< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Och Herren talade med Mose, och sade:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Tala med Israels barn, och säg till dem: Jag är Herren edar Gud.
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
I skolen icke göra efter som görs i Egypti land, der I bott hafven; och icke efter som görs i Canaans land, der jag dig införa skall; I skolen icke heller hålla eder vid deras sätt;
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Utan efter mina rätter skolen I göra, och mina stadgar skolen I hålla, att I vandren derutinnan; ty jag är Herren edar Gud.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Derföre skolen I hålla mina stadgar, och mina rätter; ty hvilken menniska dem gör, han skall derigenom lefva; ty jag är Herren.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
Ingen skall gå in till sina nästa blodsfränko, till att blotta hennes blygd; ty jag är Herren.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
Du skall dins faders och dine moders blygd icke blotta; hon är din moder, derföre skall du icke blotta hennes blygd.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
Du skall icke blotta dins faders hustrus blygd; ty det är dins faders blygd.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
Du skall icke blotta dine systers blygd, den dins faders, eller dine moders dotter är, hemma eller ute född.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
Du skall icke blotta dine sonadotters, eller dine dotterdotters blygd; ty det är din blygd.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
Du skall icke blotta dins faders hustrus dotters blygd, den dinom fader född är, och din syster är.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
Du skall icke blotta dins faders systers blygd; ty det är dins faders nästa blodsfränka.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
Du skall icke blotta dine moders systers blygd; ty hon är dine moders nästa blodsfränka.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
Du skall icke blotta dins faderbroders blygd, så att du tager hans hustru; ty hon är din svägerska.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
Du skall icke blotta dine sonahustrus blygd; ty hon är dins sons hustru, derföre skall du icke blotta hennes blygd.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
Du skall icke blotta dins broders hustrus blygd; ty hon är dins broders blygd.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
Du skall icke blotta dine hustrus, samt med hennes dotters blygd; ej heller taga hennes sons dotter, eller dotterdotter, till att blotta hennes blygd; ty hon är hennes nästa blodsfränka; och det är en last.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
Du skall ock icke taga dine hustrus syster, till att blotta hennes blygd, henne emot, medan hon ännu lefver.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
Du skall icke gå in till qvinnona, så länge hon hafver sina sjuko i sine orenhet, till att blotta hennes blygd.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
Du skall ock icke ligga när dins nästas hustru, till att beblanda dig med henne, dermed du orenar dig på henne.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
Du skall ock icke gifva af dine säd, att det skall uppbrännas för Molech, att du icke ohelgar dins Guds Namn; ty jag är Herren.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
Du skall icke ligga när dränger, såsom när ena qvinno; ty det är en styggelse.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
Du skall ock icke ligga när något djur, att du dermed orenar dig; och ingen qvinna skall skaffa hafva med något djur; ty det är en styggelse.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
I skolen uti intet af detta orena eder; förty uti allt detta hafva Hedningarna orenat sig, hvilka jag skall här utdrifva för eder.
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
Och landet är derigenom orenadt; och jag skall söka deras missgerningar på dem, så att landet skall utspy sina inbyggare.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Derföre håller mina stadgar och rätter, och görer intet af denna styggelsen, antingen inländske eller utländske ibland eder;
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
Ty all sådana styggelse hafva landsens folk gjort, som för eder voro, och hafva orenat landet;
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
På det att landet ock icke utspyr eder, då I det orenen, lika som det hafver utspytt Hedningarna, som för eder voro.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Förty de som göra denna styggelsen, deras själar skola utrotade varda utu deras folk.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Derföre håller mina stadgar, att I icke gören efter de styggeliga seder, som för eder voro, att I icke dermed orenade varden; ty jag är Herren edar Gud.

< Levitiko 18 >