< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Hear ye now what Jehovah says: Arise, contend thou before the mountains, and let the hills hear thy voice.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Hear, O ye mountains, Jehovah's controversy, and ye enduring foundations of the earth, for Jehovah has a controversy with his people, and he will contend with Israel.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
O my people, what have I done to thee? And in what have I wearied thee? Testify against me.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
For I brought thee up out of the land of Egypt, and redeemed thee out of the house of bondage. And I sent before thee Moses, Aaron, and Miriam.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
O my people, remember now what Balak king of Moab devised, and what Balaam the son of Beor answered him. Remember from Shittim to Gilgal, that ye may know the righteous acts of Jehovah.
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
With what shall I come before Jehovah, and bow myself before the high God? Shall I come before him with burnt offerings, with calves a year old?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Will Jehovah be pleased with thousands of rams, or with ten thousand rivers of oil? Shall I give my firstborn for my transgression, the fruit of my body for the sin of my soul?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
He has shown thee, O man, what is good. And what does Jehovah require of thee, but to do justly, and to love kindness, and to walk humbly with thy God?
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
The voice of Jehovah cries to the city, and the man of wisdom will see thy name. Hear ye the rod, and who has appointed it.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Are there yet treasures of wickedness in the house of the wicked, and a scant measure that is abominable?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Shall I be pure with wicked balances, and with a bag of deceitful weights?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
For the rich men of it are full of violence, and the inhabitants of it have spoken lies, and their tongue is deceitful in their mouth.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
Therefore I also have smitten thee with a grievous wound, I have made thee desolate because of thy sins.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Thou shall eat, but not be satisfied, and thy humiliation shall be in the midst of thee. And thou shall put away, but shall not save, and that which thou save I will give up to the sword.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Thou shall sow, but shall not reap, thou shall tread the olives, but shall not anoint thee with oil, and the vintage, but shall not drink the wine.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
For the statutes of Omri are kept, and all the works of the house of Ahab, and ye walk in their counsels, that I may make thee a desolation, and the inhabitants thereof a hissing. And ye shall bear the reproach of my people.

< Mika 6 >