< Luka 16 >

1 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
Ke Jesu go maadi o ŋɔdkaaba, “piado bá den ye, ki pia o ŋanlmankublo, ke bi ti cua ki tuali o ke o ŋalmankublo yeni biandi o piama.
2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
ke o piado yini o ki maadi o “Be n teni ke min gbia apo ya maama ki ŋani? Tieni nni a ŋalmankubli cɔli, kelima a ji kan ya tie n ŋalmankublo.”
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
K o ŋalmankublo maadi o pali nni “N ji ba tie ni ledi i, n cab áa ń ji bua beli nni li tuonli ne? N ji ki pia paalu ki ko, ke n ya miadi mo, li pia i fee
4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
N bani min ba tieni yaala ke bi ya beli nni n ligkubli tuonli mi ba cani ya niba ń tuo ki ga n cangu”
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
Yeni, ke o yini o canbaa pandanba yendo yendo, ki buali yua n kpia ki cua “A pia n canbaa panli yiŋa i?
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
Ke o maadi, mi kpama golindi kobga.” K o maadi o, “Ga a pantili ki kali tonma ki diani golindi piimu
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
Ke o ŋalmankublo buali tiano, “ke fini mo, a pia n canbaa panli yiŋa i? Ke o mo maadi “Mi ŋalkaama kpalpiadi kobga” Ke o maadi o “Ga a pantili ki diani kpapiadi piiniin
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
Canbaa den pagi ya ŋalmankublo n den ki tiegi yeni kelima o den tieni bu nunfanbu. Kelima ŋanduna ne bila fani yeni bi lieba ki cie mi yenyenma nni ya bila (aiōn g165)
9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
N maadi yi, Taa mani i ŋanduna janbi ŋalmani ki kpaani danlinba, li ya ti gben, yin baa yaaba n ba ga i cangu naani ke li ki pia gbenma. (aiōnios g166)
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
Yua n tiegi yaala n wa nni, ba ya tiegi yaala n yabi nni mo. Ke yua n ki tiegi yaala n wa nni kan ya tiegi yaala n yabi nni mo.
11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
A ya ki fidi ki kubi i janbi ŋalmani, ŋma ba dugi apo, ki piani a o ŋalmani yaali n mɔni i?
12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
Bi ya ki dugi a po ŋan kubi nitɔba ligi, maama, ŋma ba teni a a ligceli?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
Naaciemo bá kan fidi ki ya pia canbaanba bilie. Kelima, o ba fidi ki ya nani yendo ki nan bua o lielo, lan yaa ka wan cɔlni canbaa kpialo ki nan fali canbaalielo. A kan fidi ki ya ŋua U Tienu leni ŋalmani
14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
Farisienba ń gbadi li maama yeni, ke bi ji ñuadi o.
15 Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
Ke o maadi ba. “I ba maadi ki baa i mɔni, bi niba kani, ama U Tienu bani i pala. Bi niba ń nua yaali ke li tie kpiagdi yeni, U Tienu wani ya nunga nni ke li tie cancagndi i.
16 “Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
Yikodi maama yeni bi sawalpuaba n den kubi, ki ŋmagdi u dogu yo hali ke Janbatisi ti cua. Lan cili lanyogu, bi wangi U Tienu diema laabaalŋamo, nilo kuli tiendi ania ki kpaani wan kua lien nni
17 Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
Ama tanpoli leni ki tinga pendima ki paa ki cie li bali maama nni lanbyenli ń bodi ki kan tieni.
18 “Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
Ya nilo n ñani o denpua ki kuani potiano conbi, yua n kuani ya pua n ñani o calo kani mo conbi.
19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
Cengi mani, ŋalmandaano bá den ye ki la ti tiakpiagdi, ki di ti jiemandi, ki ye u yenyienŋamu nni daali kuli, ke o pali mani boncianla o piama po.
20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
O luodo mo den ye, ke bi yi o Lasari, ke o dua o piado bulñɔjabu kani, ki pia a nala o gbanu po kuli.
21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
O den suni ke wan baa ya jiejɔgdi n baali o piado jedikaanu, bá i sangbanli den lagdi o nala i.
22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
Ke o luodo tikpe, ke malekinba tugi o, ki duoni o Abalahama kani. O piado mo ń kpe, ban pii o,
23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
Wan den ye o mubuogu nni ki laadi fala, ki ti yaadi ki diidi, ki la Abalahama hali fagma ke o wobi Lasari ki tabni o pali. (Hadēs g86)
24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
Ke o yigni paama ki maadi, “Ti Báa Abalahama, diidi nni leni mi niñima, ki sɔni Lasari wan tuu mi ñima leni o nubili, ki maani n lanbu po, bun sɔngi, kelima n ye leni mi cacagma i ku mubuogu nni.
25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
Ama ke Abalahama maadi “N biga ya tiani ke a yenyienu nni, a den baa yaala n ŋani boncianla a po ke Lasari mo den laadi fala boncianla. Ama mɔlane, o ji ye ne, u yenyienŋamu nni, ke a mo falaciamu nni
26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
Li ya ñani lankani i, buociangu ye siiga nni, ki paadi tinba yen yinba, ke nilo kan fidi ki ña ti kani ki gedi i kani, obá mo kan fidi ki ña i kani ki cua ti kani.
27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
O ŋalmandaano ń maadi “N Báa Abalahama, mia sugli ki sɔni o n báa diegu nni.
28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
Kelima n pia naataanjaba mu, wan tuodi ki tiadi ba. N jie ke bi mo ń da ti pundi ya falacimu nni ke n ye ne.
29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
Ama ke Abalahama maadi, “Bi pia Moyiisi leni bi sawalpuaba maama; ban cengi mani “
30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
O piado ń guani ki maadi, “li kan tuo, ti Báa Abalahama, ama nilo ya ñani bi kpienba kani, ki gedi ki maadi ba, bi ba lebdi bi yama”
31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”
Ama ke Abalahama maadi, “Bi ya ki cengi Moyiisi leni bi sawalpuaba maama, bá nilo ya yiedi bi tinkpiba siiga, bi kan cengi o.”

< Luka 16 >