< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Et l’Éternel parla à Moïse, au désert de Sinaï, dans la tente d’assignation, le premier [jour] du second mois de la seconde année après leur sortie du pays d’Égypte, disant:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Relevez la somme de toute l’assemblée des fils d’Israël, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, tous les mâles, par tête:
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux d’Israël qui sont propres au service militaire, vous les compterez selon leurs armées, toi et Aaron.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
Et, avec vous, il y aura un homme par tribu, un homme chef de sa maison de pères.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Et ce sont ici les noms des hommes qui se tiendront avec vous: pour Ruben, Élitsur, fils de Shedéur;
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
pour Siméon, Shelumiel, fils de Tsurishaddaï;
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
pour Juda, Nakhshon, fils d’Amminadab;
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
pour Issacar, Nethaneël, fils de Tsuar;
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
pour Zabulon, Éliab, fils de Hélon;
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
pour les fils de Joseph, pour Éphraïm, Élishama, fils d’Ammihud; pour Manassé, Gameliel, fils de Pedahtsur;
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
pour Benjamin, Abidan, fils de Guidhoni;
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
pour Dan, Akhiézer, fils d’Ammishaddaï;
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
pour Aser, Paghiel, fils d’Ocran;
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
pour Gad, Éliasaph, fils de Dehuel;
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
pour Nephthali, Akhira, fils d’Énan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Ce sont là ceux qui furent les principaux de l’assemblée, les princes des tribus de leurs pères, les chefs des milliers d’Israël.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Et Moïse et Aaron prirent ces hommes-là, qui avaient été désignés par leurs noms,
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
et ils réunirent toute l’assemblée, le premier [jour] du second mois; et chacun déclara sa filiation, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, par tête.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
Comme l’Éternel l’avait commandé à Moïse, ainsi il les dénombra dans le désert de Sinaï.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Et les fils de Ruben, premier-né d’Israël, leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, par tête, tous les mâles, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Ruben furent 46 500.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Siméon: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, ceux qui furent dénombrés suivant le nombre des noms, par tête, tous les mâles, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Siméon furent 59 300.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Gad: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Gad furent 45 650.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Juda: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Juda furent 74 600.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils d’Issacar: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
ceux qui furent dénombrés de la tribu d’Issacar furent 54 400.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Zabulon: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Zabulon furent 57 400.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Joseph, des fils d’Éphraïm: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
ceux qui furent dénombrés de la tribu d’Éphraïm furent 40 500.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Manassé: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Manassé furent 32 200.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Benjamin: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Benjamin furent 35 400.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Dan: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Dan furent 62 700.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils d’Aser: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
ceux qui furent dénombrés de la tribu d’Aser furent 41 500.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Nephthali: leurs générations, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, suivant le nombre des noms, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
ceux qui furent dénombrés de la tribu de Nephthali furent 53 400.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Ce sont là les dénombrés que Moïse et Aaron et les douze hommes, princes d’Israël, dénombrèrent: il y avait un homme pour chaque maison de pères.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
Et tous les dénombrés des fils d’Israël, selon leurs maisons de pères, depuis l’âge de 20 ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres au service militaire en Israël,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
tous les dénombrés, furent 603 550.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Mais les Lévites, selon la tribu de leurs pères, ne furent pas dénombrés parmi eux.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
Car l’Éternel avait parlé à Moïse, disant:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Seulement, tu ne dénombreras pas la tribu de Lévi et tu n’en relèveras pas la somme parmi les fils d’Israël.
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
Et toi, tu préposeras les Lévites sur le tabernacle du témoignage, et sur tous ses ustensiles, et sur tout ce qui lui appartient: ce seront eux qui porteront le tabernacle et tous ses ustensiles; ils en feront le service, et camperont autour du tabernacle;
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
et quand le tabernacle partira, les Lévites le démonteront, et quand le tabernacle campera, les Lévites le dresseront; et l’étranger qui en approchera sera mis à mort.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Et les fils d’Israël camperont chacun dans son camp, et chacun près de sa bannière, selon leurs armées.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Et les Lévites camperont autour du tabernacle du témoignage, afin qu’il n’y ait point de colère sur l’assemblée des fils d’Israël; et les Lévites auront la garde du tabernacle du témoignage.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Et les fils d’Israël firent selon tout ce que l’Éternel avait commandé à Moïse; ils firent ainsi.

< Numeri 1 >