< Mateyu 24 >

1 Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo.
Ла еширя дин Темплу, пе кынд мерӂя Исус, ученичий Луй с-ау апропият де Ел ка сэ-Й арате клэдириле Темплулуй.
2 Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Дар Исус ле-а зис: „Ведець вой тоате ачесте лукрурь? Адевэрат вэ спун кэ нува рэмыне аич пятрэ пе пятрэ каре сэ ну фие дэрыматэ.”
3 Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn g165)
Ел а шезут жос, пе Мунтеле Мэслинилор. Ши ученичий Луй ау венит ла Ел, ла о парте, ши Й-ау зис: „Спуне-не, кынд се вор ынтымпла ачесте лукрурь? Ши каре ва фи семнул венирий Тале ши ал сфыршитулуй вякулуй ачестуя?” (aiōn g165)
4 Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni.
Дрепт рэспунс, Исус ле-а зис: „Бэгаць де сямэсэ ну вэ ыншеле чинева.
5 Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri.
Фииндкэвор вени мулць ын Нумеле Меу ши вор зиче: ‘Еу сунт Христосул!’ Шивор ыншела пе мулць.
6 Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike.
Вець аузи де рэзбоае ши вешть де рэзбоае: ведець сэ ну вэ ынспэймынтаць, кэч тоате ачесте лукрурь требуе сэ се ынтымпле. Дар сфыршитул тот ну ва фи атунч.
7 Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.
Унням се ва скула ымпотрива алтуй ням, ши о ымпэрэцие, ымпотрива алтей ымпэрэций ши, пе алокурь, вор фи кутремуре де пэмынт, фоамете ши чумь.
8 Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.
Дар тоате ачесте лукрурь ну вор фи декыт ынчепутул дурерилор.
9 “Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine.
Атунчвэ вор да сэ фиць кинуиць ши вэ вор оморы; ши вець фи урыць де тоате нямуриле пентру Нумеле Меу.
10 Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake,
Атунч, мулць воркэдя, се вор винде уний пе алций ши се вор уры уний пе алций.
11 ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.
Се вор скула мулцьпророчь минчиношь ши ворыншела пе мулць.
12 Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,
Ши, дин причина ынмулцирий фэрэделеӂий, драгостя челор май мулць се ва рэчи.
13 koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.
Дарчине ва рэбда пынэ ла сфыршит ва фи мынтуит.
14 Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”
Евангелияачаста а Ымпэрэцией вафи проповэдуитэ ын тоатэ лумя, ка сэ служяскэ де мэртурие тутурор нямурилор. Атунч ва вени сфыршитул.
15 “Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire.
Де ачея, кынд вець ведя урычуня пустиирий, деспре каре а ворбит пророкул Даниел, ашезатэ ын Локул Сфынт – чине читеште сэ ынцелягэ! –
16 Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri.
атунч, чей че вор фи ын Иудея сэ фугэ ла мунць;
17 Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba.
чине ва фи пе акоперишул касей сэ ну се кобоаре сэ-шь я лукруриле дин касэ;
18 Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake.
ши чине ва фи ла кымп сэ ну се ынтоаркэ сэ-шь я хайна.
19 Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa!
Вайде фемеиле каре вор фи ынсэрчинате ши де челе че вор да цыцэ ын зилеле ачеля!
20 Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata.
Ругаци-вэ ка фуга воастрэ сэ ну фие ярна, нич ынтр-о зи де Сабат.
21 Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena.
Пентру кэатунч ва фи ун неказ аша де маре, кум н-а фост ничодатэ де ла ынчепутул лумий пынэ акум ши нич ну ва май фи.
22 Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa.
Ши дакэ зилеле ачеля н-ар фи фост скуртате, нимень н-ар скэпа; дар, дин причина челор алешь, зилеле ачеля вор фи скуртате.
23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire.
Атунч, дакэ вэ ва спуне чинева: ‘Ятэ, Христосул есте аич сау аколо!’, сэ ну-л кредець.
24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero.
Кэч севор скула христошь минчиношь ши пророчь минчиношь, вор фаче семне марь ши минунь, пынэ аколо ынкыт сэ ыншеле, дакэ ва фи ку путинцэ, кяр ши пе чей алешь.
25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
Ятэ кэ в-ам спус май динаинте.
26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire.
