< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
Men Kora, en Søn af Jizhar, en Søn af Levis Søn Kehat, og Datan og Abiram, Sønner af Eliab, en Søn af Rubens Søn Pallu, gjorde Oprør.
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
De gjorde Oprør mod Moses sammen med 250 israelitiske Mænd, Øverster for Menigheden, udvalgte i Folkeforsamlingen, ansete Mænd.
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
Og de samlede sig og traadte op imod Moses og Aron og sagde til dem: »Lad det nu være nok, thi hele Menigheden er hellig, hver og en, og HERREN er i dens Midte; hvorfor vil I da ophøje eder over HERRENS Forsamling?«
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
Da Moses hørte det, faldt han paa sit Ansigt.
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
Derpaa talte han til Kora og alle hans Tilhængere og sagde: »Vent til i Morgen, saa vil HERREN give til kende, hvem der tilhører ham, og hvem der er hellig, saa at han vil give ham Adgang til sig; den, han udvælger, vil han give Adgang til sig.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
Saaledes skal I gøre: Skaf eder Pander, du Kora og alle dine Tilhængere,
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
og læg saa i Morgen Gløder paa og kom Røgelse paa for HERRENS Aasyn, saa skal den, HERREN udvælger, være den, som er hellig; lad det nu være nok, I Levisønner!«
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
Fremdeles sagde Moses til Kora: »Hør nu, I Levisønner!
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
Er det eder ikke nok, at Israels Gud har udskilt eder af Israels Menighed og givet eder Adgang til sig for at udføre Arbejdet ved HERRENS Bolig og staa til Tjeneste for Menigheden?
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
Han har givet dig og med dig alle dine Brødre, Levis Sønner, Adgang til sig og nu attraar I ogsaa Præsteværdigheden!
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Derfor, du og alle dine Tilhængere, som har rottet eder sammen mod HERREN, hvad er Aron, at I vil knurre mod ham!«
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
Da sendte Moses Bud efter Datan og Abiram, Eliabs Sønner, men de sagde: »Vi kommer ikke!
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
Er det ikke nok, at du har ført os bort fra et Land, der flyder med Mælk og Honning, for at lade os dø i Ørkenen, siden du oven i Købet vil opkaste dig til Herre over os!
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
Du har sandelig ikke ført os til et Land, der flyder med Mælk og Honning, eller givet os Marker og Vinbjerge! Tror du, du kan stikke disse Mænd Blaar i Øjnene? Vi kommer ikke!«
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
Da harmedes Moses højlig og sagde til HERREN: »Vend dig ikke til deres Offergave! Ikke saa meget som et Æsel har jeg frataget dem, ej heller har jeg gjort en eneste af dem noget ondt!«
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
Og Moses sagde til Kora: »I Morgen skal du og alle dine Tilhængere komme frem for HERRENS Aasyn sammen med Aron;
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
og enhver af eder skal tage sin Pande, lægge Gløder paa og komme Røgelse paa og frembære sin Pande for HERRENS Aasyn, 250 Pander, du selv og Aron skal ogsaa tage hver sin Pande!«
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
Da tog hver sin Pande, lagde Gløder paa og kom Røgelse paa, og saa stillede de sig ved Indgangen til Aabenbaringsteltet sammen med Moses og Aron;
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
og Kora kaldte hele Menigheden sammen imod dem ved Indgangen til Aabenbaringsteltet. Da kom HERRENS Herlighed til Syne for hele Menigheden,
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
og HERREN talede til Moses og Aron og sagde:
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
»Skil eder ud fra denne Menighed, saa vil jeg i et Nu tilintetgøre den!«
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
Men de faldt paa deres Ansigt og sagde: »O Gud, du Gud over alt Køds Aander, vil du vredes paa hele Menigheden, fordi en enkelt Mand synder?«
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
Da talede HERREN til Moses og sagde:
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
»Tal til Menigheden og sig: Fjern eder fra Pladsen omkring Koras, Datans og Abirams Bolig!«
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
Moses gik nu hen til Datan og Abiram, fulgt af Israels Ældste,
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
