< Nehemiya 13 >

1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
Onegoż dnia czytano w księgach Mojżeszowych, tak, iż lud słyszał. I znaleziono w nich napisane, że nie miał wchodzić Ammonitczyk i Moabczyk do zgromadzenia Bożego, aż na wieki;
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
Przeto, iż nie zaszli synom Izraelskim z chlebem i z wodą; owszem najęli przeciwko nim Balaama, aby ich przeklinał; ale obrócił Bóg nasz ono przeklęstwo w błogosławieństwo.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
A gdy usłyszeli zakon, odłączyli wszystek lud pospolity od Izraela.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
Ale się przedtem Elijasyb kapłan, przełożony nad skarbnicą domu Boga naszego, spowinowacił z Tobijaszem;
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
I zbudował mu gmach wielki, kędy przedtem odkładano dary, kadzidło, i naczynia, i dziesięciny zboża, moszczu, i oliwy świeżej, opatrzenie Lewitom, i śpiewakom, i odźwiernym, także ofiary podnoszone kapłańskie.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
Ale przy tem wszystkiem nie byłem w Jeruzalemie; albowiem roku trzydziestego i wtórego Artakserksesa, króla Babilońskiego, przyszedłem do króla, a po wyjściu kilku lat uprosiłem się u króla.
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
A gdym przyszedł do Jeruzalemu, wyrozumiałem to złe, które uczynił Elijasyb kwoli Tobijaszowi, iż mu zbudował gmach w sieniach domu Bożego.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
Co mi się bardzo nie podobało: przetoż wyrzuciłem wszystkie naczynia domu Tobijaszowego precz z onegoż gmachu;
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
I rozkazałem oczyścić one gmachy, i wniosłem tam zaś nacznia domu Bożego, dary i kadzidło.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
Nadtom się dowiedział, że działy Lewitom nie były oddawane, a iż się Lewitowie i śpiewacy, którzy pilnowali pracy, rozbiegli, każdy do roli swojej.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
Przetoż zgromiłem przełożonych, mówiąc: Przeczże opuszczamy dom Boży? A tak zebrawszy ich, postawiłem ich na miejscach ich.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
A wszystek Juda przynosili dziesięciny zboża, i moszczu, i świeżej oliwy do skarbu.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
I postanowiłem podskarbich nad skarbmi: Selemijasza kapłana, i Sadoka nauczonego w Piśmie, i Fadajasza z Lewitów, a przy nich Hanana, syna Zachurowego, syna Matanijaszowego, bo ich za wiernych miano; a ich powinność była, działy rozdawać braciom swym.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Wspomnij na mię o Boże mój! dla tego, a nie wymazuj dobroczynności moich, którem czynił przy domu Boga mego, i przy obrzędach jego.
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
W oneż dni widziałem w Judzie tłoczących prasy w sabat, i noszących snopy, które kładli na osły, także i winne grona, i figi, i wszelki ciężar, a przynoszących do Jeruzalemu w dzień sabatu, i zgromiłem ich onegoż dnia, którego sprzedawali żywność.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
Także Tyryjczycy, którzy mieszkali w niem, przynosili ryby, i rozmaite towary, a sprzedawali w sabat synom Judy, i w Jeruzalemie.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Przetożem zgromił przełożonych w Judzie, mówiąc do nich: Cóż to jest za nieprawość, której się dopuszczacie, gwałcąc dzień sabatu?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Izali nie toż czynili ojcowie wasi, przez co Bóg nasz przywiódł na nas to wszystko złe, i na to miasto? A wy przyczyniacie gniewu na Izraela, gwałcąc sabat.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
A gdy okrył cień bramy Jeruzalemskie przed sabatem, rozkazałem zamknąć wrota, i nie kazałem ich otwierać, aż po sabacie; a niektórych z sług moich postawiłem w bramach, żeby nie wnoszono żadnych brzemion w dzień sabatu.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
Przetoż zostali przez noc kupcy, i sprzedawający towary rozmaite przed miastem Jeruzalemskiem, raz i drugi.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
Przeciwko którym oświadczyłem się, i rzekłem do nich: Przecz wy zostawacie przez noc za murem? Uczynicieli to więcej, ściągnę rękę na was. A tak od onego czasu nie przychodzili w sabat.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
I rozkazałem Lewitom, aby się oczyścili, a przyszedłszy strzegli bram, i święcili dzień sabatu. I dlatego wspomnij na mię, o Boże mój! a bądź mi miłościw według obfitości miłosierdzia twego.
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
W tychże dniach ujrzałem też Żydów, którzy sobie pojęli żony Azotyckie, Ammonickie, Moabskie.
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
A synowie ich na poły mówili po azotycku, nie umiejąc mówić po żydowsku, ale według języka swego narodu.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
Przetożem ich zgromił, i przeklinałem ich, i biłem niektórych z nich, a rwałem ich za włosy, i poprzysiągłem ich przez Boga, aby nie dawali córek swoich synom ich, ani brali córek ich synom swym i sobie.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
Izaliż nie przez to zgrzeszył Salomon, król Izraelski? choć między wieloma narodami nie było króla jemu podobnego, który był miły Bogu swemu, tak, że go Bóg postanowił królem, nad wszystkim Izraelem, przecież i tego przywiodły niewiasty cudzoziemskie do grzechu.
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
A wam izali pozwolimy, żebyście się dopuszczali tej wielkiej złości, a występowali przeciwko Bogu naszemu pojmując żony cudzoziemskie?
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
Lecz jeden z synów Jojady, syna Elijasyba, kapłana najwyższego, był zięciem Sanballata Horończyka, i wygnałem go od siebie.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Wspomnijże na to, o Boże mój! przeciw tym, którzy plugawią kapłaństwo, i umowę kapłańską i Lewitską.
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
Przetożem ich oczyścił od wszelkiego cudzoziemca, i postanowiłem porządki kapłanom i Lewitom, każdemu w pracy jego,
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
I ku noszeniu drew do ofiar, czasów postanowionych, także i pierwocin. Wspomnijże na mię, Boże mój! ku dobremu.

< Nehemiya 13 >