< Nehemiya 10 >

1 Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
Now, upon the sealed writings, were, —Nehemiah the governor, son of Hacaliah, and Zedekiah;
2 Seraya, Azariya, Yeremiya
Seraiah, Azariah, Jeremiah;
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
Pashhur, Amariah, Malchijah;
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Hattush, Shebaniah, Malluch;
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
Harim, Meremoth, Obadiah;
6 Danieli, Ginetoni, Baruki,
Daniel, Ginnethon, Baruch;
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini
Meshullam, Abijah, Mijamin;
8 Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
Maaziah, Bilgai, Shemaiah, —these, were, the priests.
9 Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
And, the Levites, —Jeshua, son of Azaniah, Binnui, of the sons of Henadad, Kadmiel;
10 ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
and, their brethren, —Shebaniah, Hodiah, Kelita, Pelaiah, Hanan;
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
Mica, Rehob, Hashabiah;
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
Zaccur, Sherebiah, Shebaniah;
13 Hodiya, Bani ndi Beninu.
Hodiah, Bani, Beninu.
14 Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
The heads of the people, —Parosh, Pahath-moab, Elam, Zattu, Bani;
15 Buni, Azigadi, Bebai,
Bunni, Azgad, Bebai;
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
Adonijah, Bigvai, Adin;
17 Ateri, Hezekiya, Azuri,
Ater, Hezekiah, Azzur;
18 Hodiya, Hasumu, Bezayi
Hodiah, Hashum, Bezai;
19 Harifu, Anatoti, Nebayi,
Hariph, Anathoth, Nobai;
20 Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
Magpiash, Meshullam, Hezir;
21 Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Meshezabel, Zadok, Jaddua;
22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Pelatiah, Hanan, Anaiah;
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu
Hoshea, Hananiah, Hasshub;
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
Hallohesh, Pilha, Shobek;
25 Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Rehum, Hashabnah, Maaseiah;
26 Ahiya, Hanani, Anani,
and Ahiah, Hanan, Anan;
27 Maluki, Harimu ndi Baana.
Malluch, Harim, Baanah.
28 Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
And, the rest of the people—the priests, the Levites, the doorkeepers, the singers, the Nethinim, and all who had separated themselves from the peoples of the lands unto the law of God, their wives, their sons and their daughters, —every one having knowledge and understanding,
29 tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
were holding fast unto their distinguished brethren, and were entering into a curse and into an oath, to walk in the law of God, which was given through Moses the servant of God, —and to observe and do, all the commandments of Yahweh our Lord, and his regulations, and his statutes;
30 “Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
and that we would not give our daughters unto the peoples of the land, —and, their daughters, would we not take for our sons;
31 “Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
and, if the peoples of the land should be bringing in wares, or any corn on the sabbath day, to sell, we would not buy of them on the sabbath, or on a holy day, —and that we would remit the seventh year, and the loan of every hand.
32 “Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
And we laid on ourselves charges, appointing for ourselves the third of a shekel, yearly, —for the service of the house of our God:
33 Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
for the bread to set in array, and the continual meal-offering, and for the continual ascending-sacrifice, of the sabbaths, of the new moons, for the appointed feasts, and for things hallowed, and for victims bearing sin, to put a propitiatory-covering over Israel, —and for all the work of the house of our God.
34 “Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
Also, lots, did we cast, concerning the offering of wood among the priests, the Levites, and the people, to bring it unto the house of our God, by our ancestral houses, at times arranged, year by year, —to burn upon the altar of Yahweh our God, as it is written in the law.
35 “Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
And that we would bring in the firstfruits of our ground, and the firstfruit of all fruit of all trees, year by year, —unto the house of Yahweh;
36 “Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
also that, the firstborn of our sons, and of our cattle, as it is written in the law, —and the firstlings of our herds and of our flocks, we would bring in unto the house of our God, unto the priests who should be in attendance in the house of our God;
37 “Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
and, the first part of our meal and our heave-offerings and the fruit of all trees, new wine and oil, would we bring in unto the priests, into the chambers of the house of our God, and the tithe of our ground unto the Levites, —the Levites themselves, taking the tithes in all our cities of agriculture.
38 Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
And the priest the son of Aaron should be with the Levites, when the Levites should take the tithes, —and the Levites, should bring up the tithe of the tithe, unto the house of our God, into the chambers pertaining unto the treasure-house.
39 Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”
For, into the chambers, should the sons of Israel and the sons of Levi bring in the heave-offering of the corn, the new wine and the oil, since, there, are the utensils of the sanctuary, and the priests who are in attendance, and the doorkeepers, and the singers, —so would we not neglect the house of our God.

< Nehemiya 10 >