< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
Nowe the Lord called Moses, and spake vnto him out of the Tabernacle of the Congregation, saying,
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Speake vnto the children of Israel, and thou shalt say vnto them, If any of you offer a sacrifice vnto the Lord, ye shall offer your sacrifice of cattell, as of beeues and of the sheepe.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
If his sacrifice be a burnt offering of the heard, he shall offer a male without blemish, presenting him of his owne voluntarie will at the doore of the Tabernacle of the Congregation before the Lord.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he shall put his hande vpon the head of the burnt offering, and it shalbe accepted to the Lord, to be his atonement.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall kill the bullocke before the Lord, and the Priestes Aarons sonnes shall offer the blood, and shall sprinckle it round about vpon the altar, that is by the doore of the Tabernacle of the Congregation.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
Then shall he fley the burnt offering, and cut it in pieces.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
So the sonnes of Aaron the Priest shall put fire vpon the altar, and lay the wood in order vpon the fire.
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
Then the Priestes Aarons sonnes shall lay the parts in order, the head and the kall vpon the wood that is in the fire which is vpon the altar.
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
But the inwardes thereof and the legges thereof he shall wash in water, and the Priest shall burne all on the altar: for it is a burnt offering, an oblation made by fire, for a sweete sauour vnto the Lord.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
And if his sacrifice for the burnt offering be of the flocks (as of the sheepe, or of the goats) he shall offer a male without blemish,
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
And he shall kill it on the Northside of the altar before the Lord, and the Priestes Aarons sonnes shall sprinckle the blood thereof rounde about vpon the altar.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
And he shall cut it in pieces, separating his head and his kall, and the Priest shall lay them in order vpon the wood that lyeth in the fire which is on the altar:
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
But he shall wash the inwardes, and the legges with water, and the Priest shall offer the whole and burne it vpon the altar: for it is a burnt offering, an oblation made by fire for a sweete sauour vnto the Lord.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
And if his sacrifice be a burnt offring to the Lord of ye foules, then he shall offer his sacrifice of the turtle doues, or of the yong pigeons.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
And the Priest shall bring it vnto the altar, and wring the necke of it asunder, and burne it on the altar: and the blood thereof shall bee shed vpon the side of the altar.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
And he shall plucke out his maw with his fethers, and cast them beside the altar on the East part in the place of the ashes.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
And he shall cleaue it with his wings, but not deuide it asunder: and the Priest shall burne it vpon the altar vpon the wood that is in the fire: for it is a burnt offering, an oblation made by fire for a sweete sauour vnto the Lord.

< Levitiko 1 >