< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
У, люте мне! Понеже бых аки собираяй сламу на жатве, и яко пародок во оымании винограда не сущу гроздию, еже ясти первоплодная, яже вожделе душа моя.
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
У, люте мне, душе! Яко погибе благочестивый от земли, и исправляющаго в человецех несть: вси во кровех прятся, кийждо ближняго своего озлобляет озлоблением,
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
на зло руки своя уготовляют: князь просит, и судия мирная словеса глаголет, желание души его есть: и отиму благая их,
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
яко моль поядаяй, и ходяй по правилам в день стражбы. У, люте! У, люте! Отмщения Твоя приспеша, ныне будут плачы их.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Не верите другом, ни надейтеся на старейшины, и от сожителницы твоея хранися, еже сказати ей что:
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
понеже сын безчестит отца, дщерь востанет на матерь свою и невеста на свекровь свою, врази вси мужу домашнии его.
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
Аз же ко Господеви воззрю, потерплю Бога спаса моего, услышит мя Бог мой.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Не радуйся о мне, враждебница моя, яко падох, и востану: зане аще сяду во тме, Господь осветит мя.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
Гнев Господень стерплю, яко согреших Ему, дондеже оправдит прю мою и сотворит суд мой: и изведет мя на свет, и узрю правду Его.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
И узрит враждебница моя, и облечется в студ глаголющая ко мне: где есть Господь Бог твой? Очи мои воззрят на ню, ныне будет в попрание аки кал на путех.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
День глаждения плинфа: изглаждение твое день оный, и сотрет законы твоя день оный.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
И гради твои приидут на поравнение и в разделение Ассирийско, и гради твои твердии в разделение от Тира даже до реки Сирския, и от моря даже до моря, и от горы даже до горы, дние воды и молвы.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
И будет земля в пагубу со живущими на ней, от плодов начинаний их.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
Паси люди Твоя жезлом Твоим, овцы наследия Твоего, вселяющыяся едины в дубраве среде Кармила, попасут Васанитиду и Галаадитиду, якоже дние века.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
И по днем исхода твоего из Египта узрите чудесная.
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
Узрят языцы и усрамятся от всея крепости своея, руце возложат на уста своя, и уши их оглохнут,
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
полижут персть яко змиеве плежуще по земли, смятутся во облежении своем: о Господе Бозе нашем ужаснутся и убоятся от Тебе.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
Кто Бог якоже Ты, отемляй беззакония и оставляяй нечестия останком наследия Своего? И не удержа гнева Своего во свидение, яко Волитель милости есть.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
Той обратит и ущедрит ны, и погрузит неправды нашя и ввержет в глубины морския вся грехи нашя,
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
даст истину Иакову, (и) милость Аврааму, якоже клялся еси отцем нашым во дни первыя.

< Mika 7 >