< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
I viknu Gospod Mojsija, i reèe mu iz šatora od sastanka govoreæi:
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Kaži sinovima Izrailjevim, i reci im: kad ko izmeðu vas hoæe da prinese Gospodu žrtvu od stoke, prinesite žrtvu svoju od goveda ili od ovaca ili od koza.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
Ako mu je žrtva paljenica od goveda, neka prinese muško, zdravo; na vratima šatora od sastanka neka je prinese drage volje pred Gospodom.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
I neka metne ruku svoju na glavu žrtvi paljenici, i primiæe mu se, i oèistiæe ga od grijeha.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
I neka zakolje tele pred Gospodom, i neka sinovi Aronovi sveštenici prinesu krv, i pokrope krvlju oltar ozgo unaokolo, koji je pred vratima šatora od sastanka.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
Potom neka se odre žrtva paljenica i rasijeèe na dijelove.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
I sinovi Aronovi sveštenici neka nalože oganj na oltaru, i metnu drva na oganj.
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
Pa onda sinovi Aronovi sveštenici neka namjeste dijelove, glavu i salo na drva na ognju, koji je na oltaru.
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
A crijeva i noge neka se operu vodom; i sveštenik neka zapali sve to na oltaru; to je žrtva paljenica, žrtva ognjena na ugodni miris Gospodu.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
Ako li bi htio prinijeti žrtvu paljenicu od sitne stoke, od ovaca ili od koza, neka prinese muško, zdravo.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
I neka se zakolje na sjevernoj strani oltara pred Gospodom, i sinovi Aronovi sveštenici neka pokrope krvlju oltar ozgo unaokolo.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
I neka se rasijeèe na dijelove s glavom i sa salom, i sveštenik neka to namjesti na drva na ognju, koji je na oltaru.
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
A crijeva i noge neka se operu vodom; i sveštenik neka prinese sve to i zapali na oltaru; to je žrtva paljenica, žrtva ognjena na ugodni miris Gospodu.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
Ako li hoæe da prinese pticu Gospodu na žrtvu paljenicu, neka prinese žrtvu od grlica ili od golubiæa.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
I sveštenik neka je metne na oltar, i glavu neka joj zasijeèe noktom, i zapali na oltaru iscijedivši joj krv niz oltar sa strane.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
I neka joj izvadi volju s neèistotom i baci kraj oltara prema istoku gdje je pepeo.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
I neka je zadre za krila, ali da ne raskine; tako neka je sveštenik zapali na oltaru na drvima koja su na ognju; to je žrtva paljenica, žrtva ognjena na ugodni miris Gospodu.

< Levitiko 1 >