< Numeri 12 >

1 Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
Miriam et Aaron parlèrent contre Moïse à cause de la femme de Cuschi qu'il avait épousée, car il avait épousé une femme de Cuschi.
2 Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
Ils dirent: « Yahvé n'a-t-il parlé qu'à Moïse? N'a-t-il pas parlé aussi avec nous? » Et Yahvé les entendit.
3 (Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
Or, l'homme Moïse était très humble, plus que tous les hommes qui étaient à la surface de la terre.
4 Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
Yahvé parla soudain à Moïse, à Aaron et à Miriam: « Vous trois, sortez de la tente de la Rencontre! » Ils sortirent tous les trois.
5 Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
Yahvé descendit dans une colonne de nuée et se tint à l'entrée de la Tente. Il appela Aaron et Miriam, qui s'avancèrent tous deux.
6 Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
Il dit: « Écoutez maintenant mes paroles. S'il y a un prophète parmi vous, moi, Yahvé, je me ferai connaître à lui dans une vision. Je lui parlerai en songe.
7 Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
Ce n'est pas le cas de mon serviteur Moïse. Il est fidèle dans toute ma maison.
8 Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
Avec lui, je parlerai bouche à bouche, en clair et non en énigmes, et il verra la forme de Yahvé. Pourquoi donc n'avez-vous pas craint de parler contre mon serviteur, contre Moïse? ».
9 Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
La colère de Yahvé s'enflamma contre eux, et il s'en alla.
10 Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
La nuée se retira de dessus la tente; et voici, Miriam était lépreuse, blanche comme la neige. Aaron regarda Miriam, et voici qu'elle était lépreuse.
11 ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
Aaron dit à Moïse: « Oh, mon seigneur, ne nous compte pas ce péché, dans lequel nous avons fait des folies et dans lequel nous avons péché.
12 Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
Qu'elle ne soit pas, je t'en prie, comme un mort dont la chair est à moitié consumée lorsqu'il sort du ventre de sa mère. »
13 Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
Moïse cria à Yahvé en disant: « Guéris-la, Dieu, je t'en supplie! »
14 Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
Yahvé dit à Moïse: « Si son père lui a craché au visage, ne devrait-elle pas avoir honte pendant sept jours? Qu'elle soit enfermée hors du camp pendant sept jours, et après cela elle sera ramenée. »
15 Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
Miriam fut enfermée hors du camp pendant sept jours, et le peuple ne voyagea pas jusqu'à ce que Miriam ait été ramenée.
16 Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.
Ensuite, le peuple partit de Hatséroth et campa dans le désert de Paran.

< Numeri 12 >