< Levitiko 10 >

1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
And Nadab and Abihu, the sons of Aaron, each of them took his censer, and put fire in it, and laid incense on it, and offered strange fire before Jehovah, which he had not commanded them.
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
And there came forth fire from before Jehovah, and devoured them, and they died before Jehovah.
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
Then Moses said to Aaron, This is it that Jehovah spoke, saying, I will be sanctified in those who come near me. And I will be glorified before all the people. And Aaron remained silent.
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
And Moses called Mishael and Elzaphan, the sons of Uzziel the uncle of Aaron, and said to them, Draw near. Carry your brothers from before the sanctuary out of the camp.
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
So they drew near, and carried them in their tunics out of the camp, as Moses had said.
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
And Moses said to Aaron, and to Eleazar and to Ithamar, his sons, Let not the hair of your heads go loose, neither tear your clothes, that ye not die, and that he not be angry with all the congregation, but let your brothers, the whole house of Israel, bewail the burning which Jehovah has kindled.
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
And ye shall not go out from the door of the tent of meeting, lest ye die, for the anointing oil of Jehovah is upon you. And they did according to the word of Moses.
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
And Jehovah spoke to Aaron, saying,
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
Drink no wine nor strong drink, thou, nor thy sons with thee, when ye go into the tent of meeting, that ye not die-it shall be a statute forever throughout your generations-
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
and that ye may make a distinction between the holy and the common, and between the unclean and the clean,
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
and that ye may teach the sons of Israel all the statutes which Jehovah has spoken to them by Moses.
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
And Moses spoke to Aaron, and to Eleazar and to Ithamar, his sons who were left, Take the meal offering that remains of the offerings of Jehovah made by fire, and eat it without leaven beside the altar, for it is most holy.
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
And ye shall eat it in a holy place, because it is thy portion, and thy sons' portion, of the offerings of Jehovah made by fire. For so I am commanded.
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
And ye shall eat the wave-breast and the heave-thigh in a clean place, thou, and thy sons, and thy daughters with thee. For they are given as thy portion, and thy sons' portion, out of the sacrifices of the peace offerings of the sons of Israel.
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
They shall bring the heave-thigh and the wave-breast with the offerings made by fire of the fat, to wave it for a wave offering before Jehovah, and it shall be thine, and thy sons' with thee, as a portion forever, as Jehovah has commanded.
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
And Moses diligently sought the goat of the sin offering, and, behold, it was burnt. And he was angry with Eleazar and with Ithamar, the sons of Aaron who were left, saying,
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
Why have ye not eaten the sin offering in the place of the sanctuary, seeing it is most holy, and he has given it to you to bear the iniquity of the congregation, to make atonement for them before Jehovah?
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
Behold, the blood of it was not brought into the sanctuary inside. Ye should certainly have eaten it in the sanctuary, as I commanded.
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
And Aaron spoke to Moses, Behold, this day they have offered their sin offering and their burnt offering before Jehovah, and there have befallen me such things as these. And if I had eaten the sin offering today, would it have been well-pleasing in the sight of Jehovah?
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
And when Moses heard, it was well-pleasing in his sight.

< Levitiko 10 >