Деч, дакэ вэ вор зиче: ‘Ятэ-Л ын пустиу’, сэ ну вэ дучець аколо! ‘Ятэ-Л ын одэице аскунсе’, сэ ну кредець.
27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu.
Кэч, кум есе фулӂерул де ла рэсэрит ши се веде пынэ ла апус, аша ва фи ши вениря Фиулуй омулуй.
28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
Орьундева фи стырвул, аколо се вор адуна вултурий.
29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo, “‘dzuwa lidzadetsedwa, ndipo mwezi sudzawala; nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
Ындатэдупэ ачеле зиле де неказ, соареле сева ынтунека, луна ну-шь ва май да лумина ей, стелеле вор кэдя дин чер ши путериле черурилор вор фи клэтинате.
30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
Атунчсе ва арэта ын чер семнул Фиулуй омулуй, тоатесеминцииле пэмынтулуй се вор бочи шивор ведя пе Фиул омулуй венинд пе норий черулуй ку путере ши ку о маре славэ.
31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
Елва тримите пе ынӂерий Сэй ку трымбица рэсунэтоаре ши вор адуна пе алеший Луй дин челе патру вынтурь, де ла о марӂине а черурилор пынэ ла чялалтэ.
32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
Де ла смокин ынвэцаць пилдалуй: Кынд ый фрэӂезеште ши ынфрунзеште млэдица, штиць кэвара есте апроапе.
33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni.
Тот аша, ши вой, кынд вець ведя тоате ачесте лукрурь, сэ штиць кэ Фиул омулуй есте апроапе, есте кяр ла ушь.
34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika.
Адевэрат вэ спун кэ нува трече нямул ачеста пынэ се вор ынтымпла тоате ачесте лукрурь.
35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Черулши пэмынтул вор трече, дар кувинтеле Меле ну вор трече.
36 “Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha.
Деспре зиуа ачея ши деспре часул ачела, ну штие нимень: нич ынӂерий дин черурь, нич Фиул, чи нумайТатэл.
37 Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu.
Кум с-а ынтымплат ын зилеле луй Ное, аидома се ва ынтымпла ши ла вениря Фиулуй омулуй.
38 Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo;
Ын адевэр, кумера ын зилеле динаинте де потоп, кынд мынкау ши бяу, се ынсурау ши се мэритау пынэ ын зиуа кынд а интрат Ное ын корабие
39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu.
ши н-ау штиут нимик, пынэ кынд а венит потопул ши й-а луат пе тоць, тот аша ва фи ши ла вениря Фиулуй омулуй.
40 Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Атунч, дин дой бэрбаць каре вор фи ла кымп, унул ва фи луат ши алтул ва фи лэсат.
41 Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Дин доуэ фемей каре вор мэчина ла моарэ, уна ва фи луатэ ши алта ва фи лэсатэ.
42 “Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera.
Вегяць дар, пентру кэ ну штиць ын че зи ва вени Домнул востру.
43 Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
Сэ штицькэ, дакэ ар шти стэпынул касей ла че стражэ дин ноапте ва вени хоцул, ар вегя ши н-ар лэса сэ-й спаргэ каса.
44 Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.
Де ачея, ши вой фиць гата; кэч Фиул омулуй ва вени ын часул ын каре ну вэ гындиць.
45 “Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani?
Каре есте дечробул крединчос ши ынцелепт, пе каре л-а пус стэпынул сэу песте чата слуӂилор сале, ка сэ ле дя храна ла время хотэрытэ?
46 Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi.
Феричеде робул ачела пе каре стэпынул сэу, ла вениря луй, ыл ва гэси фэкынд аша!
47 Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
Адевэрат вэ спун кэыл ва пуне песте тоате авериле сале.
48 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’
Дар, дакэ есте ун роб рэу, каре зиче ын инима луй: ‘Стэпынул меу зэбовеште сэ винэ!’
49 nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa.
Дакэ ва ынчепе сэ батэ пе товарэший луй де службэ ши сэ мэнынче ши сэ бя ку бецивий,
50 Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa.
стэпынул робулуй ачелуя ва вени ын зиуа ын каре ел ну се аштяптэ ши ын часул пе каре ну-л штие,
51 Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
ыл ва тэя ын доуэ, ши соарта луй ва фи соарта фэцарничилор; аколовор фи плынсул ши скрышниря динцилор.

< Mateyu 24 >