< Oweruza 9 >

1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
Tedy odszedł Abimelech, syn Jerobaalów, do Sychem, do braci matki swojej, i mówił do nich, i do wszystkiego narodu domu ojca matki swej, a rzekł:
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
Mówcie proszę, gdzieby słyszeli wszyscy przełożeni Sychem: Co wam lepszego, aby nad wami panowało siedmdziesiąt mężów, wszyscy synowie Jerobaalowi, czyli żeby panował nad wami mąż jeden? Wżdy pamiętajcie, żem ja kość wasza, i ciało wasze.
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
Tedy mówili bracia matki jego o nim, gdzie słyszeli wszyscy przełożeni Sychem, wszystkie te słowa, i nakłoniło się serce ich za Abimelechem, bo rzekli: Brat nasz jest.
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
I dali mu siedmdziesiąt srebrników z domu Baalberyt, i naprzyjmował za nie Abimelech ludzi lekkomyślnych, i tułaczów, którzy chodzili za nim.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
I przyszedł w dom ojca swego do Efra, i pobił bracią swą, syny Jerobaalowe, siedmdziesiąt mężów na jednym kamieniu; tylko został Jotam, syn Jerobaalów, najmniejszy, iż się był skrył.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
I zebrali się wszyscy mężowie Sychem, i wszystek dom Mello, a szedłszy obrali Abimelecha królem na równinie, kędy stał słup w Sychem.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
Co gdy powiedziano Jotamowi, szedłszy stanął na wierzchu góry Garyzym, a podniósłszy głos swój wołał, i rzekł im: Posłuchajcie mię mężowie Sychem, a was też Bóg usłyszy.
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
Zeszły się drzewa, aby pomazały nad sobą króla, i rzekły do oliwnego drzewa: Króluj nad nami.
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
Którym odpowiedziało oliwne drzewo: Izali opuszczę tłustość moję, przez którą uczczony bywa Bóg i ludzie, a pójdę, abym wystawione było nad drzewy?
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
Rzekły potem drzewa do figowego drzewa: Pójdź ty, króluj nad nami.
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
Którym odpowiedziało figowe drzewo: Izali opuszczę słodkość moję, i owoc mój wyborny, a pójdę, abym wystawione było nad drzewy?
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
Potem rzekły drzewa do macicy winnej: Pójdź ty, króluj nad nami.
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
Tedy im odpowiedziała macica: Izali opuszczę moszcz mój, który uwesela Boga i ludzie, a pójdę, abym wystawiona była nad drzewy?
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
I rzekły wszystkie drzewa do ostu: Pójdź ty, króluj nad nami.
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
Tedy odpowiedział oset drzewom: jeźli wy prawdziwie chcecie pomazać mię za króla nad sobą, pójdźcież, a odpoczywajcie pod cieniem moim, a jeźliż nie, niech wynijdzie ogień z ostu, a spali Cedry Libańskie.
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
A tak teraz jeźliście prawdziwie a szczerze uczynili, obrawszy sobie królem Abimelecha; a jeźliście się dobrze obeszli z Jerobaalem i z domem jego, a jeźliście podług dobrodziejstw ręki jego uczynili z nim;
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
(Albowiem walczył ojciec mój za was, i podał duszę swą w niebezpieczeństwo, aby was wyrwał z ręki Madyjańczyków;
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
Aleście wy powstali przeciw domowi ojca mego dziś, i pobiliście syny jego, siedmdziesiąt mężów na jednym kamieniu, i obraliście królem Abimelecha, syna służebnicy jego, nad mężami Sychem, iż bratem waszym jest.)
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
Jeźliście prawdziwie a szczerze obeszli się z Jerobaalem, i z domem jego dnia tego, weselcież się z Abimelecha, a on niech się też weseli z was.
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
Ale jeźliż nie, niechajże wynijdzie ogień z Abimelecha, a pożre męże Sychem, i dom Mello; niechajże też wynijdzie ogień od mężów Sychem, i z domu Mello, a pożre Abimelecha.
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
Tedy uciekł Jotam, a uciekłszy poszedł do Beer, i mieszkał tam, bojąc się Abimelecha, brata swego.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
A tak panował Abimelech nad Izraelem przez trzy lata.
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
I posłał Bóg ducha złego między Abimelecha i między męże Sychemskie, a złamali wiarę mężowie Sychem Abimelechowi;
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
Aby się zemszczono krzywdy siedemdziesięciu synów Jerobaalowych, aby krew ich przyszła na Abimelecha, brata ich, który je pobił, i na męże Sychemskie, którzy zmocnili ręce jego, aby pobił bracią swoję.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
I zasadzili się nań mężowie Sychemscy na wierzchu gór, a rozbijali każdego, który jedno szedł tamtą drogą. I powiedziano to Abimelechowi.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
Nadto przyszedł Gaal, syn Obedów, i bracia jego, i przyszedł do Sychem, a poufali mu mężowie Sychem.
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
A wyszedłszy na pola zbierali wina swoje, i tłoczyli, weseląc się; a wszedłszy w dom bogów swoich, jedli i pili, a złorzeczyli Abimelechowi.
