< Marko 2 >

1 Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.
Quelques jours après, il entra de nouveau à Capernaüm, et l'on apprit qu'il était chez lui.
2 Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu.
Aussitôt, plusieurs se rassemblèrent, au point qu'il n'y avait plus de place, pas même autour de la porte; et il leur adressa la parole.
3 Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo.
Quatre personnes vinrent, lui portant un paralytique.
4 Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.
Comme ils ne pouvaient s'approcher de lui à cause de la foule, ils enlevèrent le toit où il se trouvait. Après l'avoir brisé, ils descendirent la natte sur laquelle était couché le paralytique.
5 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
Jésus, voyant leur foi, dit au paralytique: « Mon fils, tes péchés te sont pardonnés. »
6 Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti,
Mais quelques-uns des scribes, assis là, raisonnaient dans leur cœur:
7 “Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
« Pourquoi cet homme profère-t-il de tels blasphèmes? Qui peut pardonner les péchés, sinon Dieu seul? »
8 Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi?
Aussitôt, Jésus, voyant dans son esprit qu'ils raisonnaient ainsi en eux-mêmes, leur dit: « Pourquoi raisonnez-vous ainsi dans vos cœurs?
9 Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’
Lequel est le plus facile, de dire au paralytique: Tes péchés sont pardonnés, ou de lui dire: Lève-toi, prends ton lit et marche?
10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo,
Mais, afin que vous sachiez que le Fils de l'homme a sur la terre le pouvoir de pardonner les péchés, il dit au paralytique:
11 “Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.”
Je te le dis, lève-toi, prends ton lit et va dans ta maison.
12 Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
Il se leva, prit aussitôt le tapis et sortit devant eux tous, de sorte qu'ils furent tous stupéfaits et glorifièrent Dieu, en disant: « Nous n'avons jamais rien vu de tel! »
13 Yesu anatulukanso napita kumbali ya nyanja. Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye, ndipo anayamba kuliphunzitsa.
Il sortit de nouveau au bord de la mer. Toute la foule venait à lui, et il les enseignait.
14 Pamene ankayendabe, anaona Levi mwana wa Alufeyo atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anamuwuza kuti, “Tsate Ine.” Ndipo Levi anayimirira namutsata Iye.
Comme il passait, il vit Lévi, fils d'Alphée, assis au bureau des impôts. Il lui dit: « Suis-moi. » Et il se leva et le suivit.
15 Yesu atakalandira chakudya ku nyumba kwa Levi, amisonkho ambiri ndi “ochimwa” ankadya naye pamodzi ndi ophunzira ake, pakuti anali ambiri amene anamutsatira.
Il était à table dans sa maison, et beaucoup de publicains et de pécheurs étaient assis avec Jésus et ses disciples, car ils étaient nombreux, et ils le suivaient.
16 Pamene aphunzitsi amalamulo a Afarisi anamuona akudya ndi “ochimwa” ndi amisonkho, anafunsa ophunzira ake kuti, “Chifukwa chiyani amadya ndi olandira msonkho ndi ochimwa?”
Les scribes et les pharisiens, voyant qu'il mangeait avec les pécheurs et les publicains, dirent à ses disciples: « Pourquoi mange-t-il et boit-il avec les publicains et les pécheurs? »
17 Yesu atamva zimenezi, anawawuza kuti, “Anthu amene ali bwino safuna singʼanga koma odwala. Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa.”
Ayant entendu cela, Jésus leur dit: « Ceux qui sont en bonne santé n'ont pas besoin de médecin, mais ceux qui sont malades. Je suis venu non pas pour appeler les justes, mais les pécheurs à la repentance. »
18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi a Afarisi amasala kudya. Anthu ena anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Zitheka bwanji kuti ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala kudya, koma anu satero?”
Les disciples de Jean et les pharisiens étaient en train de jeûner, et ils vinrent lui demander: « Pourquoi les disciples de Jean et les disciples des pharisiens jeûnent-ils, mais tes disciples ne jeûnent pas? »
19 Yesu anayankha nati, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya bwanji pamene iye ali nawo pamodzi? Iwo sangatero, pamene iye ali nawo pamodzi.
Jésus leur dit: « Les mariés peuvent-ils jeûner tant que l'époux est avec eux? Tant qu'ils ont l'époux avec eux, ils ne peuvent pas jeûner.
20 Koma nthawi idzafika pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo, ndipo pa tsiku limenelo adzasala kudya.
Mais les jours viendront où l'époux leur sera enlevé, et alors ils jeûneront en ce jour-là.
21 “Palibe amene amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale. Ngati atatero, chigamba chatsopanocho chidzazomola chovala chakalecho, kukulitsa chibowocho.
Personne ne coud une pièce de tissu non trempé sur un vieux vêtement, sinon la pièce se rétracte et le nouveau se détache du vieux, et le trou est pire.
22 Ndipo palibe amene amathira vinyo watsopano mʼmatumba akale a vinyo. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba a vinyo ndipo vinyoyo pamodzi ndi matumbawo zidzawonongeka. Ayi, satero, amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso.”
Personne ne met du vin nouveau dans de vieilles outres, sinon le vin nouveau fait éclater les outres, et le vin se répand, et les outres sont détruites; mais on met du vin nouveau dans des outres neuves. »
23 Tsiku lina la Sabata, Yesu amadutsa pakati pa minda ya tirigu, ndipo ophunzira ake amayenda naye limodzi, nayamba kubudula ngala za tiriguyo.
Il traversait les champs de blé, le jour du sabbat, et ses disciples se mirent à arracher les épis.
24 Afarisi anati kwa Iye, “Taonani, chifukwa chiyani akuchita chosaloledwa ndi lamulo pa Sabata?”
Les pharisiens lui dirent: « Voici, pourquoi font-ils ce qui n'est pas permis le jour du sabbat? »
25 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali osowa ndi anamva njala?
Il leur dit: « N'avez-vous jamais lu ce que fit David, quand il était dans le besoin et qu'il avait faim, et ceux qui étaient avec lui?
26 Pa nthawi ya Abiatara mkulu wa ansembe, iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndi kudya buledi wopatulika amene amaloledwa kuti adye ndi ansembe okha. Ndipo anapereka wina kwa anzake.”
Comment il entra dans la maison de Dieu au moment où Abiathar, le grand prêtre, mangea le pain de proposition, qu'il n'est pas permis de manger, sauf pour les prêtres, et en donna aussi à ceux qui étaient avec lui? »
27 Pamenepo anawawuza kuti, “Sabata linapangidwira munthu, osati munthu kupangidwira Sabata.
Il leur dit: « Le sabbat a été fait pour l'homme, et non l'homme pour le sabbat.
28 Choncho Mwana wa Munthu ali Ambuye ngakhale wa Sabata.”
C'est pourquoi le Fils de l'homme est maître même du sabbat. »

< Marko 2 >