< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
Now Korah, the son of Izhar, the son of Kohath, the son of Levi, with Dathan and Abiram, the sons of Eliab, and On, the son of Peleth, sons of Reuben, took,
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
and they rose up before Moses, with certain of the sons of Israel, two hundred and fifty rulers of the congregation, called to the assembly, men of renown,
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
and they assembled themselves together against Moses and against Aaron, and said to them, Ye take too much upon you, since all the congregation are holy, every one of them, and Jehovah is among them. Why then do ye lift up yourselves above the assembly of Jehovah?
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
And when Moses heard it, he fell upon his face.
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
And he spoke to Korah and to all his company, saying, In the morning Jehovah will show who are his, and who is holy, and will cause him to come near to him, even him whom he shall choose will he cause to come near to him.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
This do: Take you censers, Korah, and all his company,
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
and put fire in them, and put incense upon them before Jehovah tomorrow. And it shall be that the man whom Jehovah chooses, he is holy. Ye take too much upon you, ye sons of Levi.
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
And Moses said to Korah, Hear now, ye sons of Levi.
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
Is it a small thing to you, that the God of Israel has separated you from the congregation of Israel, to bring you near to himself, to do the service of the tabernacle of Jehovah, and to stand before the congregation to minister to them,
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
and that he has brought thee near, and all thy brothers the sons of Levi with thee? And ye seek the priesthood also?
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Therefore thou and all thy company are gathered together against Jehovah. And Aaron, what is he that ye murmur against him?
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
And Moses sent to call Dathan and Abiram, the sons of Eliab. And they said, We will not come up.
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
Is it a small thing that thou have brought us up out of a land flowing with milk and honey, to kill us in the wilderness, but thou must make thyself also a ruler over us?
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
Moreover thou have not brought us into a land flowing with milk and honey, nor given us inheritance of fields and vineyards. Will thou put out the eyes of these men? We will not come up.
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
And Moses was very angry, and said to Jehovah, Do not respect thou their offering. I have not taken one donkey from them, neither have I hurt one of them.
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
And Moses said to Korah, Be thou and all thy company before Jehovah, thou, and they, and Aaron, tomorrow.
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
And take ye every man his censer, and put incense upon them, and bring ye before Jehovah every man his censer, two hundred and fifty censers, thou also, and Aaron, each his censer.
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
And they took every man his censer, and put fire in them, and laid incense on it, and stood at the door of the tent of meeting with Moses and Aaron.
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
And Korah assembled all the congregation against them to the door of the tent of meeting. And the glory of Jehovah appeared to all the congregation.
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
And Jehovah spoke to Moses and to Aaron, saying,
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
Separate yourselves from among this congregation, that I may consume them in a moment.
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
And they fell upon their faces, and said, O God, the God of the spirits of all flesh, shall one man sin, and will thou be angry with all the congregation?
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
Speak to the congregation, saying, Get you up from about the tabernacle of Korah, Dathan, and Abiram.
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
And Moses rose up and went to Dathan and Abiram, and the elders of Israel followed him.
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
And he spoke to the congregation, saying, Depart, I pray you, from the tents of these wicked men, and touch nothing of theirs, lest ye be consumed in all their sins.
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
So they got up from the tabernacle of Korah, Dathan, and Abiram, on every side. And Dathan and Abiram came out, and stood at the door of their tents, and their wives, and their sons, and their little ones.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
And Moses said, Hereby ye shall know that Jehovah has sent me to do all these works, for it is not of my own mind.
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
If these men die the common death of all men, or if they be visited after the visitation of all men, then Jehovah has not sent me.
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
But if Jehovah makes a new thing, and the ground opens its mouth, and swallows them up, with all that pertains to them, and they go down alive into Sheol, then ye shall understand that these men have despised Jehovah. (Sheol h7585)
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
And it came to pass, as he made an end of speaking all these words, that the ground split asunder that was under them,
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
and the earth opened its mouth, and swallowed them up, and their households, and all the men that pertained to Korah, and all their goods.
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
So they, and all that pertained to them, went down alive into Sheol. And the earth closed upon them, and they perished from among the assembly. (Sheol h7585)
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
And all Israel that were round about them fled at the cry of them, for they said, Lest the earth swallow us up.
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
And fire came forth from Jehovah, and devoured the two hundred and fifty men who offered the incense.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
Speak to Eleazar the son of Aaron the priest, that he take up the censers out of the burning, and scatter thou the fire yonder, for they are holy,
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
even the censers of these sinners against their own lives, and let them be made beaten plates for a covering of the altar, for they offered them before Jehovah, therefore they are holy, and they shall be a sign to the sons of Israel.
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
And Eleazar the priest took the brazen censers, which those who were burnt had offered, and they beat them out for a covering of the altar,
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
to be a memorial to the sons of Israel, to the end that no stranger, who is not of the seed of Aaron, come near to burn incense before Jehovah, that he not be as Korah, and as his company, as Jehovah spoke to him by Moses.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
But on the morrow all the congregation of the sons of Israel murmured against Moses and against Aaron, saying, Ye have killed the people of Jehovah.
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
And it came to pass, when the congregation was assembled against Moses and against Aaron, that they looked toward the tent of meeting, and, behold, the cloud covered it, and the glory of Jehovah appeared.
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
And Moses and Aaron came to the front of the tent of meeting.
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
Get you up from among this congregation, that I may consume them in a moment. And they fell upon their faces.
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
And Moses said to Aaron, Take thy censer, and put fire in it from off the altar, and lay incense on it, and carry it quickly to the congregation, and make atonement for them, for there is wrath gone out from Jehovah. The plague has begun.
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
And Aaron took as Moses spoke, and ran into the midst of the assembly. And, behold, the plague had begun among the people. And he put on the incense, and made atonement for the people.
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
And he stood between the dead and the living, and the plague was stopped.
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
Now those who died by the plague were fourteen thousand and seven hundred, besides those who died about the matter of Korah.
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
And Aaron returned to Moses to the door of the tent of meeting, and the plague was stopped.

< Numeri 16 >