< Mika 5 >

1 Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
Now you shall gather yourself in troops, daughter of troops. He has laid siege against us. They will strike the judge of Israel with a rod on the cheek.
2 “Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
But you, Bethlehem Ephrathah, being small among the clans of Judah, out of you one will come forth to me that is to be ruler in Israel; whose goings forth are from of old, from everlasting.
3 Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
Therefore he will abandon them until the time that she who is in labor gives birth. Then the rest of his brothers will return to the children of Israel.
4 Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
He shall stand, and shall shepherd in the strength of the LORD, in the majesty of the name of the LORD his God: and they will live, for then he will be great to the farthest parts of the earth.
5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
He will be our peace when Assyria invades our land, and when he marches through our fortresses, then we will raise against him seven shepherds, and eight leaders of men.
6 Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
They will rule the land of Assyria with the sword, and the land of Nimrod with the drawn sword. He will deliver us from the Assyrian, when he invades our land, and when he marches within our border.
7 Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
The remnant of Jacob will be in the midst of many peoples, like dew from the LORD, like showers on the grass, that do not wait for man, nor wait for the sons of men.
8 Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
The remnant of Jacob will be among the nations, in the midst of many peoples, like a lion among the animals of the forest, like a young lion among the flocks of sheep; who, if he goes through, treads down and tears in pieces, and there is no one to deliver.
9 Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
Let your hand be lifted up above your adversaries, and let all of your enemies be cut off.
10 Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
"It will happen in that day," says the LORD, "That I will cut off your horses out of the midst of you, and will destroy your chariots.
11 Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
I will cut off the cities of your land, and will tear down all your strongholds.
12 Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
I will destroy witchcraft from your hand; and you shall have no soothsayers.
13 Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
I will cut off your engraved images and your pillars out of your midst; and you shall no more worship the work of your hands.
14 Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
I will uproot your Asherim out of your midst; and I will destroy your cities.
15 Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”
I will execute vengeance in anger, and wrath on the nations that did not listen."

< Mika 5 >