshur, and shall afflict Eber, and he also shall come to destruction.
25 Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.
And Balaam rose up, and went and returned to his place, and Balak also went his way.

< Numeri 24 >