< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
An oracle: the word of YHWH to Israel by Malachi.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
"I have loved you," says YHWH. Yet you say, "How have you loved us?" "Wasn't Esau Jacob's brother?" says YHWH, "Yet I loved Jacob;
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
but Esau I hated, and made his mountains a desolation, and gave his heritage to the jackals of the wilderness."
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Whereas Edom says, "We are beaten down, but we will return and build the waste places;" thus says YHWH of hosts, "They shall build, but I will throw down; and men will call them 'The Wicked Land,' even the people against whom YHWH shows wrath forever."
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Your eyes will see, and you will say, "YHWH is great—even beyond the border of Israel."
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
"A son honors his father, and a servant his master. If I am a father, then where is my honor? And if I am a master, where is the respect due me? says YHWH of hosts to you, cohanim, who despise my name. You say, 'How have we despised your name?'
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
You offer defiled bread on my altar. You say, 'How have we defiled you?' In that you say, 'YHWH's table is despised, and its fruit, its food, is despised.'
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
When you offer the blind for sacrifice, isn't that evil? And when you offer the lame and sick, isn't that evil? Present it now to your governor. Will he be pleased with you? Or will he accept your person?" says YHWH of hosts.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
"Now, please entreat the favor of God, that he may be gracious to us. With this, will he accept any of you?" says YHWH of hosts.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
"Oh that there were one among you who would shut the doors, that you might not kindle fire on my altar in vain. I have no pleasure in you," says YHWH of hosts, "neither will I accept an offering at your hand.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
For from the rising of the sun even to the going down of the same, my name is great among the nations, and in every place incense will be offered to my name, and a pure offering: for my name is great among the nations," says YHWH of hosts.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
"But you profane it, in that you say, 'YHWH's table is defiled, and its fruit, its food, is despised.'
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
You say also, 'Look, what a weariness it is.' and you sniff scornfully at it," says YHWH of hosts; "and you have brought that which was taken by violence, the lame, and the sick; thus you bring the offering. Should I accept this from your hand?" says YHWH of hosts.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
"But the deceiver is cursed, who has in his flock a male, and vows, and sacrifices to YHWH a blemished thing; for I am a great King," says YHWH of hosts, "and my name is awesome among the nations."

< Malaki 1 >