< Luka 16 >

1 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
Men han sagde også til Disciplene: "Der var en rig Mand, som havde en Husholder, og denne blev angiven for ham som en, der ødte hans Ejendom.
2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
Og han lod ham kalde og sagde til ham: Hvad er dette, jeg hører om dig? Aflæg Regnskabet for din Husholdning; thi du kan ikke længer være Husholder.
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
Men Husholderen sagde ved sig selv: Hvad skal jeg gøre, efterdi min Herre tager Husholdningen fra mig? Jeg formår ikke at Grave, jeg skammer mig ved at tigge.
4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
Nu ved jeg, hvad jeg vil gøre, for af de skulle modtage mig i deres Huse, når jeg bliver sat fra Husholdningen.
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
Og han kaldte hver enkelt af sin Herres Skyldnere til sig og sagde til den første: Hvor meget er du min Herre skyldig?
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
Men han sagde: Hundrede Fade Olie. Og han sagde til ham: Tag dit Skyldbrev, og sæt dig hurtig ned og skriv halvtredsindstyve!
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
Derefter sagde han til en anden: Men du, hvor meget er du skyldig? Men han sagde: Hundrede Mål Hvede. Han siger til ham: Tag dit Skyldbrev og skriv firsindstyve!
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
Og Herren roste den uretfærdige Husholder, fordi han havde handlet klogelig; thi denne Verdens Børn ere klogere end Lysets Børn imod deres egen Slægt. (aiōn g165)
9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
Og jeg siger eder: Gører eder Venner ved Uretfærdighedens Mammon, for at de, når det er forbi med den, må modtage eder i de evige Boliger. (aiōnios g166)
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
Den, som er tro i det mindste, er også tro i meget, og den, som er uretfærdig i det mindste, er også uretfærdig i meget.
11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
Dersom I da ikke have været tro i den uretfærdige Mammon, hvem vil da betro eder den sande?
12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
Og dersom I ikke have været tro i det, som andre eje, hvem vil da give eder noget selv at eje?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
Ingen Tjener kan tjene to Herrer; thi han vil enten hade den ene og elske den anden, eller holde sig til den ene og ringeagte den anden; I kunne ikke tjene Gud og Mammon."
14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
Men alt dette hørte Farisæerne, som vare pengegerrige, og de spottede ham.
15 Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
Og han sagde til dem: "I ere de, som gøre eder selv retfærdige for Menneskene; men Gud kender eders Hjerter; thi det, som er højt iblandt Mennesker, er en Vederstyggelighed for Gud.
16 “Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
Loven og Profeterne vare indtil Johannes; fra den Tid forkyndes Evangeliet om Guds Rige, og enhver trænger derind med Vold.
17 Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
Men det er lettere, at Himmelen og Jorden forgå, end at en Tøddel af Loven bortfalder.
18 “Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
Hver, som skiller sig fra sin Hustru og tager en anden til Ægte, bedriver Hor; og hver, som tager til Ægte en Kvinde, der er skilt fra sin Mand, bedriver Hor.
19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
Men der var en rig Mand, og han klædte sig i Purpur og kostbart Linned og levede hver Dag i Fryd og Herlighed.
20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
Men en fattig ved Navn Lazarus var lagt ved hans Port, fuld af Sår.
21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
Og han attråede at mættes af det, som faldt fra den Riges Bord; men også Hundene kom og slikkede hans Sår.
22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
Men det skete, at den fattige døde, og at han blev henbåren af Englene i Abrahams Skød; men den rige døde også og blev begravet.
23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
Og da han slog sine Øjne op i Dødsriget, hvor han var i Pine, ser han Abraham langt borte og Lazarus i hans Skød. (Hadēs g86)
24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
Og han råbte og sagde: Fader Abraham! forbarm dig over mig, og send Lazarus, for at han kan dyppe det yderste af sin Finger i Vand og læske min Tunge; thi jeg pines svarlig i denne Lue.
25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
Men Abraham sagde: Barn! kom i Hu, at du har fået dit gode i din Livstid, og Lazarus ligeså det onde; men nu trøstes han her, og du pines.
26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
Og foruden alt dette er der fæstet et stort Svælg imellem os og eder, for at de, som ville fare herfra over til eder, ikke skulle kunne det, og de ikke heller skulle fare derfra over til os.
27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
Men han sagde: Så beder jeg dig, Fader! at du vil sende ham til min Faders Hus
28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
thi jeg har fem Brødre for at han kan vidne for dem, for at ikke også de skulle komme i dette Pinested.
29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
Men Abraham siger til ham: De have Moses og Profeterne, lad dem høre dem!
30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
Men han sagde: Nej, Fader Abraham! men dersom nogen fra de døde kommer til dem, ville de omvende sig.
31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”
Men han sagde til ham: Høre de ikke Moses og Profeterne, da lade de sig heller ikke overbevise, om nogen opstår fra de døde."

< Luka 16 >