< Luka 12 >

1 Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.
Sur ces entrefaites, les gens s'étant rassemblés par milliers, au point de se fouler les uns les autres, Jésus se mit à dire à ses disciples: " Gardez-vous avant tout du levain des Pharisiens, qui est l'hypocrisie.
2 Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
Il n'y a rien de caché qui ne doive être révélé, rien de secret qui ne doive être connu.
3 Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
C'est pourquoi, tout ce que vous aurez dit dans les ténèbres, on l'entendra au grand jour; et ce que vous aurez dit à l'oreille dans l'intérieur de la maison, sera publié sur les toits.
4 “Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu.
Mais je vous dis, à vous qui êtes mes amis: Ne craignez pas ceux qui tuent le corps, et qui après cela ne peuvent rien faire de plus.
5 Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna g1067)
Je vais vous apprendre qui vous devez craindre: craignez celui qui, après avoir tué, a le pouvoir de jeter dans la géhenne; oui, je vous le dis, craignez celui-là. (Geenna g1067)
6 Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu.
Cinq passereaux ne se vendent-ils pas deux as? Et pas un d'eux n'est en oubli devant Dieu.
7 Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
Mais les cheveux mêmes de votre tête sont tous comptés. Ne craignez donc point: vous êtes de plus de prix que beaucoup de passereaux.
8 “Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu.
Je vous le dis encore, quiconque m'aura confessé devant les hommes, le Fils de l'homme aussi le confessera devant les anges de Dieu;
9 Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu.
mais celui qui m'aura renié devant les hommes, sera renié devant les anges de Dieu.
10 Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.
Et quiconque parlera contre le Fils de l'homme, obtiendra le pardon; mais pour celui qui aura blasphémé contre l'Esprit-Saint, il n'y aura point de pardon.
11 “Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule,
Quand on vous conduira devant les synagogues, les magistrats et les autorités, ne vous mettez point en peine de la manière dont vous vous défendrez, ni de ce que vous direz;
12 pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”
car le Saint-Esprit vous enseignera à l'heure même ce qu'il faudra dire. "
13 Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”
Alors du milieu de la foule quelqu'un dit à Jésus: " Maître, dites à mon frère de partager avec moi notre héritage. "
14 Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?”
Jésus lui répondit: " Homme, qui m'a établi pour être votre juge, ou pour faire vos partages? "
15 Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
Et il dit au peuple: " Gardez-vous avec soin de toute avarice; car, dans l'abondance même, la vie d'un homme ne dépend pas des biens qu'il possède. "
16 Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri.
Puis il leur dit cette parabole: " Il y avait un homme riche dont le domaine avait beaucoup rapporté.
17 Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’
Et il s'entretenait en lui-même de ces pensées: Que ferai-je? car je n'ai pas de place pour serrer ma récolte.
18 “Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu.
Voici, dit-il, ce que je ferai. J'abattrai mes greniers, et j'en construirai de plus grands, et j'y amasserai la totalité de mes récoltes et de mes biens.
19 Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’”
Et je dirai à mon âme: Mon âme, tu as de grands biens en réserve pour beaucoup d'années; repose-toi, mange, bois, fais bonne chère.
20 “Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’
Mais Dieu lui dit: Insensé! cette nuit même on te redemandera ton âme; et ce que tu as mis en réserve, pour qui sera-t-il?
21 “Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”
Il en est ainsi de l'homme qui amasse des trésors pour lui-même, et qui n'est pas riche devant Dieu. "
22 Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
Jésus dit ensuite à ses disciples: " C'est pourquoi je vous dis: Ne vous inquiétez pas pour votre vie, de ce que vous mangerez; ni pour votre corps, de quoi vous le vêtirez.
23 Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala.
La vie est plus que la nourriture, et le corps plus que le vêtement.
24 Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
Considérez les corbeaux: ils ne sèment ni ne moissonnent; ils n'ont ni cellier ni grenier, et Dieu les nourrit. Combien ne valez-vous pas plus que ces oiseaux?
25 Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
Qui de vous pourrait, à force de soucis, ajouter une coudée à la longueur de sa vie?
26 Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?
Si donc les moindres choses sont au-dessus de votre pouvoir, pourquoi vous inquiétez-vous des autres?
27 “Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa.
Considérez les lis, comment ils croissent, ils ne travaillent ni ne filent, et, je vous le dis, Salomon dans toute sa gloire n'était pas vêtu comme l'un d'eux.
28 Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
Si Dieu revêt de la sorte l'herbe, qui est aujourd'hui dans les champs et qui demain sera jetée au four, combien plus le fera-t-il pour vous, hommes de peu de foi!