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
Tedy rzekł Gaal, syn Obedów: Cóż jest Abimelech? i co jest Sychem, żebyśmy mu służyli? azaż nie jest syn Jerobaalów, a Zebul urzędnikiem jego? raczej służcie mężom Hemora, ojca Sychemowego; bo czemuż byśmy onemu służyć mieli?
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
O by kto podał ten lud w ręce moje, aby sprzątnął Abimelecha! I rzekł Abimelechowi: Zbierz swoje wojsko, a wynijdź.
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
A usłyszawszy Zebul, przełożony miasta onego, słowa Gaala, syna Obedowego, zapalił się gniew jego.
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
I wyprawił posły do Abimelecha potajemnie, mówiąc: Oto Gaal, syn Obedów, i bracia jego przyszli do Sychem, a oto chcą walczyć z miastem przeciwko tobie.
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
A tak teraz wstań nocą, ty i lud, który jest z tobą, a uczyń zasadzkę w polu.
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
A rano, gdy słońce wznijdzie, wstawszy uderzysz na miasto; a gdy on i lud, który jest z nim, wynijdzie przeciw tobie, uczynisz z nim, co będzie chciała ręka twoja.
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
Tedy wstawszy Abimelech, i wszystek lud, który z nim był, w nocy, zasadzili się przeciw Sychem na czterech miejscach.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
A wyszedłszy Gaal, syn Obedów, stanął w samej bramie miasta; wstał też i Abimelech, i lud, który z nim był, z zasadzki.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
A widząc Gaal lud, rzekł do Zebula: Oto, lud idzie z wierzchu gór. Któremu odpowiedział Zebul: Cień góry ty widzisz, jakoby ludzie.
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
Tedy po wtóre rzekł Gaal, mówiąc: Oto, lud zstępuje z góry a jeden huf idzie drogą równiny Meonenim.
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
Tedy rzekł do niego Zebul: Gdzież teraz usta twoje, które mówiły: Co jest Abimelech, abyśmy mu służyć mieli? izali to nie ten lud, któryś wzgardził? wnijdź teraz, a walcz przeciw niemu.
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
A tak wyszedł Gaal przed mężami Sychem, a walczył przeciw Abimelechowi.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
I gonił go Abimelech, gdy przed nim uciekał, a poległo wiele rannych aż do samej bramy.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
I został Abimelech w Aruma; a Zebul wygnał Gaala z bracią jego, aby nie mieszkali w Sychem.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
Ale nazajutrz wyszedł lud w pole, i powiedziano to Abimelechowi.
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
Wziąwszy tedy lud, rozdzielił go na trzy hufce, i zasadził się w polu; a widząc, a oto lud wychodził z miasta, wypadł na nie, i pobił je.
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
Bo Abimelech i hufy, które z nim były, uderzyły na nie, i stanęli u samej bramy miasta, a inne dwa hufy uderzyły na wszystkie, którzy byli w polu, i pobili je.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
A Abimelech dobywał miasta przez on wszystek dzień, i wziął je; a lud, który w niem był, pomordował, a zburzywszy miasto, posiał je solą.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
A usłyszawszy wszyscy mężowie, którzy byli na wieży Sychem, przyszli do twierdzy domu boga Beryt.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
I opowiedziano Abimelechowi, że się tam zgromadzili wszyscy mężowie wieży Sychem.
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
Tedy szedł Abimelech na górę Salmon, on i wszystek lud, który był z nim; a nabrawszy z sobą siekier, uciął gałąź z drzewa, a wziąwszy ją, włożył na ramiona swoje, i rzekł do ludu, który z nim był: Co widzicie, żem uczynił, prędko czyńcie tak, jak o ja.
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
A tak uciąwszy z onego wszystkiego ludu każdy gałąź swoję, szli za Abimelechem, a kładli je około twierdzy i spalili niemi twierdzą ogniem, i poginęło tam wszystkich mężów wieży Sychemskiej około tysiąca mężów i niewiast.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
Potem szedł Abimelech do Tebes, a położywszy się przeciwko Tebes, dobył go.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
Ale wieża była mocna w pośrodku miasta, na którą uciekli wszyscy mężowie, i niewiasty, i wszyscy przedniejsi miasta, a zamknąwszy ją za sobą, weszli na dach wieży.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
Tedy przyszedł Abimelech aż do samej wieży, i dobywał jej, a stanąwszy u samych drzwi wieży, chciał ją spalić ogniem.
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
Między tem zrzuciła niewiasta niektóra sztukę kamienia od żarn na głowę Abimelechowę, i rozbiła wierzch głowy jego.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
Który natychmiast zawoławszy pacholika, co nosił broń jego, rzekł do niego: Dobądź miecza twego, a zabij mię, by snać nie rzeczono o mnie: Niewiasta go zabiła: a tak przebił go pacholik jego, i umarł.
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
A widząc mężowie Izraelscy, iż umarł Abimelech, rozeszli się każdy do miejsca swego.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
I oddał Bóg ono złe Abimelechowi, które uczynił nad ojcem swoim, zabiwszy siedmdziesiąt braci swych.
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
I wszystko złe mężów Sychem obrócił Bóg na głowę ich; a przyszło na nie przeklęstwo Jotama, syna Jerobaalowego.

< Oweruza 9 >