og han talte til Menigheden og sagde: »Træk eder tilbage fra disse ugudelige Mænds Telte og rør ikke ved noget af, hvad der tilhører dem, for at I ikke skal rives bort for alle deres Synders Skyld!«
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
Da fjernede de sig fra Pladsen om Koras, Datans og Abirams Bolig, og Datan og Abiram kom ud og stillede sig ved Indgangen til deres Telte med deres Hustruer og Børn, store og smaa.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
Og Moses sagde: »Derpaa skal I kende, at HERREN har sendt mig for at gøre alle disse Gerninger, og at jeg ikke handler i Egenraadighed:
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
Dersom disse dør paa vanlig menneskelig Vis, og der ikke rammer dem andet, end hvad der rammer alle andre, saa har HERREN ikke sendt mig;
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
men hvis HERREN lader noget uhørt ske, saa Jorden spiler sit Gab op og sluger dem med alt, hvad der tilhører dem, saa de farer levende ned i Dødsriget, da skal I derpaa kende, at disse Mænd har haanet HERREN!« (Sheol h7585)
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
Og straks, da han havde talt alle disse Ord, aabnede Jorden sig under dem,
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
og Jorden lukkede sit Gab op og slugte dem og deres Boliger og alle Mennesker, der tilhørte Kora, og alt, hvad de ejede;
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
og de for levende ned i Dødsriget med alt, hvad der tilhørte dem, og Jorden lukkede sig over dem, og de blev udryddet af Forsamlingen. (Sheol h7585)
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
Men hele Israel, der stod omkring dem, flygtede ved deres Skrig, thi de sagde: »Blot ikke Jorden skal opsluge os!«
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
Og Ild for ud fra HERREN og fortærede de 250 Mænd, der frembar Røgelse.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
Da talede HERREN til Moses og sagde:
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
»Sig til Eleazar, Præsten Arons Søn, at han skal tage Panderne ud af Branden og strø Gløderne ud noget derfra; thi hellige
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
er de Pander, der tilhørte disse Mænd, som begik en Synd, der kostede dem Livet. De skal udhamre dem til Plader til Overtræk paa Alteret, thi de frembar dem for HERRENS Aasyn, og derfor er de hellige; de skal nu tjene Israeliterne til Tegn.«
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
Da tog Præsten Eleazar Kobberpanderne, som de opbrændte Mænd havde frembaaret, og hamrede dem ud til. Overtræk paa Alteret
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
som et Mindetegn for Israeliterne om, at ingen Lægmand, ingen, som ikke hører til Arons Efterkommere, maa træde frem for at ofre Røgelse for HERRENS Aasyn, for at det ikke skal gaa ham som Kora og hans Tilhængere, saaledes som HERREN havde sagt ham ved Moses.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
Men Dagen efter knurrede hele Israels Menighed mod Moses og Aron og sagde: »Det er eder, der har, dræbt HERRENS Folk!«
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
Men da Menigheden samlede sig mod Moses og Aron, vendte de sig mod Aabenbaringsteltet, og se, Skyen dækkede det, og HERRENS Herlighed kom til Syne.
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
Da traadte Moses og Aron hen foran Aabenbaringsteltet,
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
og HERREN talede til Moses og Aron og sagde:
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
»Fjern eder fra denne Menighed, saa vil jeg i et Nu tilintetgøre dem!« Da faldt de paa deres Ansigt,
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
og Moses sagde til Aron: »Tag din Pande, læg Gløder fra Alteret paa og kom Røgelse paa og skynd dig saa hen til Menigheden og skaf den Soning, thi Vreden er brudt frem fra HERREN, Plagen har allerede taget fat!«
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
Da tog Aron det, saaledes som Moses havde sagt, og løb midt ind i Forsamlingen. Og se, Plagen havde allerede taget fat blandt Folket, men han kom Røgelsen paa og skaffede Folket Soning.
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
Og som han stod der midt imellem døde og levende, hørte Plagen op.
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
Men de, der omkom ved Plagen, udgjorde 14 700 Mennesker foruden dem, der omkom for Koras Skyld.
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
Saa vendte Aron tilbage til Moses ved Indgangen til Aabenbaringsteltet, efter at Plagen var ophørt.

< Numeri 16 >