< Malaki 2 >

1 “Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
»In sedaj, oh vi duhovniki, ta zapoved je za vas.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
Če ne boste poslušali in če si tega ne boste položili k srcu, da izročite slavo mojemu imenu, « govori Gospod nad bojevniki, »bom nad vas poslal celo prekletstvo in bom preklel vaše blagoslove. Da, že sem jih preklel, ker si tega niste vzeli k srcu.
3 “Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
Glejte, pokvaril bom vaše seme in razmazal gnoj na vaše obraze, celó gnoj vaših slovesnih praznikov in nekdo vas bo odvedel z njim.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
In vedeli boste, da sem to zapoved poslal k vam, da bi bila moja zaveza lahko z Levijem, « govori Gospod nad bojevniki.
5 Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
»Moja zaveza z njim je bila o življenju in miru in dal sem mu jih za strah, s katerim se me je bal in je bil prestrašen pred mojim imenom.
6 Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
Postava resnice je bila v njegovih ustih in krivičnosti ni bilo najti na njegovih ustnicah. Z menoj je hodil v miru in nepristranskosti in mnoge je odvrnil proč od krivičnosti.
7 “Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
Kajti duhovnikove ustnice naj bi ohranile spoznanje in pri njegovih ustih naj bi iskali postavo, kajti on je poslanec od Gospoda nad bojevniki.
8 Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Toda odšli ste iz poti, mnogim ste povzročili, da se spotaknejo ob postavi, pokvarili ste Lévijevo zavezo, « govori Gospod nad bojevniki.
9 “Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
»Zato sem vas tudi naredil zaničevanja vredne in vas ponižal pred vsem ljudstvom, glede na to, da se niste držali mojih poti, temveč ste bili delni v postavi.«
10 Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
Mar nimamo vsi istega očeta? Mar nas ni ustvaril en Bog? Zakaj zahrbtno postopamo vsak človek zoper svojega brata z oskrunitvijo zaveze naših očetov?
11 Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
Juda je postopal zahrbtno in ogabnost je zagrešena v Izraelu in v Jeruzalemu, kajti Juda je oskrunil svetost Gospoda, ki ga je ljubil in poročil hčer tujega boga.
12 Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
Gospod bo iztrebil človeka, ki to počne, gospodarja in učenca, iz Jakobovih šotorov in tistega, ki daruje daritev Gospodu nad bojevniki.
13 China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
In to ste ponovno storili, pokrivajoč Gospodov oltar s solzami, z jokanjem in z vzklikanjem, do take mere, da se ni več oziral na daritev ali to z dobro voljo sprejemal iz vaše roke.
14 Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
Vendar pravite: ›Zakaj?‹ Ker je bil Gospod priča med teboj in ženo tvoje mladosti, proti kateri si zahrbtno ravnal, čeprav je ona tvoja družabnica in žena tvoje zaveze.
15 Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
Mar ni on naredil eno? Vendar je imel preostanek duha. In zakaj eno? Da bi lahko iskal bogaboječe seme. Zato pazite na svojega duha in naj nihče ne postopa zahrbtno zoper ženo svoje mladosti.
16 Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
Kajti Gospod, Izraelov Bog, pravi, da sovraži ločitev, kajti nekdo zakriva nasilje s svojo obleko, ‹ govori Gospod nad bojevniki. ›Zato pazite na svojega duha, da ne ravnate zahrbtno.
17 Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”
S svojimi besedami ste izmučili Gospoda. Vendar pravite: ›V čem smo ga izmučili?‹ Ko pravite: ›Vsak, kdor počenja zlo, je dober v Gospodovih očeh in on se razveseljuje v njih‹ ali: ›Kje je Bog sodbe?‹«

< Malaki 2 >