< Marko 1 >

1 Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
([This is/I want to tell you]) the good message about Jesus Christ, the Son of God (OR, the man who was also God). [What I want to tell you] begins just like the prophet Isaiah [said it would begin, when] he wrote [these words that God said to Jesus: ] Listen! I am sending my messenger ahead of you. He will prepare [people for] your [coming].
2 monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
3 “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
He will call out to people [who pass by where he is] in the desolate area, “As people improve and straighten out pathways [before an important official arrives] [MET], make [yourselves] ready [DOU] [in order that you will be prepared when] the Lord [comes].”
4 Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
[The messenger that Isaiah predicted was] John. [People called him] ‘The Baptizer’. In the desolate area near the Jordan River he kept telling people, “If you want God to forgive you for having sinned, you must turn away from your sinful behavior [before you ask me to] baptize [you].”
5 Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
A great number [HYP] of people who lived in Jerusalem [city] and [elsewhere] in the Judea [district] were going out to where John was. There, [after hearing John’s message], they [responded by] confessing the sinful things [that they had done]. Then they were being baptized by John {John was baptizing them} in the Jordan River.
6 Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
John wore [rough] clothes made of camel’s hair. And [as the prophet Elijah had done], he wore a leather belt around his waist; and what he ate was [only] grasshoppers and honey [that he found] in that desolate area.
7 Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
He was preaching, “Very shortly a man will come who is very great. I [am nothing compared to him. Because he is so superior to me], I am not even worthy to [serve him like a slave] by stooping down and untying his sandals.
8 Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
I used [only] water when I baptized you [because you said that you wanted to change your lives], but he will put his Holy Spirit [within] you [to truly change your lives].”
9 Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
During that time [when John was preaching], Jesus came from Nazareth [town], which is in Galilee [district]. He went to [where John was preaching] and he was baptized by John {John baptized him} in the Jordan [River].
10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
Immediately after [Jesus] came up out of the water, he saw heaven opened up [and he saw] the Spirit [of God] descending on himself. He came in the form of a dove.
11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
And [God] [MTY] spoke to him from heaven saying, “You are my Son, whom I love dearly. I am very pleased with you.”
12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
(Then/Right away) the Spirit [of God] sent Jesus into the desolate area.
13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
He was there for 40 days. During that time, he was tempted by Satan {Satan tempted him}. There were wild animals [there] also. But angels took care of him.
14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
Later, after John was put in prison {after [soldiers] put John in prison} [because he had rebuked the governor Herod Antipas for his sins], Jesus went to Galilee [district]. There he was preaching the good message [that came] from God.
15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
He was repeatedly saying, “Now is the time when God will begin to rule people’s lives [in a new way]. [So] turn away from your sinful behavior! Believe the good message [in order] ([to belong to him/to become those whose lives he will rule])!”
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
[One day], while Jesus was walking along by Galilee Lake, he saw [two men], Simon and Simon’s [younger] brother, Andrew. They were casting their [fishing] net into the lake. They [earned money by] catching [and selling] fish.
17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
Then Jesus said to them, “[Just like you have been] gathering fish, come with me and I will [teach] you how to [gather people to become my disciples]” [MET].
18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
Immediately they abandoned [the work that they were doing with] their nets, and they went with him.
19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
After they had gone on a little further, Jesus saw [two other men], James and James’ [younger] brother, John. They were the sons of [a man named] Zebedee. They were both in a boat mending [fishing] nets.
20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
As soon as Jesus saw them, he told them that [they should leave their work and to come with him]. So they left their father, [who remained] in the boat with the hired servants, and they went away with Jesus.
21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
[Later] Jesus [and those disciples] arrived at Capernaum [town]. On the next (Sabbath/Jewish rest day), after Jesus had entered (the synagogue/the Jewish meeting place), he began teaching [the people who had gathered there].
22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
They were continually amazed at the way he taught. [He did] not [just teach what others had taught], like the men who teach the [Jewish] laws did. [They habitually just repeated what other people had taught]. Instead, he taught with [his own] authority.