29 Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
Vous non plus, ne cherchez pas ce que vous mangerez ou ce que vous boirez, et ne soyez pas en suspens dans l'inquiétude.
30 Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi.
Car ce sont les gens de ce monde qui se préoccupent de toutes ces choses; mais votre Père sait que vous en avez besoin.
31 Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
Au reste, cherchez le royaume de Dieu, et tout cela vous sera donné par surcroît.
32 “Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
Ne craignez point, petit troupeau, car il a plus à votre Père de vous donner le royaume.
33 Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge.
Vendez ce que vous avez, et donnez l'aumône. Faites-vous des bourses que le temps n'use pas, un trésor inépuisable dans les cieux, où les voleurs n'ont point d'accès, et où les mites ne rongent point.
34 Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
Car là où est votre trésor, là aussi sera votre cœur.
35 “Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka,
Ayez la ceinture aux reins et vos lampes allumées!
36 ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko.
Soyez semblables à des hommes qui attendent le moment où leur maître reviendra des noces, afin que, dès qu'il arrivera et frappera à la porte, ils lui ouvrent aussitôt.
37 Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira.
Heureux ces serviteurs que le maître, à son retour, trouvera veillant! Je vous le dis en vérité, il se ceindra, il les fera mettre à table, et s'approchera pour les servir.
38 Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku.
Qu'il arrive à la deuxième veille, qu'il arrive à la troisième, s'il les trouve ainsi, heureux ces serviteurs!
39 Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
Mais sachez bien que si le père de famille savait à quelle heure le voleur doit venir, il veillerait et ne laisserait point percer sa maison.
40 Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
Vous aussi, tenez-vous prêts, car le Fils de l'homme viendra à l'heure que vous ne pensez pas. "
41 Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
Alors Pierre lui dit: " Est-ce à nous que vous adressez cette parabole, ou bien est-ce aussi à tous? "
42 Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera?
Le Seigneur répondit: " Quel est l'économe fidèle et sage que le maître établira sur ses serviteurs, pour distribuer, au temps convenable, la mesure de froment?
43 Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.
Heureux ce serviteur, que le maître, à son arrivée, trouvera agissant ainsi!
44 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
Je vous le dis, en vérité, il l'établira sur tous ses biens.
45 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera.
Mais si ce serviteur dit en lui-même: Mon maître tarde à venir; et qu'il se mette à battre les serviteurs et les servantes, à manger, à boire et à s'enivrer,
46 Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
le maître de ce serviteur viendra au jour où il ne s'attend pas et à l'heure qu'il ne sait pas, et il le fera déchirer de coups, et lui assignera sa part avec les infidèles.
47 “Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri.
Ce serviteur-là qui aura connu la volonté de son maître, et qui n'aura rien tenu prêt, ni agi selon sa volonté, recevra un grand nombre de coups.
48 Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
Mais celui qui ne l'aura pas connue, et qui aura fait des choses dignes de châtiment, recevra peu de coups. On exigera beaucoup de celui à qui l'on a beaucoup donné; et plus on aura confié à quelqu'un, plus on lui demandera.
49 “Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale.
Je suis venu jeter le feu sur la terre, et que désiré-je, si déjà il est allumé?
50 Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika!
Je dois encore être baptisé d'un baptême, et quelle angoisse en moi jusqu'à ce qu'il soit accompli!
51 Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana.
Pensez-vous que je sois venu établir la paix sur la terre? Non, vous dis-je, mais bien la division.
52 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu.
Car désormais, s'il y a cinq personnes dans une maison, elles seront divisés, trois contre deux, et deux contre trois;
53 Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”
le père sera divisé contre son fils, et le fils contre son père; la mère contre sa fille et la fille contre sa mère; la belle-mère contre sa belle-fille, et la belle-fille contre sa belle-mère. "
54 Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi.
Il disait encore au peuple: " Lorsque vous voyez la nuée se lever au couchant, vous dites aussitôt: La pluie vient; et cela arrive ainsi.
55 Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi.
Et quand vous voyez souffler le vent du midi, vous dites: Il fera chaud, et cela arrive.
56 Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?
Hypocrites, vous savez reconnaître les aspects du ciel et de la terre; comment donc ne reconnaissez-vous pas le temps où nous sommes?
57 “Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita?
Et comment ne discernez-vous pas de vous-mêmes ce qui est juste?
58 Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende.
En effet, lorsque tu te rends avec ton adversaire devant le magistrat, tâche en chemin de te dégager de sa poursuite, de peur qu'il ne te traîne devant le juge, et que le juge ne te livre à l'officier de justice, et que celui-ci ne te jette en prison.
59 Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”
Je te le dis, tu ne sortiras point de là que tu n'aies payé jusqu'à la dernière obole. "

< Luka 12 >