< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
And it came to pass in those days that there went out a decree from Caesar Augustus, that all the world should be registered.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
(This registering was the first made while Quirinius was governor of Syria.)
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
And all went to be registered, each to his own city.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
And Joseph also went up from Galilee out of the city of Nazareth into Judaea, to the city of David, which is called Bethlehem, because he was of the house and lineage of David,
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
to be registered with Mary who had been betrothed to him, who was with child.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
And it came to pass, while they were there, that the days for her delivery were completed.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
And she brought forth her firstborn son, and wrapped him in swathing-clothes, and laid him in a manger, because there was no room for them in the inn.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
And there were in the same country shepherds abiding in the field, and keeping watch over their flock by night.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
And an angel of the Lord came to them, and the glory of the Lord shone around them; and they were in great fear.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
And the angel said to them, Fear not; for lo! I bring you good tidings of great joy, which shall be to the whole people;
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
for to you hath been born this day, in the city of David, a Saviour, who is the Christ, the Lord.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
And this shall be the sign to you: Ye shall find a babe wrapped in swathing-clothes, [[lying]] in a manger.
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
And suddenly there was with the angel a multitude of the heavenly host praising God, and saying,
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
“Glory to God in the highest, and on earth peace among men of good will!”
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
And it came to pass, when the angels had gone away from them into heaven, that the shepherds said one to another, Let us go at once to Bethlehem, and see that which hath come to pass, which the Lord hath made known to us.
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
And they came with haste, and found Mary and Joseph, and the babe lying in the manger.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
And when they had seen it, they made known abroad what had been told them concerning this child.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
And all who heard wondered at the things which were told them by the shepherds.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
But Mary kept all these things, and pondered them in her heart.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
And the shepherds returned, glorifying and praising God for all which they had heard and seen, as had been told them.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
And when eight days were completed for him to be circumcised, his name was called Jesus, the name given by the angel before he was conceived in the womb.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
And when the days of their purification according to the law of Moses were completed, they brought him to Jerusalem to present him to the Lord,
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
as it is written in the law of the Lord: “Every first-born male shall be called holy to the Lord,”
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
and to offer a sacrifice, according to what is directed in the law of the Lord: “A pair of turtle doves, or two young pigeons.”
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
And lo! there was a man in Jerusalem, whose name was Simeon; and he was a righteous and devout man, waiting for the consolation of Israel. And the Holy Spirit was upon him;
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
and it had been revealed to him by the Holy Spirit, that he should not see death before he had seen the Christ of the Lord.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
And he came in the Spirit into the temple; and when the parents brought in the child Jesus, to do for him according to the custom of the law,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
he took him in his arms, and blessed God, and said,
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
Lord! now lettest thou thy servant depart in peace, according to thy word;
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
for mine eyes have seen thy salvation,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
which thou hast prepared before the face of all the peoples;
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
a light to enlighten the gentiles, and to be the glory of thy people Israel.
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
And his father and his mother marveled at what was spoken concerning him.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
And Simeon blessed them, and said to Mary his mother, Behold, this child is appointed for the fall and rising of many in Israel, and for a sign that will be spoken against; —
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
yea, a sword will pierce through thine own soul, —that the thoughts of many hearts may be revealed.
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
And there was Anna, a prophetess, daughter of Phanuel: of the tribe of Asher; she was of great age, and had lived with a husband seven years from her virginity;
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
and she was a widow eighty-four years old, who never left the temple, worshipping with fastings and prayers night and day.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
And she came up at this very time, and gave thanks to God, and spoke of him to all that were looking for the redemption of Jerusalem.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
And when they had performed all things according to the law of the Lord, they returned to Galilee, to their own city Nazareth.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
And the child grew, and waxed strong, being filled with wisdom; and the grace of God was upon him.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Now his parents used to go yearly to Jerusalem at the feast of the passover.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
And when he was twelve years old, and they went up, after the custom of the feast,
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
and had completed the days, on their returning, the child Jesus tarried behind in Jerusalem; and his parents did not know it,
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
but, supposing him to be in the company, went a day's journey; and they sought him among their kinsfolk and acquaintance;
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
and not finding him, they returned to Jerusalem in search of him.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
And it came to pass, that after three days they found him in the temple sitting in the midst of the teachers, both listening to them and asking them questions.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
And all who heard him were astonished at his understanding and his answers.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
And when they saw him, they were amazed; and his mother said to him, Son, why hast thou thus dealt with us? behold, thy father and I have been seeking thee in much distress.
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
And he said to them, Why is it that ye have been seeking me? Did ye not know that I must be about my Father's business?
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
And they understood not what he spoke to them.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
And he went down with them, and came to Nazareth, and was subject to them. And his mother kept all these things in her heart.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
And Jesus increased in wisdom and stature, and in favor with God and men.

< Luka 2 >