< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
Forasmuch as many have undertaken to draw up a relation concerning the matters fully believed among us,
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
as those who from the beginning were eye-witnesses of and attendants on the Word have delivered them to us,
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
it has seemed good to me also, accurately acquainted from the origin with all things, to write to thee with method, most excellent Theophilus,
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
that thou mightest know the certainty of those things in which thou hast been instructed.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
There was in the days of Herod, the king of Judaea, a certain priest, by name Zacharias, of the course of Abia, and his wife of the daughters of Aaron, and her name Elizabeth.
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
And they were both just before God, walking in all the commandments and ordinances of the Lord blameless.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
And they had no child, because Elizabeth was barren, and they were both advanced in years.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
And it came to pass, as he fulfilled his priestly service before God in the order of his course,
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
it fell to him by lot, according to the custom of the priesthood, to enter into the temple of the Lord to burn incense.
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
And all the multitude of the people were praying without at the hour of incense.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
And an angel of [the] Lord appeared to him, standing on the right of the altar of incense.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
And Zacharias was troubled, seeing [him], and fear fell upon him.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
But the angel said to him, Fear not, Zacharias, because thy supplication has been heard, and thy wife Elizabeth shall bear thee a son, and thou shalt call his name John.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
And he shall be to thee joy and rejoicing, and many shall rejoice at his birth.
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
For he shall be great before [the] Lord, and he shall drink no wine nor strong drink; and he shall be filled with [the] Holy Spirit, even from his mother's womb.
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
And many of the sons of Israel shall he turn to [the] Lord their God.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
And he shall go before him in [the] spirit and power of Elias, to turn hearts of fathers to children, and disobedient ones to [the] thoughts of just [men], to make ready for [the] Lord a prepared people.
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
And Zacharias said to the angel, How shall I know this, for I am an old man, and my wife advanced in years?
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
And the angel answering, said to him, I am Gabriel, who stand before God, and I have been sent to speak to thee, and to bring these glad tidings to thee;
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
and behold, thou shalt be silent and not able to speak, till the day in which these things shall take place, because thou hast not believed my words, the which shall be fulfilled in their time.
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
And the people were awaiting Zacharias, and they wondered at his delaying in the temple.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
But when he came out he could not speak to them, and they recognised that he had seen a vision in the temple. And he was making signs to them, and continued dumb.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
And it came to pass, when the days of his service were completed, he departed to his house.
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
Now after these days, Elizabeth his wife conceived, and hid herself five months, saying,
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
Thus has [the] Lord done to me in [these] days in which he looked upon [me] to take away my reproach among men.
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
But in the sixth month, the angel Gabriel was sent of God to a city of Galilee, of which [the] name [was] Nazareth,
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
to a virgin betrothed to a man whose name [was] Joseph, of the house of David; and the virgin's name [was] Mary.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
And the angel came in to her, and said, Hail, [thou] favoured one! the Lord [is] with thee: [blessed art thou amongst women].
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
But she, [seeing] [the angel], was troubled at his word, and reasoned in her mind what this salutation might be.
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
And the angel said to her, Fear not, Mary, for thou hast found favour with God;
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
and behold, thou shalt conceive in the womb and bear a son, and thou shalt call his name Jesus.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
He shall be great, and shall be called Son of [the] Highest; and [the] Lord God shall give him the throne of David his father;
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
and he shall reign over the house of Jacob for the ages, and of his kingdom there shall not be an end. (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
But Mary said to the angel, How shall this be, since I know not a man?
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
And the angel answering said to her, [The] Holy Spirit shall come upon thee, and power of [the] Highest overshadow thee, wherefore the holy thing also which shall be born shall be called Son of God.
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
And behold, Elizabeth, thy kinswoman, she also has conceived a son in her old age, and this is the sixth month to her that was called barren:
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
for nothing shall be impossible with God.
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
And Mary said, Behold the bondmaid of [the] Lord; be it to me according to thy word. And the angel departed from her.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
And Mary, rising up in those days, went into the hill country with haste, to a city of Judah,
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
and entered into the house of Zacharias, and saluted Elizabeth.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
And it came to pass, as Elizabeth heard the salutation of Mary, the babe leaped in her womb; and Elizabeth was filled with [the] Holy Spirit,
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
and cried out with a loud voice and said, Blessed [art] thou amongst women, and blessed the fruit of thy womb.
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
And whence [is] this to me, that the mother of my Lord should come to me?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
For behold, as the voice of thy salutation sounded in my ears, the babe leaped with joy in my womb.
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
And blessed [is] she that has believed, for there shall be a fulfilment of the things spoken to her from [the] Lord.
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
And Mary said, My soul magnifies the Lord,
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
and my spirit has rejoiced in God my Saviour.
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
For he has looked upon the low estate of his bondmaid; for behold, from henceforth all generations shall call me blessed.
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
For the Mighty One has done to me great things, and holy [is] his name;
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
and his mercy [is] to generations and generations to them that fear him.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
He has wrought strength with his arm; he has scattered haughty [ones] in the thought of their heart.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
He has put down rulers from thrones, and exalted the lowly.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
He has filled the hungry with good things, and sent away the rich empty.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
He has helped Israel his servant, in order to remember mercy,
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
(as he spoke to our fathers, ) to Abraham and to his seed for ever. (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
And Mary abode with her about three months, and returned to her house.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
But the time was fulfilled for Elizabeth that she should bring forth, and she gave birth to a son.
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
And her neighbours and kinsfolk heard that [the] Lord had magnified his mercy with her, and they rejoiced with her.
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
And it came to pass on the eighth day they came to circumcise the child, and they called it after the name of his father, Zacharias.
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
And his mother answering said, No; but he shall be called John.
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
And they said to her, There is no one among thy kinsfolk who is called by this name.
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
And they made signs to his father as to what he might wish it to be called.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
And having asked for a writing-table, he wrote saying, John is his name. And they all wondered.
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
And his mouth was opened immediately, and his tongue, and he spake, blessing God.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
And fear came upon all who dwelt round about them; and in the whole hill-country of Judaea all these things were the subject of conversation.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
And all who heard them laid them up in their heart, saying, What then will this child be? And [the] Lord's hand was with him.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
And Zacharias his father was filled with [the] Holy Spirit, and prophesied, saying,
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
Blessed be [the] Lord the God of Israel, because he has visited and wrought redemption for his people,
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
and raised up a horn of deliverance for us in the house of David his servant;
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
as he spoke by [the] mouth of his holy prophets, who have been since the world began; (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
deliverance from our enemies and out of the hand of all who hate us;
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
to fulfil mercy with our fathers and remember his holy covenant,
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
[the] oath which he swore to Abraham our father,
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
to give us, that, saved out of the hand of our enemies, we should serve him without fear
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
in piety and righteousness before him all our days.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
And thou, child, shalt be called [the] prophet of [the] Highest; for thou shalt go before the face of [the] Lord to make ready his ways;
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
to give knowledge of deliverance to his people by [the] remission of their sins
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
on account of [the] bowels of mercy of our God; wherein [the] dayspring from on high has visited us,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
to shine upon them who were sitting in darkness and in [the] shadow of death, to guide our feet into [the] way of peace.
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
— And the child grew and was strengthened in spirit; and he was in the deserts until the day of his shewing to Israel.

< Luka 1 >