< Levitiko 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Jahve reče Mojsiju:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
“Govori Aronu, njegovim sinovima i svima Izraelcima te im reci: 'Evo što je zapovjedio Jahve:
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
svaki onaj od Izraelova doma koji u taboru ili izvan tabora zakolje vola, ili ovcu, ili kozu,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
a ne donese ih na ulaz u Šator sastanka da se prinesu na dar Jahvi pred njegovim Prebivalištem, svaki takav neka je odgovoran: prolio je krv i neka se odstrani iz svoga naroda.'
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
Zato neka Izraelci svoje žrtve koje bi htjeli klati vani u polju dovedu na ulaz u Šator sastanka, k svećeniku, i neka ih prinose kao žrtve pričesnice.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
Neka svećenik izlije krv po Jahvinu žrtveniku koji se nalazi na ulazu u Šator sastanka, a loj spali na ugodan miris Jahvi,
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
tako da ubuduće ne prinose svojih žrtava klanica jarcima s kojima se odaju bludu. Neka je ovo trajan zakon za njih i njihove naraštaje.
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
I kaži im: 'Svaki pojedinac od Izraelova doma, ili stranac koji među vama boravi, koji prinese paljenicu ili klanicu
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
a ne donese je na ulaz u Šator sastanka da se prinese Jahvi, taj neka se odstrani iz svoga naroda.'”
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
“Nadalje, protiv svakoga pojedinca od Izraelova doma, a tako i protiv svakoga pridošlice među vama koji bi blagovao bilo kakvu krv, ja ću se okrenuti, svakoga tko blaguje krv odstranit ću iz njegova naroda.
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
Jer je život živoga bića u krvi. Tu krv ja sam vama dao da na žrtveniku njome obavljate obred pomirenja za svoje živote. Jer krv je ono što ispašta za život.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Zato sam kazao Izraelcima: neka nitko od vas ne jede krvi; neka ni stranac koji među vama bude ne jede krvi.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
Tko god, Izraelac ili stranac koji među vama boravi, uhvati u lovu kakvu zvijer ili pticu što se može jesti neka joj prolije krv i zatrpa zemljom.
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Jer život svakoga živog bića jest njegova krv. Zato sam i rekao Izraelcima: ne smijete jesti krvi ni od kakva živog bića, jer život svakoga živog bića jest njegova krv. Tko god je bude jeo, neka se odstrani.
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
Tko bi god, Izraelac ili stranac, jeo što je uginulo ili što su zvijeri rastrgale neka opere svoju odjeću, u vodi se okupa i ostane nečistim do večeri. Tada će postati čist.
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
Ali ako je ne opere i ne okupa svoga tijela, neka snosi posljedice svoje krivnje.”

< Levitiko 17 >