< Oweruza 20 >

1 Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Then all the people of Israel came out as one man, from Dan to Beersheba, including the land of Gilead also, and they assembled together before Yahweh at Mizpah.
2 Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
The leaders of all the people, of all the tribes of Israel, took their places in the assembly of the people of God—400,000 men on foot, who were ready to fight with the sword.
3 Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
Now the people of Benjamin heard that the people of Israel had gone up to Mizpah. The people of Israel said, “Tell us how this wicked thing happened.”
4 Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
The Levite, the husband of the woman who had been murdered, answered, “I came to Gibeah in the territory that belongs to Benjamin, I and my concubine, to spend the night.
5 Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
During the night, the leaders of Gibeah attacked me, surrounding the house, intending to kill me. They raped my concubine, and she died.
6 Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
I took my concubine and cut her body into pieces, and sent them into each region of Israel's inheritance, because they have committed such wickedness and outrage in Israel.
7 Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
Now, all you Israelites, give your advice and counsel here.”
8 Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
All the people arose together as one man, and they said, “None of us will go to his tent, and none of us will return to his house!
9 Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
But now this is what we must do to Gibeah: We will attack it as the lot directs us.
10 Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
We will take ten men of a hundred throughout all the tribes of Israel, and one hundred of a thousand, and one thousand of ten thousand, to get provisions for these people, so that when they come to Gibeah in Benjamin, they may punish them for the wickedness they committed in Israel.”
11 Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
So all the soldiers of Israel assembled against the city, as one man.
12 Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
The tribes of Israel sent men through all the tribe of Benjamin, saying, “What is this wickedness that was done among you?
13 Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
Therefore, give us those wicked men of Gibeah, so we may put them to death, and so we will completely remove this evil from Israel.” But the Benjamites would not listen to the voice of their brothers, the people of Israel.
14 Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
Then the people of Benjamin came together out of the cities to Gibeah to get ready to fight against the people of Israel.
15 Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
The people of Benjamin brought together from their cities to fight on that day twenty-six thousand soldiers who were trained to fight with the sword. In addition, there were seven hundred of their chosen men from the inhabitants of Gibeah.
16 Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
Among all these soldiers were seven hundred chosen men who were left-handed. Each of them could sling a stone at a hair and not miss.
17 Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
The people of Israel, not counting the number from Benjamin, numbered 400,000 men, who were trained to fight with the sword. All of these were men of war.
18 Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
The people of Israel arose, went up to Bethel, and asked for advice from God. They asked, “Who first will attack the people of Benjamin for us?” Yahweh said, “Judah will attack first.”
19 Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
The people of Israel got up in the morning and they moved their camp near Gibeah.
20 Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
The people of Israel went out to fight against Benjamin. They set up their battle positions against them at Gibeah.
21 A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
The people of Benjamin came out of Gibeah, and they killed twenty-two thousand men of the army of Israel on that day.
22 Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
But the people of Israel strengthened themselves and they formed the battle line in the same place where they had taken positions on the first day.
23 Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
Then the people of Israel went up and they wept before Yahweh until evening, and they sought direction from Yahweh. They said, “Should we go again to fight against our brothers, the people of Benjamin?” Yahweh said, “Attack them!”
24 Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
So the people of Israel went against the soldiers of Benjamin the second day.
25 Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
On the second day, Benjamin went out against them from Gibeah and they killed eighteen thousand men from the people of Israel. All were men who trained to fight with the sword.
26 Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
Then all the soldiers of Israel and all the people went up to Bethel and wept, and there they sat before Yahweh and they fasted that day until the evening and offered burnt offerings and peace offerings before Yahweh.
27 Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
The people of Israel asked Yahweh—for the ark of the covenant of God was there in those days,
28 Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
and Phinehas, son of Eleazar son of Aaron, was serving before the ark in those days—”Should we go out to battle once more against the people of Benjamin, our brothers, or stop?” Yahweh said, “Attack, for tomorrow I will help you defeat them.”
29 Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
So Israel set men in secret places around Gibeah.
30 Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
The people of Israel fought against the people of Benjamin for the third day, and they formed their battle lines against Gibeah as they had done before.
31 Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
The people of Benjamin went and fought against the people, and they were drawn away from the city. They began to kill some of the people. There were about thirty men of Israel who died in the fields and on the roads. One of the roads went up to Bethel, and the other went to Gibeah.
32 Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
Then the people of Benjamin said, “They are defeated and they are running away from us, just as at first.” But the soldiers of Israel said, “Let us run back and draw them away from the city to the roads.”
33 Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
All the people of Israel rose up out of their places and formed themselves into lines for battle at Baal Tamar. Then the soldiers of Israel who had been hiding in secret places ran out from their places from Maareh Gibeah.
34 Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
There came out against Gibeah ten thousand chosen men out of all Israel, and the fighting was fierce, but the Benjamites did not know that disaster was close to them.
35 Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
Yahweh defeated Benjamin before Israel. On that day, the soldiers of Israel killed 25,100 men of Benjamin. All these who died were those who had been trained to fight with the sword.
36 Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
So the soldiers of Benjamin saw they were defeated. The men of Israel had given ground to Benjamin, because they were counting on the men they had placed in hidden positions outside Gibeah.
37 Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
Then the men who were hiding got up and hurried and they rushed into Gibeah, and they struck all the city with the edge of the sword.
38 Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
The arranged signal between the soldiers of Israel and the men hiding in secret would be that a great cloud of smoke would rise up out of the city.
39 ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
When the signal was sent the soldiers of Israel would turn from the battle. Now Benjamin began to attack and they killed about thirty men of Israel, and they said, “It is sure that they are defeated before us, as in the first battle.”
40 Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
But when a pillar of smoke began to rise up out of the city, the Benjamites turned and saw the smoke rising to the sky from the whole city.
41 Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
Then the people of Israel turned against them. The men of Benjamin were terrified, for they saw that disaster had come on them.
42 Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
So they ran away from the people of Israel, escaping on the way to the wilderness. But the fighting overtook them. The soldiers of Israel came out of the cities and killed them where they stood.
43 Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
They surrounded the Benjamites, chased them and trampled them down at Nohah, all the way to the east side of Gibeah.
44 Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
From the tribe of Benjamin, eighteen thousand people died, all of them men who were distinguished in battle.
45 Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
They turned and fled toward the wilderness to the rock of Rimmon. The Israelites killed five thousand more of them along the roads. They kept going after them, following them closely all the way to Gidom, and there they killed two thousand more.
46 Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
All the soldiers of Benjamin who fell that day were twenty-five thousand—men who were trained to fight with the sword; all of them were distinguished in battle.
47 Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
But six hundred men turned and fled to the wilderness, toward the rock of Rimmon. For four months they stayed at the rock of Rimmon.
48 Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.
The soldiers of Israel turned back against the people of Benjamin and struck them with the edge of the sword, the city, including the animals and everything that they found. They also burned down every town in their path.

< Oweruza 20 >