< Luka 4 >

1 Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
Исус пак пун Духа Светог врати се од Јордана, и одведе Га Дух у пустињу,
2 kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
И четрдесет дана куша Га ђаво, и не једе ништа за то дана; и кад се они навршише, онда огладне,
3 Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
И рече Му ђаво: Ако си Син Божји, реци овом камену да постане хлеб.
4 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
И одговори му Исус говорећи: У писму стоји: Неће живети човек о самом хлебу, него о свакој речи Божијој.
5 Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
И изведавши Га ђаво на гору високу показа Му сва царства овог света у тренућу ока,
6 Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
И рече Му ђаво: Теби ћу дати сву власт ову и славу њихову, јер је мени предана, и коме ја хоћу даћу је;
7 Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
Ти, дакле, ако се поклониш преда мном биће све твоје,
8 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
И одговарајући Исус рече му: Иди од мене, сотоно; у писму стоји: Поклањај се Господу Богу свом, и Њему једином служи.
9 Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
И одведе Га у Јерусалим, и постави Га наврх цркве, и рече Му: Ако си Син Божји, скочи одавде доле;
10 Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
Јер у писму стоји да ће анђелима својим заповедити за тебе да те сачувају,
11 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
И узеће те на руке да где не запнеш за камен ногом својом.
12 Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
И одговарајући Исус рече му: Казано је: Не кушај Господа Бога свог.
13 Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
И кад сврши ђаво све кушање, отиде од Њега за неко време.
14 Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
И врати се Исус у сили духовној у Галилеју; и отиде глас о Њему по свему оном крају.
15 Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
И Он учаше по зборницама њиховим, и сви Га хваљаху.
16 Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
И дође у Назарет где беше одрастао, и уђе по обичају свом у дан суботни у зборницу, и устаде да чита.
17 Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
И даше Му књигу пророка Исаије, и отворивши књигу нађе место где беше написано:
18 “Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
Дух је Господњи на мени; зато ме помаза да јавим јеванђеље сиромасима; посла ме да исцелим скрушене у срцу; да проповедим заробљенима да ће се отпустити, и слепима да ће прогледати; да отпустим сужње;
19 ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
И да проповедам пријатну годину Господњу.
20 Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
И затворивши књигу даде слузи, па седе: и сви у зборници гледаху на Њ.
21 ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
И поче им говорити: Данас се изврши ово писмо у ушима вашим.
22 Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
И сви Му сведочаху, и дивљаху се речима благодати које излажаху из уста Његових, и говораху: Није ли ово син Јосифов?
23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
И рече им: Ви ћете мени без сумње казати ову причу: Лекару! Излечи се сам; шта смо чули да си чинио у Капернауму учини и овде на својој постојбини.
24 Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
Рече пак: Заиста вам кажем: никакав пророк није мио на својој постојбини.
25 Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
А заиста вам кажем: Многе удовице беху у Израиљу у време Илијино кад се небо затвори три године и шест месеци и би велика глад по свој земљи;
26 Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
И ни к једној од њих не би послан Илија до у Сарепту сидонску к жени удовици.
27 Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
И многи беху губави у Израиљу за пророка Јелисија; и ниједан се од њих не очисти до Неемана Сиријанина.
28 Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
И сви се у зборници напунише гнева кад чуше ово.
29 Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
И уставши истераше Га напоље из града, и одведоше Га наврх горе где беше њихов град сазидан да би Га бацили одозго.
30 Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
Али Он прође између њих, и отиде.
31 Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
И дође у Капернаум град галилејски, и учаше их у суботе.
32 Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
И чуђаху се науци Његовој; јер Његова беседа беше силна.
33 Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
И у зборници беше човек у коме беше нечисти дух ђаволски, и повика гласно
34 “Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
Говорећи: Прођи се, шта је теби до нас, Исусе Назарећанине? Дошао си да нас погубиш? Знам Те ко си, Светац Божји.
35 Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
И запрети му Исус говорећи: Умукни, и изиђи из њега. И оборивши га ђаво на среду, изиђе из њега, и нимало му не науди.
36 Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
И у све уђе страх, и говораху један другом говорећи: Каква је то реч, да влашћу и силом заповеда нечистим духовима, и излазе?
37 Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
И отиде глас о Њему по свима околним местима.
38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
Уставши, пак, из зборнице дође у кућу Симонову; а ташту Симонову беше ухватила велика грозница, и молише Га за њу.
39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
И ставши више ње запрети грозници, и пусти је. И одмах устаде и служаше им.
40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
А кад захођаше сунце, сви који имаху болеснике од различних болести, довођаху их к Њему; а Он на сваког од њих меташе руке, и исцељиваше их.
41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
А и ђаволи излажаху из многих вичући и говорећи: Ти си Христос Син Божји. И запрећиваше им да не говоре да знају да је Он Христос.
42 Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
А кад наста дан, изиђе и отиде у пусто место; и народ Га тражаше, и дође к Њему, и задржаваху Га да не иде од њих.
43 Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
А Он им рече: и другим градовима треба ми проповедити јеванђеље о царству Божијем; јер сам на то послан.
44 Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.
И проповедаше по зборницама галилејским.

< Luka 4 >