< Levitiko 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
I reèe Gospod Mojsiju i Aronu govoreæi im:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
Kažite sinovima Izrailjevim i recite: ovo su životinje koje æete jesti izmeðu svijeh životinja na zemlji:
3 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Što god ima papke i papci su mu razdvojeni i preživa izmeðu životinja, to jedite.
4 “‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Ali onijeh što samo preživaju ili što samo imaju papke razdvojene, ne jedite, kao što je kamila, jer preživa ali nema papaka razdvojenih; da vam je neèista;
5 Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
I pitomi zec, jer preživa ali nema papaka razdvojenih; neèist da vam je;
6 Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
I zec divlji, jer preživa ali nema papaka razdvojenih; neèist da vam je;
7 Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
I svinja, jer ima papke razdvojene ali ne preživa; neèista da vam je;
8 Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
Mesa od njih ne jedite niti se strva njihova dodijevajte; jer vam je neèisto.
9 “‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
A izmeðu svega što je u vodi ovo jedite: što god ima pera i ljusku u vodi, po moru i po rijekama, jedite.
10 Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
A što nema pera i ljuske u moru i u rijekama izmeðu svega što se mièe po vodi i živi u vodi, da vam je gadno.
11 Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
Gadno da vam je; mesa da im ne jedete, i na strv njihov da se gadite.
12 Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
Što god nema pera i ljuske u vodi, to da vam je gadno.
13 “‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
A izmeðu ptica ove da su vam gadne i da ih ne jedete: orao i jastrijeb i morski orao,
14 nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
Eja i kraguj po svojim vrstama,
15 akhungubwi a mitundu yonse,
I svaki gavran po svojim vrstama,
16 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
I sovuljaga i æuk i liska i kobac po svojim vrstama,
17 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
I buljina i gnjurac i ušara,
18 tsekwe, vuwo, dembo,
I labud i gem i svraka,
19 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
I roda i èaplja po svojim vrstama, i pupavac i ljiljak.
20 “‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
Što god gamiže a ima krila i ide na èetiri noge, da vam je gadno.
21 Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
Ali izmeðu svega što gamiže a ima krila i ide na èetiri noge jedite što ima stegna na nogama svojim, kojima skaèe po zemlji.
22 Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
Izmeðu njih jedite ove: arba po vrstama njegovim, salema po vrstama njegovim, argola po vrstama njegovim i agava po vrstama njegovim.
23 Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
A što još gamiže a ima krila i èetiri noge, da vam je gadno.
24 “‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
I o njih æete se oskvrniti; ko se god dotakne mrtva tijela njihova, da je neèist do veèera.
25 Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
I ko bi god nosio mrtva tijela njihova, neka opere haljine svoje, i da je neèist do veèera.
26 “‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
Svaka životinja koja ima papke ali nerazdvojene i ne preživa, da vam je neèista; ko ih se god dotakne, da je neèist.
27 Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
I što god ide na šapama izmeðu svijeh životinja èetvoronogih, da vam je neèisto; ko bi se dotakao strva njihova, da je neèist do veèera.
28 Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
I ko bi nosio strv njihov, neka opere haljine svoje, i da je neèist do veèera; to da vam je neèisto.
29 “‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
I izmeðu životinja koje pužu po zemlji da su vam neèiste: lasica i miš i kornjaèa po svojim vrstama,
30 gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
I jež i gušter i tvor i puž i krtica.
31 Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
To vam je neèisto izmeðu životinja koje pužu; ko ih se dotakne mrtvijeh, da je neèist do veèera.
32 Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
I svaka stvar na koju padne koje od njih mrtvo biæe neèista, bila sprava drvena ili haljina ili koža ili torba, i svaka stvar koja treba za kakav posao, neka se metne u vodu, i da je neèista do veèera, poslije da je èista.
33 Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
A svaki sud zemljani, u koji padne što od toga, i što god u njemu bude, biæe neèist, i razbijte ga.
34 Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
I svako jelo što se jede, ako na njega doðe onaka voda, da je neèisto, i svako piæe što se pije u svakom takom sudu, da je neèisto.
35 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
I na što bi palo što od tijela njihova mrtva sve da je neèisto, i peæ i ognjište neka se razvali, jer je neèisto i neka vam je neèisto.
36 Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
A studenac i ubao, gdje se voda skuplja, biæe èist; ali što se dotakne strva njihova, biæe neèisto.
37 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
Ako li što od strva njihova padne na sjeme, koje se sije, ono æe biti èisto.
38 Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
Ali ako bude polito sjeme vodom, pa onda padne što od strva njihova na sjeme, da vam je neèisto.
39 “‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
I kad ugine životinja od onijeh koje jedete, ko se dotakne strva njezina, da je neèist do veèera.
40 Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
A ko bi jeo od strva njezina, neka opere haljine svoje i da je neèist do veèera; i ko bi odnio strv njezin, neka opere haljine svoje, i da je neèist do veèera.
41 “‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
I sve što puže po zemlji, da vam je gadno, da se ne jede.
42 Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
Što god ide na trbuhu i što god ide na èetiri noge ili ima više noga izmeðu svega što puže po zemlji, to ne jedite, jer je gad.
43 Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
Nemojte se poganiti nièim što gamiže i nemojte se skvrniti njima, da ne budete neèisti s njih.
44 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
Jer ja sam Gospod Bog vaš; zato se osveæujte i budite sveti, jer sam ja svet; i nemojte se skvrniti nièim što puže po zemlji.
45 Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
Jer ja sam Gospod, koji sam vas izveo iz zemlje Misirske da vam budem Bog; budite dakle sveti, jer sam ja svet.
46 “‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
Ovo je zakon za zvijeri i za ptice, i za sve životinje što se mièu po vodi, i za svaku dušu živu koja puže po zemlji,
47 Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”
Da se raspoznaje neèisto od èistoga i životinja koja se jede od životinje koja se ne jede.

< Levitiko 11 >