23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
Suddenly, [while he was teaching], a man [appeared] in their worship place who had an evil spirit in him, and he shouted,
24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
“Jesus, from Nazareth [town, since] we [evil spirits] have nothing in common with you, ([do not interfere with us]!/what do you want with us [evil spirits]?) [RHQ] (Do not destroy us [now]!/Have you come to destroy us [now]?) [RHQ] I know who you are. I know that you are the holy one [who has come] from God!”
25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
Jesus rebuked [the evil spirit], saying, “Be quiet! And come out [of the man]!”
26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
The evil spirit shook the man hard. He screamed loudly, and then he came out of the man [and left].
27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
All [the people who were there] were amazed. As a result, they discussed this among themselves, [exclaiming], “(This is [amazing]!/What is this?) [RHQ] Not only does he teach in a new and authoritative way, but also the evil spirits obey him [when] he commands [them]!”
28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
The people very soon told [many others] throughout the whole Galilee district what Jesus [had done].
29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
After they left (the synagogue/the Jewish meeting place), [Jesus, Simon and Andrew], along with James and John went directly to Simon and Andrew’s house.
30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
Simon’s mother-in-law was lying in bed because she had a [high] fever. Right away someone told Jesus about her [being sick].
31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
He went to her, and helped her up by taking hold of her hand. She recovered [at once] from the fever, and then she [got up and] served them [some food].
32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
That evening, after the sun had gone down [and restrictions about travel on the Sabbath/on the Jewish rest day]) [were ended], some people brought to Jesus many people who were sick and others whose lives evil spirits were controlling.
33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
[It seemed as though] everyone [HYP, MTY] [who lived in] the town was gathered at the doorway [of Simon’s house].
34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
Jesus healed many people who were ill with various diseases. He also expelled many demons [from people]. He did not allow the demons to tell people [about him], because they knew that he [had come from God, and for various reasons he did not want everyone to know that yet].
35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
Jesus got up very early [the next morning] while it was still dark. He left [the house] and went away [from the town] to a place where there were no people. Then he prayed there.
36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
Simon and his companions searched for him. When they found him, [wanting him to go back to town to help other people], they said to him,
37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
“[Come back to the town with us, because] many [HYP] people [in Capernaum] are looking for you!”
38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
He said to them, “[No], let’s go on to the neighboring towns in order that I can preach there also, because the reason that I came [into the world] was to [preach to people] in many places!”
39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
So they went throughout Galilee [district. As they did so, each (Sabbath/Jewish rest day]) he preached in (synagogues/Jewish meeting places). He was also expelling evil spirits [from people].
40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
[One day] a man who had [a bad skin disease called] leprosy came to Jesus. He knelt down in front of Jesus and then he pleaded with him saying, “[Please heal me, because I know] you are able to heal me if you want to!”
41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
Jesus felt very sorry for him. [So he ignored the religious laws about coming close to people who had that disease]. He reached out his hand and touched the man. Then he said to him, “Since I am willing [to heal you], be healed {I heal you} [now]!”
42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
Immediately the man was healed! He was no longer a leper!
43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
Jesus spoke sternly to him before he sent him away.
44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
What Jesus said was, “Go to a local priest and show yourself to him [in order that he may examine you and verify that you are healed]. Then, [after the priest tells the local people], they will know [that you have been healed, and you will be able to associate with them again]. Make sure that you do not tell others [about what happened] Then go to [Jerusalem and take to the priest what Moses commanded that people who have been healed from leprosy should offer, in order that he] may offer it [as a sacrifice to God].”
45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.
The man went [and presented himself to the priest. But then] he began to tell many people about [how Jesus had healed him] [DOU]. As a result, Jesus was no longer able to enter any town publicly [because the crowds would surround him]. Instead, he remained outside [the towns] in places [where no people lived]. But people kept coming to him from all over that region.

< Marko 1 >