< Levitiko 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spoke to Moses, saying,
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
Take Aaron and his sons with him, and the garments, and the anointing oil, and a bullock for the sin-offering, and two rams, and a basket of unleavened bread;
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
And assemble thou all the congregation to the door of the tabernacle of the congregation.
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
And Moses did as the LORD commanded him; and the assembly was gathered to the door of the tabernacle of the congregation.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
And Moses said to the congregation, This [is] the thing which the LORD commanded to be done.
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
And Moses brought Aaron and his sons, and washed them with water.
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
And he put upon him the coat, and girded him with the girdle, and clothed him with the robe, and put the ephod upon him, and he girded him with the curious girdle of the ephod, and bound [it] to him with it.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
And he put the breast-plate upon him: also he put in the breast-plate the Urim and the Thummim.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
And he put the miter upon his head; also upon the miter, [even] upon his front, did he put the golden plate, the holy crown; as the LORD commanded Moses.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
And Moses took the anointing oil, and anointed the tabernacle and all that [was] in it, and sanctified them.
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
And he sprinkled part of it upon the altar seven times, and anointed the altar and all its vessels, both the laver and its foot, to sanctify them.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
And he poured of the anointing oil upon Aaron's head, and anointed him, to sanctify him.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
And Moses brought Aaron's sons, and put coats upon them, and girded them with girdles, and put bonnets upon them; as the LORD commanded Moses.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
And he brought the bullock for the sin-offering: and Aaron and his sons laid their hands upon the head of the bullock for the sin-offering.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
And he slew [it]; and Moses took the blood, and put [it] upon the horns of the altar round about with his finger, and purified the altar, and poured the blood at the bottom of the altar, and sanctified it, to make reconciliation upon it.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
And he took all the fat that [was] upon the inwards, and the caul [above] the liver, and the two kidneys, and their fat, and Moses burned [it] upon the altar.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
But the bullock, and his hide, his flesh, and his dung, he burnt with fire without the camp; as the LORD commanded Moses.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
And he brought the ram for the burnt-offering: and Aaron and his sons laid their hands upon the head of the ram.
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
And he killed [it]; and Moses sprinkled the blood upon the altar round about.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
And he cut the ram into pieces; and Moses burnt the head, and the pieces, and the fat.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
And he washed the inwards and the legs in water; and Moses burnt the whole ram upon the altar: it [was] a burnt-sacrifice for a sweet savor, [and] an offering made by fire to the LORD; as the LORD commanded Moses.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
And he brought the other ram, the ram of consecration: and Aaron and his sons laid their hands upon the head of the ram.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
And he slew [it]; and Moses took of its blood, and put [it] upon the tip of Aaron's right ear, and upon the thumb of his right hand, and upon the great toe of his right foot.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
And he brought Aaron's sons, and Moses put of the blood upon the tip of their right ear, and upon the thumbs of their right hands, and upon the great toes of their right feet: and Moses sprinkled the blood upon the altar round about.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
And he took the fat, and the rump, and all the fat that [was] upon the inwards, and the caul [above] the liver, and the two kidneys, and their fat, and the right shoulder:
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
And out of the basket of unleavened bread, that [was] before the LORD, he took one unleavened cake, and a cake of oiled bread, and one wafer, and put [them] on the fat, and upon the right shoulder:
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
And he put all upon Aaron's hands, and upon his sons' hands, and waved them [for] a wave-offering before the LORD.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
And Moses took them from off their hands, and burnt [them] on the altar upon the burnt-offering: they [were] consecrations for a sweet savor: it [is] an offering made by fire to the LORD.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
And Moses took the breast, and waved it [for] a wave-offering before the LORD: [for] of the ram of consecration it was Moses's part; as the LORD commanded Moses.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
And Moses took of the anointing oil, and of the blood which [was] upon the altar, and sprinkled [it] upon Aaron, [and] upon his garments, and upon his sons, and upon his sons' garments with him; and sanctified Aaron, [and] his garments, and his sons, and his sons' garments with him.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
And Moses said to Aaron and to his sons, Boil the flesh [at] the door of the tabernacle of the congregation; and there eat it with the bread that [is] in the basket of consecrations, as I commanded, saying, Aaron and his sons shall eat it.
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
And that which remaineth of the flesh and of the bread shall ye burn with fire.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
And ye shall not go out of the door of the tabernacle of the congregation [in] seven days, until the days of your consecration shall be at an end: for seven days shall he consecrate you.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
As he hath done this day, [so] the LORD hath commanded to do, to make an atonement for you.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
Therefore shall ye abide [at] the door of the tabernacle of the congregation day and night seven days, and keep the charge of the LORD, that ye die not: for so I am commanded.
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
So Aaron and his sons did all things which the LORD commanded by the hand of Moses.

< Levitiko 8 >